< 1 Mbiri 16 >

1 Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
I kad donesoše kovèeg Božji, namjestiše ga usred šatora, koji mu razape David; i prinesoše žrtve paljenice i žrtve zahvalne pred Bogom.
2 Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
Potom prinesavši David žrtve paljenice i žrtve zahvalne, blagoslovi narod u ime Gospodnje.
3 Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
I razdade svijem Izrailjcima, i ljudima i ženama, svakom po jedan hljeb i komad mesa i vrè vina.
4 Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
Potom postavi pred kovèegom Gospodnjim sluge izmeðu Levita da pominju i slave i hvale Gospoda Boga Izrailjeva:
5 Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
Asafa poglavara, a drugoga za njim Zahariju, i Jeila i Semiramota i Jehila i Matatiju i Elijava i Venaju i Ovid-Edoma; i Jeilo udaraše u psaltire i gusle, a Asaf u kimvale,
6 ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
A Venaja i Jazilo sveštenici bijahu jednako s trubama pred kovèegom zavjeta Gospodnjega.
7 Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
U taj dan naredi David prvi put da hvale Gospoda Asaf i braæa njegova:
8 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
Hvalite Gospoda; glasite ime njegovo; javljajte po narodima djela njegova.
9 Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
Pjevajte mu, slavite ga, kazujte sva èudesa njegova.
10 Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
Hvalite se svetijem imenom njegovijem; neka se veseli srce onijeh koji traže Gospoda.
11 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
Tražite Gospoda i silu njegovu; tražite lice njegovo bez prestanka.
12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
Pamtite èudesa njegova, koja je uèinio, znake njegove i sudove usta njegovijeh.
13 inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
Sjeme Izrailjevo sluge su njegove, sinovi Jakovljevi izbrani njegovi.
14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
On je Gospod Bog naš, po svoj su zemlji sudovi njegovi.
15 Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
Pamtite uvijek zavjet njegov, rijeè koju je dao na tisuæu koljena.
16 pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
Što je zavjetovao Avramu i za što se kleo Isaku,
17 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
To je postavio Jakovu za zakon i Izrailju za zavjet vjeèni,
18 “Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
Govoreæi: tebi æu dati zemlju Hanansku u našljedni dio.
19 Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
Tada vas još bijaše malo na broj, bijaše vas malo, i bijaste došljaci.
20 iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
Iðahu od naroda do naroda, i iz jednoga carstva k drugomu plemenu.
21 Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
Ne dade nikomu da im naudi, i karaše za njih careve:
22 “Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
Ne dirajte u pomazanike moje, i prorocima mojim ne èinite zla.
23 Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Pjevaj Gospodu, sva zemljo! javljajte od dana na dan spasenje njegovo.
24 Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
Kazujte po narodima slavu njegovu, po svijem plemenima èudesa njegova.
25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
Jer je velik Gospod i valja ga hvaliti veoma; strašniji je od svijeh bogova.
26 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
Jer su svi bogovi u naroda ništa; a Gospod je nebesa stvorio.
27 Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
Slava je i velièanstvo pred njim, sila i radost u stanu njegovu.
28 Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
Dajte Gospodu, plemena narodna, dajte Gospodu slavu i èast.
29 perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
Dajte Gospodu slavu prema imenu njegovu, nosite dare i idite preda nj, poklonite se Gospodu u svetoj krasoti.
30 Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
Strepi pred njim, sva zemljo; zato je vasiljena tvrda i neæe se pomjestiti.
31 Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
Nek se vesele nebesa i zemlja se raduje; i neka govore po narodima: Gospod caruje.
32 Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
Neka pljeska more i što je u njemu; neka skaèe polje i sve što je na njemu.
33 Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
Tada neka se raduju drveta šumska pred Gospodom, jer ide da sudi zemlji.
34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
Hvalite Gospoda, jer je dobar, jer je dovijeka milost njegova.
35 Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
I recite: spasi nas, Bože spasenja našega, i skupi nas i izbavi nas od naroda da slavimo sveto ime tvoje, da se hvalimo tvojom slavom.
36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
Blagosloven Gospod Bog Izrailjev od vijeka i do vijeka. Tada sav narod reèe: amin; i hvališe Gospoda.
37 Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
I ostavi ondje pred kovèegom zavjeta Gospodnjega Asafa i braæu njegovu da služe pred kovèegom bez prestanka kao što treba od dana na dan,
38 Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
I Ovid-Edoma i braæu njegovu, šezdeset i osam, Ovid-Edoma sina Jedutunova i Osu, da budu vratari;
39 Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
A Sadoka sveštenika i braæu njegovu sveštenike pred šatorom Gospodnjim na visini u Gavaonu,
40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
Da prinose žrtve paljenice Gospodu na oltaru za žrtve paljenice bez prestanka jutrom i veèerom, i da èine sve što je napisano u zakonu Gospodnjem što je zapovjedio Izrailju,
41 Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
I s njima Emana i Jedutuna i druge izabrane, koji biše poimence imenovani da hvale Gospoda, jer je dovijeka milost njegova,
42 Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
S njima Emana i Jedutuna, da trube u trube i udaraju u kimvale i u druge sprave muzièke Bogu; a sinove Jedutunove da budu vratari.
43 Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.
Potom se razide sav narod, svak svojoj kuæi, a David se vrati da blagoslovi dom svoj.

< 1 Mbiri 16 >