< ᎨᏥᏅᏏᏛ ᏄᎾᏛᏁᎵᏙᎸᎢ 9 >

1 ᏐᎳᏃ ᎠᏏᏉ ᎬᏬᎳᏕᏍᎨ ᏕᎦᎾᏰᏓᏁᎮ ᎠᎴ ᏧᎯᏍᏗᏱ ᎧᏁᎨ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎬᏩᏍᏓᏩᏗᏙᎯ, ᏄᎬᏫᏳᏒ ᎠᏥᎸ-ᎨᎶᎯ ᏧᏬᎸ ᏭᎶᏎᎢ,
Pa nthawi imeneyi, Saulo ankaopsezabe okhulupirira Ambuye nafuna kuwapha. Iye anapita kwa mkulu wa ansembe,
2 ᎠᎴ ᏚᏔᏲᏎᎴ ᎪᏪᎵ ᏧᏅᏍᏗ ᏕᎹᏍᎦ ᏗᎦᏚᎲ ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ, ᎾᏍᎩᏃ ᎢᏳ ᏱᏚᏩᏛᎲ ᎩᎶ ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᏗᏂᎧᎿᎭᏩᏕᎩ, ᎠᏂᏍᎦᏯ ᎠᎴ ᎠᏂᎨᏴ, ᎾᏍᎩ ᏗᎨᎦᎸᎢᏛ ᏧᏘᏃᎯᏍᏗᏱ ᏥᎷᏏᎵᎻ.
ndi kukapempha makalata a chilolezo kuti apite nawo ku masunagoge a ku Damasiko, kuti ngati atakapezeka ena kumeneko otsata Njirayo, kaya ndi amuna kapena amayi, akawamange ndi kuwatenga kubwera nawo ku Yerusalemu.
3 ᎠᎢᏒᏃ ᏕᎹᏍᎦ ᎾᎥ ᏭᎷᏤᎢ, ᎤᏰᎶᎢᏍᏔᏁᏃ ᎢᎦᎦᏘ ᎦᎸᎳᏗ ᏅᏓᏳᎶᏒᎯ ᏚᏚᏫᏍᏔᏁᎢ.
Akuyandikira ku Damasikoku paulendo wake, mwadzidzidzi kuwala kochokera kumwamba kunamuzungulira iye.
4 ᎡᎳᏗᏃ ᎤᏅᏨ ᎤᏛᎦᏁ ᎩᎶ ᎧᏁᎬᎢ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎲᎢ; ᏐᎳ, ᏐᎳ, ᎦᏙᏃ ᎤᏲ ᏂᏍᏋᏁᎭ?
Iye anagwa pansi ndipo anamva mawu akuti, “Saulo, Saulo ukundizunziranji Ine?”
5 ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏎᎢ; ᎦᎪ ᏂᎯ, ᏣᎬᏫᏳᎯ? ᎤᎬᏫᏳᎯᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᎠᏴ ᏥᏌ ᎤᏲ ᏥᏂᏴᏁᎭ: ᎤᏕᏯᏙᏗᏳ ᏗᏣᎲᏖᏍᏗᏱ ᏗᎪᏍᏓᏯ.
Saulo anafunsa kuti, “Ndinu yani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza.”
6 ᎾᏍᎩᏃ ᎤᏪᎾᏪ ᎠᎴ ᎤᏍᏆᏂᎪᏎ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᏣᎬᏫᏳᎯ, ᎦᏙ ᏣᏚᎵ ᎠᏆᏛᏁᏗᏱ? ᎤᎬᏫᏳᎯᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎴᎢ; ᏔᎴᎲᎦ, ᏗᎦᏚᎲ ᎮᎾ, ᏓᏰᏣᏃᏁᎵᏃ ᎢᏣᏛᏁᏗᏱ.
“Tsopano dzuka, lowa mu mzindamo, ndipo udzawuzidwa zoyenera kuchita.”
7 ᎠᏁᎯᏃ ᎠᏂᏫᏅ ᏧᏅᎨᏫ ᎾᏍᎩᏯ ᏓᏂᏙᎨᎢ, ᎠᎾᏛᎩᏍᎨ ᎧᏁᎬᎢ, ᎠᏎᏃ ᎥᏝ ᎩᎶ ᏯᏂᎪᏩᏘᏍᎨᎢ.
