< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎷᎦ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 3 >

1 ᎯᏍᎩᎦᏚᏏᏁᏃ ᎤᏕᏘᏴᏌᏗᏒ ᏓᏈᎵᏯ ᏏᏌ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎨᏒᎢ, ᏋᏗᏯ ᏆᎴᏗ ᏧᏗᏱ ᏣᎦᏁᎶᏗ ᎨᏎᎢ, ᎠᎴ ᎡᎶᏛ ᎨᎵᎵ ᏍᎦᏚᎩ ᎨᏒ ᎠᏥᎦᏘᏗᏍᏗ ᎨᏎᎢ, ᎤᏅᏟᏃ ᏈᎵᎩ ᎢᏚᎵ ᎠᎴ ᏝᎪᏂᏗ ᎠᏥᎦᏘᏗᏍᏗ ᎨᏎᎢ, ᎵᏌᏂᏯᏃ ᎠᏈᎵᏂ ᎠᏥᎦᏘᏗᏍᏗ ᎨᏎᎢ;
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 ᎡᎾᏃ ᎠᎴ ᎦᏱᏆ ᏄᏂᎬᏫᏳᏒ ᎠᏥᎸ-ᎠᏁᎶᎯ ᎨᏎᎢ, ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏬᏂᏒᎯ ᎢᎾᎨ ᎤᎷᏤᎴ ᏣᏂ ᏤᎦᎳᏯ ᎤᏪᏥ.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᎷᏤ ᎤᏪᏙᎴ ᏦᏓᏂ ᎾᎥᏂᎨ ᎨᏒᎢ, ᎠᎵᏥᏙᎲᏍᎨ ᎧᏃᎮᏍᎨ ᏗᏓᏬᏍᏗ ᎨᏒ ᎦᏁᏟᏴᏛ ᎨᏒ ᎣᏓᏅᏛᎢ, ᎾᏍᎩ ᎦᏴᏓᏘᏁᏗᏱ ᎣᏍᎦᏅᏨᎢ;
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 ᎾᏍᎩᏯ ᏂᎬᏅ ᎪᏪᎸ ᎪᏪᎵᎯ ᎢᏌᏯ ᎠᏙᎴᎰᏍᎩ ᎤᏪᏂᏒᎯ, ᎯᎠ ᏥᏂᎦᏪᎭ; ᎤᏪᎷᎦ ᎩᎶ ᎢᎾᎨᎢ, ᎯᎠ ᏂᎦᏪᎭ; ᎡᏣᏛᏅᎢᏍᏓᏏ ᏱᎰᏩ ᎤᎶᎯᏍᏗᏱ, ᏚᏅᏅ ᏗᏥᏥᏃᎯᏍᏓ.
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 ᏚᎨᏓᎵᏴᏅ ᏂᎦᏗᏳ ᏗᎧᎵᎢᏍᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᏙᏓᎸᏃ ᎠᎴ ᏚᏌᎯᎸ ᏂᎦᏗᏳ ᎡᎳᏗᎭ ᎢᏗᎬᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᏧᏓᏥᏃᏍᏈᏗᏰᏛᏃ ᎨᏒ ᏗᎦᏥᏃᎯᏍᏙᏗ ᎨᏎᏍᏗ, ᎤᏲᏃ ᏕᎦᏅᏅ ᎬᎾᏕᏍᎩ ᎢᏗᎬᏁᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 ᏂᎦᏛᏃ ᎤᏇᏓᎵ ᏛᎪᎯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏓᏍᏕᎸᏙᏗ ᎨᏒᎢ.
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 ᎿᎭᏉᏃ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎴ ᎤᏂᏣᏘ ᎾᏍᎩ ᏗᎨᎦᏬᏍᏗᏱ ᎤᏂᎸᏐᎸᎯ; Ᏺ ᎢᎾᏛ ᏧᏁᏥ ᏂᎯ! ᎦᎪ ᎢᏤᏯᏔᏅ ᎡᏣᎵᎡᏗᏱ ᎤᏔᎳᏬᎯᏍᏗ ᎤᎷᎯᏍᏗ ᎨᏒᎢ?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎢᏥᎾᏄᎪᏩ ᎠᏙᎴᎰᎯᏍᏙᏗ ᏕᏥᏁᏟᏴᏒ ᏕᏣᏓᏅᏛᎢ; ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᎢᏣᎴᏅᎲ ᎯᎠ ᎢᏥᏪᏒ ᏕᏣᏓᏅᏛᎢ; ᎡᏆᎭᎻ ᎣᎩᏙᏓ ᎠᏴ; ᎢᏨᏲᏎᏰᏃ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᏰᎵᏉ ᎯᎠ ᏅᏯ ᏱᏕᎬᏓ ᏱᏕᎪᏢᎾ ᎡᏆᎭᎻ ᏧᏪᏥ.
