< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎹᏚ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 23 >

1 ᎿᎭᏉᏃ ᏥᏌ ᏚᏬᏁᏔᏅᎩ ᎤᏂᏣᏘ ᎠᎴ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ,
Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake:
2 ᎯᎠ ᏄᏪᏒᎩ; ᏗᏃᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎠᏂᏆᎵᏏ ᎼᏏ ᎤᏪᏍᎩᎸ ᎠᏂᎾ;
“Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose.
3 ᎾᏍᎩ ᎯᏳᏍᏗ ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᏗᏥᎧᎿᎭᏩᏚᎦ ᎨᏦᏎᎮᏍᏗ ᏕᏥᎧᎿᎭᏩᏕᎨᏍᏗ ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏂᏣᏛᏁᎮᏍᏗ; ᎠᏎᏃ ᎾᏍᎩ ᎾᎾᏛᏁᎲᎢ ᏞᏍᏗ ᏱᏂᏣᏛᏁᎮᏍᏗ; ᎠᏂᏁᎪᏰᏃ ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎾᏍᎩ ᏱᎾᎾᏛᏁᎰᎢ.
Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa.
4 ᏓᎾᏓᎵᏢᏍᎪᏰᏃ ᏗᎦᎨᏛ ᏗᎵᏒᏍᏗ ᎠᎴ ᎤᏕᏯᏙᏗ ᏗᎵᏒᏍᏗᏱ, ᎾᏍᎩᏃ ᏴᏫ ᏓᏂᏃᎭᏝᎲᏍᎪᎢ; ᎠᏎᏃ ᎤᏅᏒ ᎥᏝ ᏌᏉ ᎠᏂᏰᏌᏛ ᏴᎬᏅᏓ ᏱᏙᎬᏂᏖᎸᎲᎦ.
Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.
5 ᏂᎦᏗᏳᏍᎩᏂ ᏚᏂᎸᏫᏍᏓᏁᎲ ᏴᏫᏉ ᎬᏩᏂᎪᏩᏛᏗᏱ ᎤᏂᏰᎸᏐᎢ. ᏗᏯᏖᎾ ᏂᏓᏅᏁᎰ ᏧᎾᎬᏓᏃᏍᏗ, ᎠᎴ ᏓᏂᏯᏛᎥᏍᏗᏍᎪ ᏕᎦᏓᎷᏯᏛ ᏧᎾᏄᏬ;
“Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo.
6 ᎠᎴ ᎤᏂᎸᏉᏙ ᏄᎬᏫᏳᏒ ᏧᎾᏂᏢᏗᏱ ᏓᎾᎵᏍᏓᏴᎲᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᏄᎬᏫᏳᏒ ᏕᎦᏍᎩᎸ ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ,
Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge.
7 ᎠᎴ ᎨᏥᏲᎵᏍᏗᏱ ᏗᎦᏃᏙᏗᏱ, ᎠᎴ ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᎬᏩᏃᏎᏗᏱ ᏴᏫ.
Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’
8 ᏂᎯᏍᎩᏂ ᏞᏍᏗ ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᏰᏦᏎᎮᏍᏗ; ᎠᏏᏴᏫᏰᏃ ᏗᏤᏲᎲᏍᎩ, ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ; ᏂᎦᏛᏃ ᏂᎯ ᎢᏣᎵᏅᏟᏉ.
“Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale.
9 ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᎩᎶ ᎡᏙᏓ ᎡᏦᏎᎸᎩ ᎠᏂ ᎡᎶᎯ; ᎠᏏᏴᏫᏉᏰᏃ ᎢᏥᏙᏓ, ᎾᏍᎩ ᎦᎸᎳᏗ ᏨᏤᎭ.
Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba.
10 ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᏍᏆᏘᏂᏙᎯ ᏰᏦᏎᎮᏍᏗ ᏂᎯ, ᎠᏏᏴᏫᏉᏰᏃ ᏗᏣᏘᏂᏙᎯ, ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ.
Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu.
11 ᎩᎶᏍᎩᏂ ᎤᏟ ᎠᏥᎸᏉᏗᏳ ᎨᏎᏍᏗ ᏂᎯ ᎢᏤᎲᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᏥᏅᏏᏓᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani.
12 ᎩᎶᏃ ᎤᏩᏒᏉ ᎢᎠᏓᏌᎳᏗᏍᎨᏍᏗ ᎡᎳᏗ ᎢᏯᎬᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ; ᎩᎶᏃ ᎤᏩᏒᏉ ᎡᎳᏗ ᎾᏓᏛᏁᎮᏍᏗ ᎠᏥᏌᎳᏙᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.