Anthu amene anali naye paulendo, anasowa chonena; iwo anamva mawu koma sanaone wina aliyense.
8 ᏐᎳᏃ ᏕᎤᎴᏅ ᎡᎳᏗ ᎦᏅᎢ, ᎠᎴ ᏗᎦᏙᎵ ᏚᎵᏍᏚᎢᏒ ᎥᏝ ᎩᎶ ᏳᎪᎮᎢ, ᎬᏬᏱᏅᏎᏃ ᏕᎹᏍᎦ ᏫᎬᏩᏴᏔᏁᎢ.
Saulo anayimirira, ndipo pamene anatsekula maso ake sanathe kuona. Kotero anamugwira dzanja ndi kulowa naye mu Damasiko.
9 ᏦᎢᏃ ᏧᏒᎯᏛ ᎾᎪᏩᏗᏍᎬᎾ ᎨᏎᎢ, ᎠᎴ ᎾᎵᏍᏓᏴᎲᏍᎬᎾ ᎠᎴ ᎾᏗᏔᏍᎬᎾ ᎨᏎᎢ.
Anakhala wosaona kwa masiku atatu ndiponso sanadye kapena kumwa kanthu kalikonse.
10 ᎩᎶᏃ ᎢᏳᏍᏗ ᏧᏁᎶᏗ ᎡᎮ ᏕᎹᏍᎦ, ᎡᏂᎾᏯ ᏧᏙᎢᏛ; ᎾᏍᎩᏃ ᎤᏁᎳᏫᏎᎲ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎴᎢ; ᎡᏂᎾᏯ. ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏎᎢ; ᎠᏂ, ᏣᎬᏫᏳᎯ.
Ku Damasiko kunali wophunzira wina dzina lake Hananiya. Ambuye anamuyitana mʼmasomphenya kuti, “Hananiya!” Iye anayankha kuti, “Ine Ambuye.”
11 ᎯᎠᏃ ᏄᏪᏎᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ; ᏔᎴᎲᎦ, ᎮᎾ ᏗᎦᎳᏅᏛ ᎦᏥᏃᏍᏛ ᏥᏚᏙᎥ, ᏧᏓᏏᏃ ᎦᏁᎸ ᏫᏲᎦ ᏐᎳ ᏧᏙᎢᏛ ᏓᏌ ᎡᎯ. ᎬᏂᏳᏰᏃ ᎠᏓᏙᎵᏍᏗᎭ,
Ambuye anamuwuza iye kuti, “Nyamuka, pita ku nyumba ya Yudasi imene ili pa Njira Yolunjika ndipo ukafunse za munthu wochokera ku Tarisisi dzina lake Saulo, pakuti akupemphera.
12 ᎠᎴ ᎤᏁᎳᏫᏎᎲ ᎤᎪᎲ ᎠᏍᎦᏯ ᎡᏂᎾᏯ ᏧᏙᎢᏛ ᎤᏴᎵᎸ ᎠᎴ ᎤᏏᏔᏛ ᎥᎤᎪᏩᏛᏗᏱ.
Ndipo waona mʼmasomphenya munthu, dzina lake Hananiya atabwera ndi kumusanjika manja kuti aonenso.”
13 ᎡᏂᎾᏯᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᏣᎬᏫᏳᎯ, ᏥᏯᏛᎦᏁᎸ ᎯᎠ ᎠᏍᎦᏯ ᎤᏂᏣᏔ ᎬᎩᏃᏁᎸ ᎤᏣᏘ ᎤᏲ ᏂᏚᏩᏁᎸ ᏗᏣᏤᎵ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᏥᎷᏏᎵᎻ.
Hananiya anayankha kuti, “Ambuye, ndinamva zambiri za munthu uyu ndi zonse zoyipa anachitira oyera mtima a ku Yerusalemu.
14 ᎠᏂᏃ ᎤᎭ ᎬᏩᏁᏤᎸᎯ ᏄᏂᎬᏫᏳᏒ ᎠᏥᎸ-ᎠᏁᎶᎯ ᏧᎸᏍᏗᏱ ᏂᎦᏛ ᏕᏣᏙᎥ ᎠᏂᏁᎢᏍᏗᏍᎩ.
Ndipo wabwera kuno ndi ulamuliro wa akulu ansembe kuti adzamange onse amene amayitana pa dzina lanu.”
