< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 9 >

1 ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᏥᏁᎦ ᎦᎶᏁᏛ ᎠᎦᏔᎲᎢ, ᎥᏝ ᏱᎦᏥᎪᎥᏍᎦ, ᎠᏆᏓᏅᏛ ᎾᏍᏉ ᎠᏉᎯᏳᏓᏁᎯ ᏂᎦᎵᏍᏗᎭ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ,
Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni.
2 ᎾᏍᎩ ᎤᏣᏘ ᎡᎯᏍᏗ ᎠᏆᏓᏅᏔᏩᏕᎬ ᎠᎴ ᏂᎪᎯᎸ ᎤᏲ ᎠᎩᏰᎸᏒ ᎠᎩᎾᏫᏱ.
Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga.
3 ᎬᏆᏚᎸᏗᏉᏰᏃ ᎠᏋᏒ ᎨᏒ ᎥᎩᏍᎦᏨᎯ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᎥᏆᏓᏓᎴᏙᏗᏱ ᎦᎶᏁᏛ ᎡᎲᎢ ᎦᏥᏍᏕᎵᏍᎬ ᎣᏣᏓᏅᏟ, ᎪᎱᏍᏗ ᏗᏋᏅ Ꭰ ᎤᏇᏓᎵ ᎨᏒᎢ;
Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga,
4 ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎵ ᏧᏁᏢᏔᏅᏛ ᏥᎩ; ᎾᏍᎩ ᎤᎾᏤᎵᎦ ᏥᎩ [ ᎤᏁᎳᏅᎯ ] ᏧᏪᏥ ᎢᎨᎬᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎧᏃᎮᏛ ᏓᏠᎯᏍᏛᎢ, ᎠᎴ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ ᎨᏥᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎠᏚᎢᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ;
anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake.
5 ᎾᏍᎩ ᏧᏂᏙᏓ ᏥᎩ ᎠᏂᎦᏴᎵᎨᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎠᏁᎲᎢ, Ꭰ ᎠᏇᏓᎵ ᎨᏒ ᏧᎷᏤ ᎦᎶᏁᏛ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏥᎩ, ᏄᏓᎴᏒ ᎤᎬᏫᏳᏌᏕᎩ, ᏫᎾᏍᏛᎾ ᎦᎸᏉᏙᏗ. ᎡᎹᏅ. (aiōn g165)
Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni. (aiōn g165)
6 ᎥᏝ ᎠᏗᎾ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏁᏨ ᎠᏎᏉᏉ ᏥᏄᎵᏍᏔᏃ ᎾᏍᎩᏯ [ ᏱᏥᏁᎦ, ] ᎥᏝᏰᏃ ᏂᎦᏛ ᎢᏏᎵ ᏱᎩ ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎵ ᏧᏁᏢᏔᏅᏛ ᏥᎩ.
Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli.
7 ᎥᏝ ᎠᎴ ᎡᏆᎭᎻ ᏧᏁᏢᏔᏅᏛ ᏥᎩ ᎾᏍᎩ ᏱᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᏂᎦᏛ ᏧᏪᏥ ᏱᎩ; ᎡᏏᎩᏉᏍᎩᏂ ᏚᏙᎥ ᎨᏥᏯᏅᏗᏍᎨᏍᏗ ᏣᏁᏢᏔᏅᎯ.
Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake.
8 ᎾᏍᎩ ᏯᏛᏅ, ᎤᏇᏓᎵ ᎨᏒ ᎤᎾᏕᏔᏅᎯ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎥᏝ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏧᏪᏥ ᏱᎩ; ᎠᏚᎢᏍᏛᏍᎩᏂ ᎤᎾᏕᏔᏅᎯ ᎨᏒ ᎾᏍᎩ ᏧᏪᏥ ᏧᏰᎸᏗ.
Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu.
9 ᎯᎠᏰᏃ ᏄᏍᏗ ᎤᎵᏁᏨ ᎠᏚᎢᏍᏛᎢ. ᎯᎠᏉ ᎢᏳ ᏓᏥᎷᏥ, ᎠᎴ ᏎᎵ ᏓᎦᎾᏄᎪᏫᏏ ᎠᏧᏣ.
Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”
10 ᎥᏝ ᎠᎴ ᎾᏍᎩᏉ ᏱᏄᏍᏗ; ᎵᏇᎩᏍᎩᏂ ᎾᏍᏉ ᎤᏁᎵᏨ, ᎾᏍᎩ ᎠᏏᏴᏫ ᎠᏥᏁᎵᏤᎸ, ᎾᏍᎩ ᎢᎩᏙᏓ ᎡᏏᎩ;
Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake.
11 ᏗᏂᏲᎵᏰᏃ ᎠᏏ ᎾᎾᏕᎲᏍᎬᎾ ᎨᏎᎢ, ᎠᎴ ᎠᏏ ᎪᎱᏍᏗ ᎣᏍᏛ ᎠᎴ ᎤᏲᎢ ᎾᎾᏛᏁᎲᎾ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᏓᏅᏖᎸ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎾᏍᎩᏯ ᏧᏑᏰᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᏲᎢᏍᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ, ᎥᏝ ᏚᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎬᎢ, ᎾᏍᎩᏯᏍᎩᏂ ᏗᏯᏂᏍᎩ ᎤᏓᏅᏖᎸᎢ;
Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire,
12 ᎯᎠ ᎾᏥᏪᏎᎴᎢ, ᎤᏓᏂᎵᎨ ᏚᏁᎶᏕᏍᏗ ᎣᏂ ᎡᎯ;
osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.”
13 ᎾᏍᎩᏯ ᎯᎠ ᏥᏂᎬᏅ ᏥᎪᏪᎳ, ᏤᎦᏈ ᎣᏏᏳ ᏥᏰᎸᏅ, ᎢᏐᏍᎩᏂ ᏥᏂᏆᏘᎸ.
Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”
14 ᎾᏍᎩᏃ ᏥᏄᏍᏗ ᎦᏙ ᏓᏓᏛᏂ? ᏥᎪ ᏂᏚᏳᎪᏛᎾ ᎨᏒ ᎤᏪᎭ ᎤᏁᎳᏅᎯ? ᎬᏩᏟᏍᏗ.
Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe!
15 ᎣᏏᏰᏃ ᎯᎠ ᎾᏥᏪᏎᎭ, ᏥᏯᏙᎵᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏥᏯᏙᎵᎩ ᎨᎵᏍᎨᏍᏗ, ᎠᎴ ᎤᏪᏙᎵᏍᏗ ᏥᏯᏓᏅᏓᏗᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎤᏪᏙᎵᏍᏗ ᏥᏯᏓᏅᏓᏓ ᎨᎵᏍᎨᏍᏗ.
Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti, “Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo, ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”
16 ᎾᏍᎩᏃ ᏥᏄᏍᏗ ᎥᏝ ᎩᎶ ᎤᏚᎸᎲ ᏱᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ, ᎥᏝ ᎠᎴ ᏚᏍᏆᎸᏔᏅ ᏱᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ, ᎤᎾᎳᏅᎯᏍᎩᏂ ᎤᏓᏅᏖᎸᎢ ᎾᏍᎩ ᏗᎦᏙᎵᎩ ᏥᎩ.
Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu.
17 ᎪᏪᎵᎯᏰᏃ ᎯᎠ ᎾᏥᏪᏎ ᏇᏓᏲ, ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᏕᎬᏯᎴᏔᏅ, ᎾᏍᎩ ᎠᎩᎾᏄᎪᏫᏍᏗᏱ ᎠᏆᎵᏂᎩᏗᏳ ᎨᏒ ᏂᎯ ᎬᏴᏗᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᏓᏆᏙᎥ ᏧᏃᏣᎶᎢᏍᏗᏱ ᎡᎶᎯ ᏂᎬᎾᏛᎢ.
Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.”
18 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎦᏙᎵᎪ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏥᏯᏙᎵᎩ ᎡᎳ, ᎠᎴ ᎩᎶ ᏥᏍᏓᏱᏓ ᎡᎳ ᎠᏍᏓᏱᏗᏍᎪᎢ.
Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.
