< 1 Mbiri 16 >

1 Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
A gdy przynieśli arkę Boga i umieścili ją pośrodku namiotu wzniesionego przez Dawida, złożyli całopalenia i ofiary pojednawcze przed Bogiem.
2 Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
A gdy Dawid skończył składanie całopaleń i ofiar pojednawczych, błogosławił lud w imię PANA.
3 Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
I rozdał wszystkim Izraelitom, tak mężczyźnie, jak i kobiecie, po bochenku chleba i po kawałku mięsa oraz po bukłaku [wina].
4 Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
Ustanowił też niektórych Lewitów sługami przed arką PANA, aby wspominali i chwalili [go], i dziękowali PANU, Bogu Izraela:
5 Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
Asafa, naczelnika, a po nim Zachariasza, Jejela, Szemiramota, Jechiela, Mattitiasza, Eliaba, Benajasza i Obed-Edoma: Jejela [do gry] na instrumentach: cytrach i harfach, a Asafa – na cymbałach;
6 ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
A kapłanów Benajasza i Jachaziela, aby [stali] nieustannie z trąbami przed arką przymierza Boga.
7 Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
Wtedy w tym dniu Dawid postanowił po raz pierwszy, aby Asaf i jego bracia chwalili PANA [tym psalmem]:
8 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
Wysławiajcie PANA, wzywajcie jego imienia, opowiadajcie między narodami sprawy jego.
9 Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
Śpiewajcie mu, śpiewajcie mu psalmy, rozmawiajcie o wszystkich jego cudach.
10 Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
Chlubcie się jego świętym imieniem, niech się raduje serce szukających PANA.
11 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
Szukajcie PANA i jego mocy, szukajcie zawsze jego oblicza.
12 Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
Przypominajcie sobie dzieła, które czynił, jego cuda i wyroki jego ust.
13 inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
Wy, potomkowie Izraela, jego sługi; wy, synowie Jakuba, jego wybrańcy!
14 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
On [jest] PANEM, naszym Bogiem, jego sądy na całej ziemi.
15 Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
Pamiętajcie zawsze o jego przymierzu, o słowie, które nakazał po tysiąc pokoleń;
16 pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
[O przymierzu], które zawarł z Abrahamem, i o przysiędze złożonej Izaakowi.
17 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
Ustanowił je jako prawo dla Jakuba, jako wieczne przymierze dla Izraela;
18 “Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
Mówiąc: Tobie dam ziemię Kanaan jako dział waszego dziedzictwa;
19 Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
Kiedy było was niewielu, [byliście] nieliczni i obcy w niej.
20 iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
I wędrowali od narodu do narodu, z jednego królestwa do innego ludu;
21 Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
Nikomu nie pozwolił ich krzywdzić, nawet karcił królów z ich powodu, [mówiąc];
22 “Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
Nie dotykajcie moich pomazańców, a moim prorokom nie czyńcie [nic] złego.
23 Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
Śpiewaj PANU, cała ziemio, opowiadajcie dzień po dniu o jego zbawieniu.
24 Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
Głoście wśród narodów jego chwałę, pośród wszystkich ludów – jego cudowne dzieła;
25 Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
Wielki bowiem [jest] PAN i godny wszelkiej chwały, straszliwszy nad wszystkich bogów;
26 Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
Gdyż wszyscy bogowie narodów [są] bożkami, a PAN uczynił niebiosa.
27 Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
Chwała i cześć przed nim, moc i radość w jego przybytku.
28 Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
Oddajcie PANU, rodziny narodów, oddajcie PANU chwałę i moc.
29 perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
Oddajcie PANU chwałę jego imienia. Przynoście dary i przychodźcie przed jego oblicze. Oddajcie PANU pokłon w ozdobie świętości.
30 Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
Zadrżyj przed nim, cała ziemio. Świat będzie utwierdzony, aby się nie poruszył.
31 Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
Niech się weselą niebiosa i niech się raduje ziemia, niech mówią wśród narodów: PAN króluje!
32 Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
Niech zaszumi morze i to, co je napełnia, niech radują się pola i wszystko, co [jest] na nich.
33 Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
Wtedy radośnie wykrzykną leśne drzewa przed PANEM, bo idzie, aby sądzić ziemię.
34 Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
Wysławiajcie PANA, bo jest dobry, bo jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
35 Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
I mówcie: Zbaw nas, BOŻE naszego zbawienia, i zgromadź nas, i wybaw nas od pogan, abyśmy wielbili twoje święte imię i chlubili się twoją chwałą.
36 Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
Błogosławiony PAN, Bóg Izraela, na wieki wieków. I cały lud powiedział: Amen i chwalił PANA.
37 Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
I [Dawid] zostawił tam przed arką przymierza PANA Asafa i jego braci, aby nieustannie pełnili służbę przed arką, według potrzeby każdego dnia;
38 Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
Także Obed-Edoma i ich braci, sześćdziesięciu ośmiu; a Obed-Edoma, syna Jedutuna, i Chosę [uczynił] odźwiernymi.
39 Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
Kapłana Sadoka i jego braci kapłanów [pozostawił] przed przybytkiem PANA na wyżynie w Gibeonie;
40 kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
Aby składali PANU nieustannie, rano i wieczorem, całopalenia na ołtarzu całopaleń, zgodnie ze wszystkim, co jest napisane w Prawie PANA, które nadał on Izraelowi;
41 Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
A z nimi [pozostawił] Hemana i Jedutuna oraz resztę wybranych, imiennie wyznaczonych, aby chwalili PANA, bo jego miłosierdzie [trwa] na wieki.
42 Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
I u nich, u Hemana i Jedutuna, [pozostawił] trąby i cymbały dla grających na tych i na [innych] instrumentach muzycznych dla Boga. Synowie zaś Jedutuna [byli] odźwiernymi.
43 Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.
Potem cały lud się rozszedł, każdy do swego domu. Dawid też wrócił, aby błogosławić swojemu domowi.

< 1 Mbiri 16 >