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 ᎠᎴ ᎾᏍᏉ ᎦᏳᎳ ᎦᎷᏯᏍᏗ ᎠᏅᎯ ᏚᎿᎭᏍᏕᏢ ᏕᏡᎬᎢ; ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᏂᎦᏗᏳ ᏕᏡᎬ ᎣᏍᏛ ᎾᏓᏛᏍᎬᎾ ᎢᎨᏎᏍᏗ ᏗᎦᎴᏴᏍᏙᏗ ᎠᎴ ᎠᏥᎸᏱ ᏫᏓᏗᏅᏗ ᎨᏎᏍᏗ.
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 ᎤᏂᏣᏘᏃ ᎬᏩᏛᏛᏁ ᎯᎠ ᏂᎬᏩᏪᏎᎴᎢ; ᎦᏙ ᏓᏲᏣᏛᏁᎵ?
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 ᎤᏁᏨ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎴᎢ; ᎩᎶ ᏔᎵ ᏗᎦᏌᎴᎾ ᏚᎾᎡᏍᏗ, ᏄᎾᎥᎾ ᎨᏒ ᎦᏅᏁᎮᏍᏗ; ᎩᎶᏃ ᎠᎵᏍᏓᏴᏗ ᎤᎮᏍᏗ, ᎾᏍᎩᏯ ᎾᏛᏁᎮᏍᏗ.
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 ᎾᏍᏉᏃ ᎠᏕᎸ-ᎠᏂᎩᏏᏙᎯ ᎤᏂᎸᏐᎴ ᏗᎨᎦᏬᏍᏗᏱ, ᎠᎴ ᎯᎠ ᏂᎬᏩᏪᏎᎴᎢ; ᏔᏕᏲᎲᏍᎩ, ᎦᏙ ᏓᏲᏣᏛᏁᎵ?
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 ᎯᎠᏃ ᏂᏚᏪᏎᎴᎢ; ᏞᏍᏗ ᏱᏥᎶᏒᏍᏗᏍᎨᏍᏗ ᎢᎦᎢ ᎡᏥᏁᏤᎸ ᎢᏥᎩᏏᏓᏍᏗᏱ.
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 ᎠᏂᏯᏫᏍᎩᏃ ᎾᏍᏉ ᎢᎬᏩᏛᏛᏁ, ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏎᎢ; ᎠᏴ ᎾᏃ ᎦᏙ ᏓᏲᏣᏛᏁᎵ? ᎯᎠᏃ ᏂᏚᏪᏎᎴᎢ; ᏞᏍᏗ ᎩᎶ ᎬᏍᎦᎢᏍᏓᎩ ᎢᏰᏨᏁᎸᎩ, ᎠᎴ ᏞᏍᏗ ᎦᏰᎪᎩ ᏱᏣᏓᎳᏫᏎᎮᏍᏗ; ᎠᎴ ᏰᎵᏉ ᎢᏥᏰᎸᏎᏍᏗ ᎡᏣᎫᏴᎡᎲᎢ.
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 ᎤᏂᏣᏘᏃ ᎠᏂᎦᏖᏃᎮᎢ, ᎠᎴ ᏂᎦᏛᏉ ᎠᏫ ᏙᏧᎾᏓᏅᏛ ᎬᏩᏓᏅᏖᏍᎨ ᏣᏂ, ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ ᎨᏒ, ᎠᎴ ᎦᎶᏁᏛ ᏂᎨᏒᎾ ᎨᏒᎢ;
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 ᏣᏂ ᎤᏁᏤ ᎯᎠ ᏂᏚᏪᏎᎴ ᏂᎦᏛ, ᎠᏴ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᎠᎹ ᏕᏨᏯᏬᏍᏗᎭ; ᏓᏯᎢᏍᎩᏂ ᎤᏟ ᎤᎵᏂᎩᏗᏳ ᎡᏍᎦᏉ ᎠᏴ, ᎾᏍᎩ ᏓᎧᏁᏌᏛ ᏧᎳᏑᎶᎩ ᎥᏝ ᏰᎵ ᏱᏂᎪᎢ ᏗᎩᎧᏁᏴᏗᏱ; ᎾᏍᎩ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ ᎠᎴ ᎠᏥᎸ ᏙᏓᏣᏬᏍᏔᏂ;
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 ᎾᏍᎩ ᎤᎳᏐᏫᏍᏗ ᎠᏰᎭ, ᎠᎴ ᏂᎦᏛ ᏓᎦᎳᏐᏫᏏ ᎠᏲᏓᏝᎲᎢ, ᎤᏣᎴᏍᏗᏃ ᏓᎦᏟᏌᏂ ᏛᏂ ᎤᏗᏱ; ᎤᏬᎭᏄᎶᏔᏅᎯᏍᎩᏂ ᏛᎪᎲᏍᏔᏂ ᎠᏥᎸᏱ ᏂᎬᏠᏍᎬᎾ.
