< ᏉᎳ ᎪᎶᏏ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 1 >

1 ᏉᎳ, ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎠᎩᏅᏏᏛ ᎾᏍᎩᏯ ᎣᏏᏳ ᎤᏰᎸᏅ ᎤᏁᎳᏅᎯ, ᎠᎴ ᏗᎹᏗ ᎢᎩᏅᏟ,
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
2 ᏫᏨᏲᏪᎳᏏ ᎢᏣᏓᏅᏘ ᎪᎶᏏ ᎢᏤᎯ ᎠᎴ ᎢᏣᎵᏅᏟ ᎦᎶᏁᏛ ᎡᏦᎯᏳᎲᏍᎩ; ᎬᏩᎦᏘᏯ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ, ᎠᎴ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᎢᏤᎳᏗᏙᎮᏍᏗ ᏅᏓᏳᎾᎵᏍᎪᎸᏔᏅᎯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎢᎩᏙᏓ, ᎠᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ.
Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
3 ᎣᏣᎵᎡᎵᏤᎭ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎠᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᎦᏤᎵ ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏙᏓ, ᎣᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎪ ᏂᎪᎯᎸ ᎢᏨᏯᏅᏓᏗᏍᎪᎢ,
Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
4 ᎣᎦᏛᎦᏅᎯ ᎨᏒ ᎦᎶᏁᏛ ᏥᏌ ᎡᏦᎢᏳᏒᎢ, ᎠᎴ ᏕᏥᎨᏳᏒ ᎾᏂᎥ ᎤᎾᏓᏅᏘ;
Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
5 ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ ᎤᏚᎩ ᎢᏨᏒ ᎾᏍᎩ ᎦᎸᎳᏗ ᏤᏣᏛᏅᎢᏍᏓᏁᎸᎢ, ᎾᏍᎩ ᎦᏳᎳ ᎢᏣᏛᎦᏅᎯ ᏥᎩ ᎾᎿᎭᎦᏰᎪᎩ ᏂᎨᏒᎾ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛᏱ,
Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
6 ᎾᏍᎩ ᎢᏥᎷᏤᎸᎯ ᏥᎩ, ᎾᏍᎩᏯ ᏂᎬᎾᏛ ᎡᎶᎯ ᏧᏂᎷᏤᎸ; ᎠᎴ ᏥᎦᎾᏄᎪᏫᏍᎦ ᎤᏓᏔᏅᎯ ᎾᏍᎩᏯ ᏥᏂᎦᎵᏍᏗ ᏂᎯ ᎢᏤᎲᎢ, ᏅᏓᎬᏩᏓᎴᏅᏛ ᎢᏣᏛᎦᏅ ᎾᏍᎩ, ᎠᎴ ᎤᏙᎯᏳᎯ ᎢᏥᎦᏙᎥᏒ ᎬᏩᎦᏘᏯ ᎤᏓᏙᎵᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᏁᎳᏅᎯ;
umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
7 ᎾᏍᎩᏯ ᎾᏍᏉ ᏤᏣᏛᎦᏁᎸ ᎡᎦᏆ ᎣᏥᎨᏳᎢ ᎢᏧᎳᎭ ᎣᎩᏅᏏᏓᏍᏗ, ᏂᎯᏃ ᏥᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗ ᎣᏍᏛ ᎢᏯᏛᏁᎯ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᏅᏏᏓᏍᏗ.
Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
8 ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏲᎲᏁᎸᎯ ᏕᏣᏓᎨᏒ ᎠᏓᏅᏙ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ.
Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
9 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎠᏴ ᎾᏍᏉ, ᎣᎦᏛᎦᏅ ᏅᏓᎬᏩᏓᎴᏅᏛ, ᎥᏝ ᏲᏥᏲᎯᏍᏗᏍᎪ ᎣᏣᏓᏙᎵᏍᏗᏍᎬ ᎠᎴ ᎣᏥᏔᏲᎯᎲ ᎾᏍᎩ ᎠᏓᏅᏖᏍᎬ ᎠᎦᏙᎥᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎢᏥᎧᎵᎢᏍᏗᏱ, ᎾᏍᎩ ᏂᎦᎥ ᎠᎦᏙᎥᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎠᎴ ᎠᏓᏅᏙ ᎤᎬᏩᎵ ᎪᎵᏥᏓᏍᏗ ᎨᏒᎢ;
Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
10 ᎾᏍᎩ ᎢᏣᎴᏂᏓᏍᏗᏱ ᎾᏍᎩᏯ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏗᏂᎧᎿᎭᏩᏕᎩ ᎢᏳᎾᏛᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᏂᎦᎥ ᎣᏏᏳ ᎤᏰᎸᏗ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎣᏍᏛ ᏗᎦᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎤᏣᏘ ᎢᏥᎾᏄᎪᏫᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᎧᏁᏉᎬ ᎡᏥᎦᏙᎥᏍᎬ ᎤᏁᎳᏅᎯ;
Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
11 ᏕᏣᎵᏂᎪᏍᎬᎢ ᎬᏔᏅᎯ ᎤᏣᏘ ᎤᎵᏂᎩᏛ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩᏯ ᏄᎵᏂᎬᎬ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎤᏤᎵᎦ, ᎾᏍᎩ ᏂᎦᎥᏉ ᎤᎬᏩᎵ ᏗᏨᏂᏗᏳ ᎢᏣᎵᏍᏙᏗᏱ, ᎠᎴ ᎪᎯᏗᏳ ᎤᏁᎳᎩ ᎢᏤᎵᏍᎬ ᎢᏥᎩᎵᏲᎬᎢ, ᎤᎵᏠᏯᏍᏙᏗᏱ ᎠᎵᎮᎵᏍᏗ ᎨᏒᎢ;
Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
12 ᎡᏣᎵᎡᎵᏤᎲ ᎠᎦᏴᎵᎨᎢ ᎾᏍᎩ ᏰᎵᏉ ᎢᎦᏠᏯᏍᏙᏗ ᎢᎬᏩᎵᏍᏙᏗ ᎢᎬᏁᎸᎯ ᏥᎩ ᎤᎾᏤᎵ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗ ᎨᏒ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎢᎦ-ᎦᏛ ᎠᏁᎯ;
ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
13 ᎾᏍᎩ ᎢᎫᏓᎴᏛ ᏥᎩ ᎤᎵᏂᎩᏗᏳ ᎨᏒ ᎤᎵᏏᎩ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏫᏗᎩᎧᏅᎯ ᏥᎩ ᎾᎿᎭᎤᎬᏫᏳᎯ ᎨᏒ ᎤᎨᏳᎯ ᎤᏪᏥ;
Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
14 ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏩᏂᏌᏛ ᎡᎦᎫᏴᏛ ᏥᎩ ᎤᎩᎬ ᎬᏔᏅᎯ, ᎾᏍᎩ ᎢᎩᏍᎦᏅᏨ ᎡᎩᏙᎵᏨᎢ;
Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
15 ᎾᏍᎩ ᏣᎦᏟᎶᏍᏔᏅᎯ ᏥᎩ ᏄᏍᏛ ᎬᎪᏩᏛᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎤᏁᎳᏅᎯ, ᎾᏍᎩ ᎢᎬᏱ ᎤᏕᏅᎯ ᏥᎩ ᏂᎦᏗᏳ ᎨᎦᏁᎳᏅᎯ ᎠᏁᎲᎢ.
Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
16 ᎾᏍᎩᏰᏃ ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᏧᏬᏢᏅᎯ, ᎾᏍᎩ ᎦᎸᎳᏗ ᏤᎭ, ᎠᎴ ᎡᎶᎯ ᏤᎭ, ᎬᎪᏩᏛᏗ ᎠᎴ ᎬᎪᏩᏛᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᏥᎩ, ᎢᏳ ᎤᏂᎬᏫᏳᎯ ᏧᏂᏗᏱ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᎤᏂᎬᏫᏳᏌᏕᎩ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᎨᏥᎸᏉᏗ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᏧᎾᎵᏂᎩᏛ ᏱᎩ; ᏂᎦᏗᏳ ᏄᏓᎴᏒ ᎾᏍᎩ ᏚᏬᏢᏁᎢ, ᎠᎴ ᎤᏩᏒ ᏚᏓᏙᏢᎾᏁᎴᎢ;
Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
17 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎢᎬᏱ ᏁᎰᎢ ᎣᏂ ᏂᎦᎥ ᏧᏓᎴᏅᏛ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᏂᎬᏂᏏᎭ ᏂᎦᎥ ᎪᎱᏍᏗ ᏤᎭ;
Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
18 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏍᎪᎵ Ꭰ ᎠᏰᎸ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᎤᎾᏓᏡᎬᎢ; ᎾᏍᎩ ᏗᏓᎴᏅᏗᏍᎩ, ᏧᏓᎴᏅᏔᏅᎯ ᎤᏲᎱᏒ ᏧᎴᎯᏌᏅᎯ, ᎾᏍᎩ ᏂᎦᏗᏳ ᏄᎾᏓᎴᏒ ᎢᎬᏱ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ.
Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
19 ᎣᏏᏳᏰᏃ ᎠᏰᎸᏅᎯ ᎨᏎ ᎾᏍᎩ ᎤᏪᎯ ᎢᏳᎵᏍᏙᏗᏱ ᏂᎦᎥ ᎠᎧᎵᎢᎯ ᎨᏒᎢ;
Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
20 ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎠᎬᏗᏍᎬ ᎤᏩᏒ ᏙᎯᏱ ᎢᏳᏅᏁᏗᏱ ᏂᎦᏗᏳ ᏧᏓᎴᏅᏛ, ᎤᎩᎬ ᏓᏓᎿᎭᏩᏍᏛ ᎤᏨᏅᎯ ᎤᏬᎯᏳᏍᏔᏅ; ᎾᏍᎩ ᎠᎬᏗᏍᎬᎢ, ᎢᏳᏃ ᎡᎶᎯ ᎠᏁᎯ ᏱᎩ, ᎠᎴ ᎦᎸᎳᏗ ᎠᏁᎯ ᏱᎩ.
Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
21 ᏂᎯᏃ ᎢᎸᎯᏳ ᏁᏣᏓᎴᏉ ᏥᎨᏎᎢ, ᎠᎴ ᎡᏥᏍᎦᎩ ᏥᎨᏎ ᏙᏗᏣᏓᏅᏛᎢ ᎾᏍᎩ ᎤᏲ ᏕᏥᎸᏫᏍᏓᏁᎲᎢ ᎠᏎᏃ ᎪᎯ ᎿᎭᏉ ᎢᏦᎯᏍᏓᏁᎸ,
Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
22 ᎤᏮᏔᏅ ᎠᏰᎸ ᎤᏇᏓᎵ ᎨᏒ ᎠᏲᎱᏍᎬᎢ, ᏧᎬᏩᎴ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏨᏁᏗᏱ ᏂᏥᏍᎦᏅᎾ ᎠᎴ ᎪᎱᏍᏗ ᏁᏧᎢᏍᏛᎾ ᎠᎴ ᎦᏰᏥᎳᏫᏎᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᎾᏍᎩ ᎠᎦᏔᎲᎢ;
Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
23 ᎢᏳᏃ ᏱᏅᏩᏍᏗᏗᏉ ᎢᏦᎯᏳᏒᎢ, ᎦᎫᏍᏛᏅᎯ ᎠᎴ ᎠᏍᏓᏱᏛᎯ ᎨᏒᎢ, ᎠᎴ ᎢᏴᏛ ᎢᎦᏰᏨᏁᏗ ᏂᎨᏒᎾ ᏱᎩ ᎤᏚᎩ ᎢᏨᏒ ᎣᏍᏛ ᎧᏃᎮᏛᏱ, ᎾᏍᎩ ᎢᏣᏛᎦᏅᎯ ᏥᎩ, ᎾᏂᎥ ᎨᎦᏁᎳᏅᎯ ᎨᏒ ᎨᎦᎵᏥᏙᏁᎸᎯ ᏥᎩ ᎦᎸᎶ ᎭᏫᏂᏗᏢ ᏄᎾᏛᏅᎢ; ᎾᏍᎩ ᎾᎿᎭᎠᏴ ᏉᎳ ᎪᎱᏍᏗ ᎦᏛᏁᎯ ᏥᏅᏋᏁᎸ;
ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
24 ᎠᏴ ᎾᏍᎩ ᎪᎯ ᎨᏒ ᏥᎦᎵᎡᎵᎦ ᎢᏨᎩᎵᏲᏤᎲᎢ, ᎠᎴ ᏥᏥᎧᎵᏏᏏ ᎠᏏ ᎤᏃᏒᎢ ᎦᎶᏁᏛ ᎤᎩᎵᏲᏨ ᎾᏍᎩᏯ ᎠᎩᏇᏓᎸ ᏥᎩᎵᏲᎬᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏰᎸ ᏥᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᎭ, ᎾᏍᎩ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᎤᎾᏓᏡᎬ ᏥᎩ;
Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
25 ᎾᎿᎭᎠᏴ ᏗᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎯ ᏅᏋᏁᎸ ᎾᏍᎩᏯ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏓᏁᏤᏗ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎠᏴ ᏨᎩᏁᎸ ᏂᎯ ᎢᏣᎵᏍᏕᎸᏙᏗ, ᎾᏍᎩ ᎠᎧᎵᎢ ᎠᏆᎵᏥᏙᏗᏱ ᎧᏃᎮᏛ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏤᎵᎦ;
Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
26 ᎾᏍᎩ ᎤᏕᎵᏛ ᎬᏍᎦᎳᏅᎯ ᏥᎨᏒᎩ ᎡᏘ ᏥᎨᏒ ᎠᎴ ᎤᎾᏓᏁᏟᏴᏒᏒ ᏅᏓᎬᏩᏓᎴᏅᏛ, ᎠᏎᏃ ᎪᎯ ᏥᎩ ᎬᏂᎨᏒ ᏥᏂᎨᎬᏁᎸ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᏧᏤᎵᎦ; (aiōn g165)
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
27 ᎾᏍᎩ [ ᎤᏓᏅᏘ ] ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏚᎵᏍᎨ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏧᏩᏁᏗᏱ ᏂᎦᎥ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎨᏒ ᎯᎠ ᎾᏍᎩ ᎤᏕᎵᏛ ᎨᏒ ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ ᎠᏁᎲ [ ᎬᏂᎨᏒ ᏥᏄᏩᏁᎸ; ] ᎾᏍᎩ ᎦᎶᏁᏛ ᏥᎩ ᏂᎯ ᎢᏥᏯᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᏚᎩ ᎨᏨᏗ ᏥᏂᎬᏁ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᏗᎨᏒ ᏫᏥᎾᏄᎪᎢᏍᏗᏱ.
Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
28 ᎾᏍᎩ Ꮎ ᎬᏂᎨᏒ ᏥᏃᏨᏁᎭ, ᎾᏂᎥ ᏥᏙᏤᏯᏔᎲᏍᎦ, ᎠᎴ ᎾᏂᎥ ᏥᏙᏤᏲᎲᏍᎦ ᏦᏨᏗᎭ ᏂᎦᎥ ᎠᎵᏏᎾᎯᏍᏙᏗ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎾᏂᎥ ᎬᏂᎨᏒ ᎢᏦᏨᏁᏗᏱ ᏄᏂᎪᎸᎾ ᎦᎶᏁᏛ ᏥᏌ ᏚᎾᏁᎶᏛᎢ;
Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
29 ᎾᏍᎩ ᎾᏍᏉ ᎤᎬᏩᎵ ᏥᏓᎩᎸᏫᏍᏓᏁᎭ, ᏥᎦᏟᏂᎬᏁᎭ ᎾᏍᎩᏯ ᏧᎸᏫᏍᏓᏁᏗ ᎨᏒᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᎵᏂᎩᏗᏳ ᏥᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎭ ᏗᏆᏓᏅᏛᎢ.
Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

< ᏉᎳ ᎪᎶᏏ ᎠᏁᎯ ᏧᏬᏪᎳᏁᎸᎯ 1 >