13 ᏂᎯᏍᎩᏂ ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᏕᏥᏍᏚᏁᎰᏰᏃ ᏴᏫ ᎦᎸᎳᏗ ᎤᏤᎵᎪᎯ; ᎥᏝᏰᏃ ᎢᏨᏒ ᏱᏥᏴᎯᎰᎢ, ᎠᎴ ᎥᏝ ᎤᎾᏁᎳᎩ ᏩᏂᏴᎭ ᏱᏗᏤᎵᏎᎰ ᏩᏂᏴᎯᎯ.
“Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe.
14 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᏕᏥᏒᏁᎰᏰᏃ ᏧᏃᏑᎶᏨᎯ ᏓᏂᏁᎸᎢ, ᎠᎴ ᎢᏣᏠᎾᏍᏛ ᎪᎯᏗᏳ ᎢᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎪᎢ. ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎤᏟᎯᏳ ᎢᎦᎢ ᎢᏥᎩᎵᏲᎢᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.
15 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᏕᏣᏕᏲᎰᏰᏃ ᎠᎺᏉᎯ ᎠᎴ ᎦᏙᎯ ᎡᏥᏲᎰ ᎠᏏᏴᏫ ᏄᏍᏛ ᎢᏦᎯᏳᏒ ᎪᎯᏳᎲᏍᎩ ᎢᏰᏨᏁᏗᏱ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏁᏨᎦ ᏔᎵ ᎢᏳᏩᎫᏗ ᎤᏟ ᏨᏍᎩᏃᎢ ᎤᏪᏥ ᏁᏨᏁᎰ ᎡᏍᎦᏉ ᎢᏨᏒ. (Geenna g1067)
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu. (Geenna g1067)
16 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ, ᏗᏥᎨᏫ ᏗᏣᏓᏘᏂᏙᎯ! ᎯᎠ ᎢᏥᏪᏍᎩ; ᎩᎶ ᎢᎠᏎᎵᏛᏍᎨᏍᏗ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎤᏛᏅ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ, ᎠᏎᏉᏉ ᎾᏍᎩ; ᎩᎶᏍᎩᏂ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᏕᎸ ᏓᎶᏂᎨ ᎤᏛᎾ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ ᎠᎲᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏍᏓᏱᏳ ᎤᏚᏓᎳ.
“Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
17 ᎢᏥᏁᎫ ᎠᎴ ᏗᏥᎨᏫ! ᎦᏙ ᎤᏍᏗ ᎤᏟ ᎦᎸᏉᏗᏳ, ᎠᏕᎸᏍᎪ ᏓᎶᏂᎨᎢ, ᎤᏛᎾ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱᎨ ᎾᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏥᏂᎬᏁᎭ ᎠᏕᎸ ᏓᎶᏂᎨᎢ?
Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo?
18 ᎠᎴ, ᎩᎶ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᏥᎸ-ᎨᎳᏍᏗᏱ, ᎠᏎᏉᏉ ᎾᏍᎩ; ᎩᎶᏍᎩᏂ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯ ᎾᎿᎭᎠᎲᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏍᏓᏱᏳ ᎤᏚᏓᎳ.
Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’
19 ᎢᏥᏁᎫ ᎠᎴ ᏗᏥᎨᏫ! ᎦᏙ ᎤᏍᏗ ᎤᏟ ᎦᎸᏉᏗᏳ, ᎠᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯᏍᎪ, ᎠᏥᎸᎨ-ᎨᎳᏍᏗᏱ, ᎾᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏥᏂᎬᏁᎭ ᎠᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯ?
Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo?
20 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎩᎶ ᎢᎠᏎᎵᏛᏍᎨᏍᏗ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎠᏥᎸᎨᎳᏍᏗᏱ, ᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎠᎴ ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᎾᎿᎭᎠᎲᎢ.
Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo.
21 ᎠᎴ ᎩᎶ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎤᏛᏅ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ, ᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎾᏍᎩ ᎠᎴ ᎾᎿᎭᎦᏁᎳ.
Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo.
22 ᎠᎴ ᎩᎶ ᎢᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎦᎸᎳᏗ, ᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏪᏗᏱ ᎠᎴ ᎾᎿᎭᎤᏬᎵ.
Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.
