< 1 Mbiri 18 >

1 Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
A poslije toga pobi David Filisteje i pokori ih, i uze Gat i sela njegova iz ruku Filistejskih.
2 Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
Pobi i Moavce, i postaše Moavci sluge Davidove i plaæahu mu danak.
3 Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
Razbi David i Adar-Ezera cara Sovskoga u Ematu izašav da raširi vlast svoju do rijeke Efrata.
4 Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
I uze mu David tisuæu kola i sedam tisuæa konjika i dvadeset tisuæa pješaka, i podreza David žile svijem konjma kolskim, samo ostavi za sto kola.
5 Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
A bijahu došli Sirci iz Damaska u pomoæ Adar-Ezeru caru Sovskomu, i David pobi dvadeset i dvije tisuæe Siraca.
6 Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
I namjesti David vojsku u Siriji što je pod Damaskom, i Sirci postaše sluge Davidove plaæajuæi mu danak. I Gospod èuvaše Davida kuda god iðaše.
7 Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
I David uze zlatne štitove koje imahu sluge Adar-Ezerove, i donese ih u Jerusalim.
8 Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
I iz Tivata i iz Huna gradova Adar-Ezerovijeh odnese David silnu mjed, od koje Solomun naèini more mjedeno i stupove i posuðe mjedeno.
9 Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
A kad èu Toja car Ematski da je David pobio svu vojsku Adar-Ezera cara Sovskoga,
10 anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
Posla Adorama sina svojega k caru Davidu da ga pozdravi i da mu èestita što je vojevao na Adar-Ezera i ubio ga, jer Toja imaše rat s Adar-Ezerom, i svakojakih zaklada zlatnijeh i srebrnijeh i mjedenijeh.
11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
Pa i to car David posveti Gospodu sa srebrom i zlatom što bješe uzeo od svijeh naroda, od Edomaca i od Moavaca i od sinova Amonovijeh i od Filisteja i od Amalika.
12 Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
I Avisaj sin Serujin pobi osamnaest tisuæa Idumejaca u slanoj dolini.
13 Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
I namjesti vojsku po Idumeji, i svi Idumejci postaše sluge Davidove. I Gospod èuvaše Davida kuda god iðaše.
14 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
Tako carova David nad svijem Izrailjem sudeæi i dajuæi pravdu svemu narodu svojemu.
15 Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
I Joav sin Serujin bješe nad vojskom, a Josafat sin Ahiludov pametar,
16 Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
A Sadok sin Ahitovov i Avimeleh sin Avijatarov sveštenici, a Susa pisar,
17 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.
A Venaja sin Jodajev bješe nad Heretejima i Feletejima, a sinovi Davidovi prvi do cara.

< 1 Mbiri 18 >