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 ᎠᎴ ᎤᏣᏖ ᏧᏓᎴᏅᏛ ᏕᎦᏬᏁᏗᏍᎬ ᏚᎵᏥᏙᏁᎴ ᏴᏫ.
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 ᎡᎶᏛᏍᎩᏂ ᏍᎦᏚᎩ ᎠᏥᎦᏘᏗᏍᏗ ᎨᏒᎢ, ᏣᏂ ᎤᎬᏍᎪᎸᏁ ᏗᎵᏰᎢᎸᏍᏗᏍᎨ ᎡᎶᏗᏏ ᎤᏅᏟ ᏈᎵᎩ ᎤᏓᎴᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᏉ ᏂᎦᏛ ᎤᏣᏘᏂ ᏄᏛᏁᎸ ᎡᎶᏛ,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 ᎠᏏ ᏭᏓᎪᎾᏛ ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᏄᏛᏁᎴᎢ, ᏣᏂ ᏗᏓᏍᏚᏗᏱ ᎤᏍᏚᏁᎢ.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 ᎿᎭᏉᏃ ᎯᎠ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᏂᎦᏛ ᏴᏫ ᏕᎨᎦᏬᎥ ᏥᏌ ᎾᏍᏉ ᎠᎦᏬᎡᎢ, ᎠᎴ ᎤᏓᏙᎵᏍᏔᏅ ᎦᎸᎳᏗ ᎤᎵᏍᏚᎢᏎᎢ,
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 ᎠᎴ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ ᏧᏠᎠᏎ ᎾᏍᎩ ᎤᏪᏯᎸᏤᎢ, ᎠᏰᎸ ᏧᎴ-ᏗᏍᎪᏂᎯ ᎾᏍᎩᏯ ᎨᏎ ᎤᏙᏢᏒᎢ; ᎧᏁᎬᏃ ᎦᎸᎳᏗ ᏧᎶᏎ ᎯᎠ ᏅᏧᏪᏎᎢ; ᎯᎯ ᎬᎨᏳᎢ ᎠᏇᏥ; ᎣᏏᏳ ᎬᏰᎸᎢ ᏂᎯ.
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 ᏥᏌᏃ ᎿᎭᏉ ᎠᏎ ᏦᎠᏍᎪᎯ ᎢᏳᏕᏘᏴᏛ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᏩ ᎤᏪᏥ ᎤᏂᏰᎸᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎯᎳᏱ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 ᎾᏍᎩ ᎹᏓᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎵᏫ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎺᎵᎦᏱ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏣᎾ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᏩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 ᎾᏍᎩ ᎹᏗᏓᏯ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᎼᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏁᎠᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᏏᎳ, ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎾᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 ᎾᏍᎩ ᎺᎠᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎹᏗᏓᏯ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏏᎻᏯ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᏩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏧᏓ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 ᎾᏍᎩ ᏦᎠᎾ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎵᏌ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏥᎳᏇᎵ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏌᎳᏓᏱᎵ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏏᎳᏱ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 ᎾᏍᎩ ᎺᎵᎦᏱ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏓᏱ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎪᏌᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᎵᎼᏓᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎥᎵ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 ᎾᏍᎩ ᏦᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎢᎵᎡᏌ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᎵᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎹᏓᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎵᏫ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 ᎾᏍᎩ ᏏᎻᏯᏂ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏧᏓ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᏩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏦᎾᏂ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎢᎳᏱᎩᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 ᎾᏍᎩ ᎻᎵᎠ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎻᎾᏂ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎹᏓᏓ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏁᏓᏂ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏕᏫ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 ᎾᏍᎩ ᏥᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎣᏆᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏉᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏌᎵᎹ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎾᏐᏂ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 ᎾᏍᎩ ᎡᎻᏂᏓ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᎵᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎢᏏᎳᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏇᎵᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏧᏓ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 ᎾᏍᎩ ᏤᎦᏈ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᏏᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎡᏆᎭᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏕᎳ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏁᎰ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 ᎾᏍᎩ ᏎᎳᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎴᎪ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏇᎵᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎯᏆ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏎᎳ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 ᎾᏍᎩ ᎧᏱᏅ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏆᏣ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏎᎻ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏃᏯ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎴᎻᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 ᎾᏍᎩ ᎻᏚᏏᎳ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎢᏃᎩ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏤᎳᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎹᎵᎵᎵ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎧᏱᏅ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 ᎾᏍᎩ ᎢᏃᏏ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᏎᏗ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏓᏫ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏪᏥ ᎨᏎᎢ.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛ ᎷᎦ ᎤᏬᏪᎳᏅᎯ 3 >