23 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᎠᏍᎪᎯᏁᏰᏃ ᎢᏣᎫᏱᏍᎪ ᏒᏟ ᎠᎴ ᎡᏒ ᎠᎴ ᎦᎻᏂ; ᏕᏥᏃᎯᏯᏍᎪᏃ ᎤᏟ ᎤᎵᏍᎨᏛᏯ ᎨᏒ ᏗᎧᎿᎭᏩᏛᏍᏗ, ᏚᏳᎪᏛ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎠᏓᏙᎵᏍᏗᏱ, ᎠᎴ ᎪᎯᏳᏗᏱ. ᎾᏍᎩᏍᎩᏂ ᎯᎠ ᏱᏂᏣᏛᏁᎴᎢ, ᎠᎴ ᏐᎢ ᏂᏥᏃᎯᏴᎾᏉ ᏱᎨᏎᎢ.
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo.
24 ᏗᏥᎨᏫ ᏗᏣᏓᏘᏂᏙᎯ! ᏙᏒ ᎢᏥᎿᎭᏐᎸᏍᏗᏍᎩ ᎨᎻᎵᏃ ᎢᏥᎩᏍᎩ.
Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.
25 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᎢᏦᏑᎴᏍᎪᏰᏃ ᎦᏚᎢᏗᏢ ᎤᎵᏍᏈᏗ ᎠᎴ ᎠᏖᎵᏙ, ᎠᏎᏃ ᎠᏫᏂᏗᏢ ᎤᎧᎵᏨᎯ ᎨᏐ ᎠᏎᏉ ᎠᏓᎩᎡᏗ ᎨᏒᎢ ᎠᎴ ᏚᏳᎪᏛ ᏂᎨᏒᎾ.
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa.
26 ᎯᏆᎵᏏ ᏘᎨᏫ! ᎢᎬᏱ ᎯᏅᎦᎸ ᎠᏫᏂᏗᏢ ᎤᎵᏍᏈᏗ ᎠᎴ ᎠᏖᎵᏙ, ᎦᏚᎢᏗᏢᏃ ᎾᏍᏉ ᏧᏓᏅᎦᎸᏛ ᎨᏎᏍᏗ.
Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.
27 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᎾᏍᎩᏯᏉᏰᏃ ᏂᎯ ᏧᏁᎬ ᎢᏗᎬᏁᎸᎯ ᏓᏤᎵᏍᏛᎢ, ᎾᏍᎩ ᎦᏚᎢᏗᏢ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᏧᏬᏚᎯᏳ ᏥᎨᏐᎢ, ᎠᏎᏃ ᎠᏫᏂᏗᏢ ᏧᎧᎵᏨᎯ ᏥᎨᏐ ᏧᏂᏲᎱᏒᎯ ᏧᏂᎪᎳ ᎠᎴ ᏂᎦᎥ ᎦᏓᎭ ᎨᏒᎢ
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse.
28 ᎾᏍᎩᏯᏉᏍᎩᏂ ᎾᏍᏉ ᏂᎯ ᎦᏚᎢᏗᏢ ᎢᏣᏓᏅᏘᏳ ᏅᏩᏍᏙᎢ ᏴᏫ ᏗᎨᏣᎧᏃᏗᏱ, ᎠᏎᏃ ᎠᏫᏂᏗᏢ ᎢᏥᎧᎵᏨᎯ ᎨᏐ ᎢᏣᏠᎾᏍᏛᎢ ᎠᎴ ᎤᏲᎢ.
Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.
29 ᎤᏲᎢᏳ ᎢᏣᎵᏍᏓᏁᏗ ᏗᏦᏪᎵᏍᎩ ᎠᎴ ᎢᏥᏆᎵᏏ ᎢᏣᏠᎾᏍᏗ! ᏕᏦᏢᎯᏏᏍᎪᏰᏃ ᏕᎦᏂᏌᎲ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ, ᎠᎴ ᏕᏦᏚᎢᏍᏗᏍᎪ ᏓᏤᎵᏍᏛ ᎤᎾᏓᏅᏘ;
“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama.
30 ᎯᎠᏃ ᏂᏥᏪᏍᎪᎢ; ᎢᏳᏃ ᎠᏴ ᏲᏤᎮ ᎾᎯᏳ ᏦᎩᏙᏓ ᏣᏁᎮᎢ, ᎥᏝ ᏱᏙᎦᏲᏣᎵᎪᏁᎴ ᎩᎬ ᏚᎾᏤᏪᎸ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ.
Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’
31 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎢᏨᏒ ᎬᏂᎨᏒ ᏂᏣᏓᏛᏁ ᎾᏍᎩ ᏗᏥᏙᏓ ᎨᏒ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᏧᏂᎸᎯ.
Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.
32 ᎢᏥᎧᎵᏣᎪᎦ ᏗᏥᏙᏓ ᎤᎾᏟᎶᎥᎢ.
Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!
33 ᎢᎾᏛ ᏂᎯ! ᎤᏂᏍᎦᏎᏗ ᎢᎾᏛ ᏧᏁᏥ ᏂᎯ! ᎦᏙᏃ ᏱᎦᎵᏍᏙᏓ ᏰᏣᏗᏫᏏ ᎠᎩᎵᏲᎢᏍᏗ ᏗᎨᏒ ᏨᏍᎩᏃᎢ? (Geenna g1067)
“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? (Geenna g1067)
34 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎬᏂᏳᏉ ᏕᏥᏅᎵ ᎾᎿᎭᏗᏤᎲ ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᎠᎴ ᎠᏂᎦᏔᎿᎭᎢ ᎠᎴ ᏗᏃᏪᎵᏍᎩ; ᎢᎦᏛᏃ ᏙᏓᏥᎵ ᎠᎴ ᏙᏓᏣᏛᏂ ᏓᏓᎿᎭᏩᏍᏛᎢ, ᎢᎦᏛᏃ ᏙᏓᏥᎵᎥᏂᎵ ᏗᏥᎳᏫᎢᏍᏗᏱ, ᎠᎴ ᎤᏲ ᏂᏙᏓᏨᏁᎵ ᏕᎦᏚᎿᎭᎥᎢ;
Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina.
35 ᎾᏍᎩ ᎢᏥᎷᏤᏗᏱ ᏂᎦᏛ ᎣᏍᏛ ᎩᎬ ᎡᎶᎯ ᎤᏤᏬᏨᎯ, ᎤᏓᏅᏘ ᎡᏈᎵ ᎤᎩᎬ ᏅᏓᎬᏩᏓᎴᏅᏛ, ᏤᎦᎳᏯ ᎤᎩᎬ ᏇᎵᎦᏯ ᎤᏪᏥ ᏅᏛᏍᏗ, ᎾᏍᎩ ᏤᏥᎸ ᎤᏜᏓᏅᏛ ᎤᏛᎾ-ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ ᎠᏥᎸᏃ-ᎨᎳᏍᏗᏱ.
Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu.
36 ᎤᏙᎯᏳᎯᏯ ᎯᎠ ᏂᏨᏪᏎᎭ; ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᏂᎦᏛ ᏓᏳᎾᎵᏱᎶᎮᎵ ᎯᎠ ᎪᎯ ᏣᏁᎭ.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.
37 ᏥᎷᏏᎵᎻ! ᏥᎷᏏᎵᎻ! ᎠᎾᏙᎴᎰᏍᎩ ᏘᎯᎯ, ᎠᎴ ᎨᏣᎷᏤᏗᏱ ᎨᏥᏅᏒᎯ ᏅᏯ ᏛᏂᏍᏗᏍᎩ! ᏯᏃᎩᏳ ᎠᏆᏚᎵᏍᎬ ᎦᏥᏯᏟᏐᏗᏱ ᏗᏤᏥ, ᎾᏍᎩᏯ ᏣᏔᎦ ᏥᏕᎦᏟᏏᏍᎪ ᏧᏪᏥ ᎠᏂᏛ ᏗᎧᏃᎨᏂ ᎭᏫᏂᏗᏢ; ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᏱᏣᏚᎵᏍᎨᎢ.
“Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune.
38 ᎬᏂᏳᏉ ᎢᏣᏤᎵ ᎦᎵᏦᏕ ᏅᏔ ᏁᏨᏁᎸ.
Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja.
39 ᎯᎠᏰᏃ ᏂᏨᏪᏎᎭ; ᎥᏝ ᏴᎨᏍᎩᎪᏩᏛ ᎪᎯ ᎢᏳᏓᎴᏅᏛ, ᎬᏂ ᎯᎠ ᏂᏥᏪᏒᎭ; ᎠᏥᎸᏉᏗᏳ ᎾᏍᎩ ᏱᎰᏩ ᏕᎤᏙᎥ ᏥᎦᎷᎯᏍᏗᎭ.
Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’”

< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎹᏚ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 23 >