19 ᎯᎠ Ꭷ ᎨᎵ ᏅᏛᏍᎩᏪᏎᎵ, ᎦᏙᏃ ᎠᏏᏉ ᎡᏍᎦ ᎠᏰᎸᏍᎦ? ᎦᎪᏰᏃ ᏚᎦᏘᎴᏅ ᏄᏍᏛ ᎠᏓᏅᏖᏍᎬᎢ?
Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?”
20 ᎠᏎᏃ ᏂᎯ ᏴᏫᏉ ᎦᎪ ᎢᏣᏍᏗ ᏥᏁᏤᎭ ᏕᎯᎦᏘᎴᎬ ᎤᏁᎳᏅᎯ? ᏥᎪ ᎪᎱᏍᏗ ᎠᏢᏅᎯ ᎯᎠ ᏅᏓᎦᏪᏎᎵ ᎾᏍᎩ ᎤᏬᏢᏅᎯ, ᎦᏙᏃ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏂᏍᏋᏁᎸ ᎢᏍᏉᏢᏅ?
Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’”
21 ᏝᏍᎪ ᏗᏩᎵ ᏗᎪᏢᏍᎩ ᏳᎭ ᎠᏓᏅᏖᏍᎬ ᎢᏳᏩᏁᎵᏓᏍᏗᏱ ᎦᏓᏆᎳ, ᎾᏍᎩᏉ ᎦᎾᏆᎸᏒ ᎠᎬᎭᎸᏛ ᏌᏉ ᎠᏖᎵᏙ ᎤᏬᏢᏗᏱ ᎦᎸᏉᏙᏗ, ᏅᏩᏓᎴᏃ ᎦᎸᏉᏙᏗ ᏂᎨᏒᎾ?
Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?
22 [ ᎦᏙᏃ ᏳᏍᏗ, ] ᎢᏳᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏚᎵᏍᎬ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏳᏩᏁᏗᏱ ᎤᏔᎳᏬᎯᏍᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎤᎵᏂᎬᎬ ᎤᎾᏄᎪᏫᏍᏗᏱ, ᎬᏂᏗᏳ ᎨᏒ ᎬᏗᏍᎬ ᎪᎯᏗᏳ ᎤᏁᎳᎩ ᏱᏚᏪᎵᏎᎸ ᏗᏖᎵᏙ ᎤᏔᎳᏬᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᏗᏟᏍᏗ, ᏗᏛᏅᎢᏍᏔᏅᎯ ᏗᏛᏙᏗᏱ;
Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko.
23 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ [ ᎤᏚᎵᏍᎬ ] ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏳᏩᏁᏗᏱ ᎤᏤᎵ ᎤᏣᏔᏅᎯ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᏕᎬᏗᏍᎬ ᏗᏖᎵᏙ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᏗᏟᏍᏗ, ᎾᏍᎩ ᏧᏛᏅᎢᏍᏔᏅᎯ ᏥᏂᎨᏎ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏗᎨᏒ ᏭᎾᏕᏗᏱ,
Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake
24 ᎾᏍᎩ ᎠᏴ, ᎢᎩᏯᏅᏛ ᏥᎩ, ᎥᏝ ᎠᏂᏧᏏᏉ ᎤᏅᏒ ᎠᏁᎲᎢ, ᎾᏍᏉᏍᎩᏂ ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ ᎠᏁᎲᎢ;
ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina.
25 ᎾᏍᎩᏯ ᎾᏍᏉ ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪ ᎰᏏᎠ ᎤᏬᏪᎸᎢ; ᏗᏆᏤᎵ ᏴᏫ ᎦᏥᏲᏎᎮᏍᏗ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏗᏆᏤᎵ ᏴᏫ ᏂᎨᏒᎾ ᏥᎨᏒᎩ; ᎠᎴ ᏥᎨᏳᎢ ( ᏥᏲᏎᎮᏍᏗ, ) ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏥᎨᏳᎢ ᏂᎨᏒᎾ ᏥᎨᏒᎩ.
Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti, “Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’ ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”
26 ᎠᎴ ᎯᎠ ᏅᏓᎦᎵᏍᏔᏂ, ᎾᎿᎭᏂ ᎯᎠ ᏂᎨᏥᏪᏎᎸᎢ, ᏂᎯ ᎥᏝ ᎠᏴ ᏗᏆᏤᎵ ᏴᏫ ᏱᎩ; ᎾᎿᎭᏂ ᎬᏂᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏧᏪᏥ ᎨᎪᏎᎮᏍᏗ.
ndipo, “Pamalo omwewo pamene ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’”
27 ᎢᏌᏯ ᎾᏍᏉ ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ ᎢᏏᎵ ᏕᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎬᎢ; ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ ᎾᏍᏉ ᏃᏳ ᎠᎺᏉᎯ ᎦᎳᎨᏴ ᎾᏍᎩᏯ ᏱᏄᎾᏧᏈᏍᏗ, ᎤᎾᎵᏃᎯᏴᎯ ᎠᏎ ᎨᏥᏍᏕᎸᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti, “Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiye adzapulumuke.
28 ᏛᏍᏆᏗᏰᏃ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᏚᏳᎪᏛ ᎬᏗ ᎤᎵᏍᏗᏳ ᎾᏍᎩ ᏅᏛᏛᏁᎵ; ᎤᎵᏍᏗᏰᏃ ᏅᏛᏛᏁᎵ ᏄᏍᏛ ᏚᏭᎪᏔᏅ ᎡᎶᎯ.
Pakuti Ambuye adzagamula milandu ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”
29 ᎠᎴ ᎾᏍᎩᏯ ᎢᏌᏯ ᎦᏳᎳ ᎯᎠ ᏥᏄᏪᏐᎢ, ᎢᏳᏃ ᏱᎰᏩ ᎤᏂᏣᏘ ᏧᏓᏘᎾᎢ ᏂᎩᏃᎯᏰᎸᎾ ᏱᎨᏎ ᎤᎵᏃᎯᏴᎯ, ᏐᏓᎻᏉ ᏱᏗᏓᏤᎴᎢ, ᎠᎴ ᎪᎹᎵ ᏄᏍᏛ ᎾᏍᎩᏯ ᏱᏂᎦᏍᏕᎢ.
Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti, “Ngati Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira zidzukulu, ife tikanawonongeka ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”
30 ᎾᏍᎩᏃ ᏥᏄᏍᏗ ᎦᏙ ᏓᏓᏛᏂ? ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ, ᎾᏍᎩ ᎠᏚᏓᎴᏍᏗ ᎨᏒ ᏄᏂᏍᏓᏩᏛᏒᎾ ᎨᏒ, ᎾᏍᎩ ᎠᏚᏓᎴᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᏂᏩᏛᎲ, ᎾᏍᎩ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᎠᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᏥᎩ.
Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro
31 ᎢᏏᎵᏍᎩᏂ ᎤᏂᏍᏓᏩᏛᏛ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ ᎠᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎥᏝ ᏳᏂᏩᏛᎲ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ ᎠᏚᏓᎴᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ.
koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire.
32 ᎦᏙᏃ? ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᎾᏍᎩ ᎪᎯᏳᏗ ᎨᏒ ᏄᏅᏔᏅᎾ ᎨᏒᎢ, ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗᏍᎩᏂ ᏂᎦᏪᏍᎬ ᎢᏯᏛᏁᏗ ᎨᏒ ᎤᏅᏔᏅᎢ; ᏚᏃᏕᏍᏔᏁᏰᏃ ᎾᏍᎩ Ꮎ ᏅᏯ ᏗᏓᏙᏕᎯᎯ ᎨᏒᎢ;
Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.”
33 ᎾᏍᎩᏯ ᎯᎠ ᏥᏂᎬᏅ ᏥᎦᏪᎳ, ᎬᏂᏳᏉ ᏌᏯᏂ ᏓᏥᏂ ᏅᏯ ᏗᏓᏙᏕᎯᎯ, ᎠᎴ ᏅᏯ ᎠᏓᎿᎭᏍᏆᎶᏍᏗᏍᎩ; ᎠᎴ ᎩᎶ ᎪᎯᏳᎲᏍᎨᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎥᏝ ᎤᏕᎰᎯᏍᏗ ᏱᎨᏎᏍᏗ.
Monga momwe kwalembedwa kuti, “Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”

< ᏉᎳ ᎶᎻ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 9 >