15 ᎠᏎᏃ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎴᎢ; ᎮᎾ, ᎾᏍᎩᏰᏃ ᏥᏯᏑᏰᏛ ᎠᏖᎵᏙ ᎠᏆᏤᎵᎦ ᏓᏆᏙᎥ ᎠᏱᏙᎯ ᎠᏂᎦᏔᎲ ᏧᎾᏓᎴᏅᏛ ᏴᏫ ᎠᎴ ᎤᏂᎬᏫᏳᎯ ᎠᎴ ᎢᏏᎵ ᏧᏪᏥ.
Koma Ambuye anati kwa Hananiya, “Pita! Munthu uyu ndi chida changa chosankhika chonyamulira dzina langa pamaso pa anthu a mitundu ina ndi mafumu awo ndiponso kwa anthu a Israeli.
16 ᎬᏂᎨᏒᏰᏃ ᏅᏓᏥᏴᏁᎵ ᏄᏣᏛ ᎠᏎ ᎤᎩᎵᏲᎢᏍᏗᏱ ᏓᏆᏙᎥ ᏅᏗᎦᎵᏍᏙᏗᏍᎬᎢ.
Ine ndidzamuonetsa zowawa zonse zimene ayenera kumva chifukwa cha dzina langa.”
17 ᎡᏂᎾᏯᏃ ᎤᏪᏅᏎᎢ, ᎠᎴ ᎠᏓᏁᎸ ᎤᏴᎴᎢ, ᏚᏏᏔᏛᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎢ; ᏐᎳ ᎥᎩᏅᏟ, ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ, ᎾᏍᎩ ᎬᏂᎨᏒ ᏥᏂᏣᏛᏁᎴ ᏔᎢᏒᎢ ᏗᎩᏅᏒ ᎥᏣᎪᏩᏛᏗᏱ ᎠᎴ ᏣᎧᎵᎢᏍᏗᏱ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ.
Pamenepo Hananiya ananyamuka ndi kukalowa mʼnyumbayo. Anamusanjika manja Sauloyo ndipo anati, “Mʼbale Saulo, Ambuye Yesu, amene anakuonekera pa msewu pamene umabwera kuno wandituma kuti uwonenso ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.”
18 ᎩᎳᏉᏃ ᎢᏴᏛ ᏚᎦᏔᏅᎪᎠᏎ ᎤᏩᏥᏍᎦᎸ ᎢᏳᏍᏗ, ᎠᎴ ᎩᎳᏉ ᎢᏴᏛ ᎬᏩᎪᏩᏛᏗ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ; ᏚᎴᏅᏃ ᎠᎦᏬᎡᎢ.
Nthawi yomweyo mʼmaso mwa Saulo munachoka zinthu zokhala ngati mamba ansomba, ndipo anayambanso kuona. Iye anayimirira nabatizidwa,
19 ᎤᎵᏍᏓᏴᏅᏃ ᎤᎵᏂᎪᏎᎢ. ᏐᎳᏃ ᎢᎸᏍᎩ ᏧᏒᎯᏛ ᏚᏪᎳᏗᏙᎴ ᎠᏃᎯᏳᎲᏍᎩ ᏕᎹᏍᎦ ᎠᏁᎯ.
ndipo atadya chakudya, anapezanso mphamvu. Saulo anakhala masiku angapo ndi ophunzira a ku Damasiko.
20 ᎢᎬᏪᏅᏛᏃ ᏗᎦᎳᏫᎢᏍᏗᏱ ᏕᎪᏢᏩᏗᏒ ᎤᎵᏥᏙᏁᎢ, ᎤᏃᎮᎴ ᎦᎶᏁᏛ ᎾᏍᎩ ᎤᏁᎳᏅᎯ ᎤᏪᏥ ᎨᏒᎢ.
Posakhalitsa anayamba kulalikira mʼsunagoge kuti Yesu ndiye Mwana wa Mulungu.
21 ᏂᎦᏛᏃ ᎤᎾᏛᎦᏅᎯ ᎤᏂᏍᏆᏂᎪᏎᎢ, ᎠᎴ ᎯᎠ ᏄᏂᏪᏎᎢ; ᏝᏍᎪ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᏱᎩ ᏥᏓᎩᎵᏲᎢᏍᏙᏗᏍᎬ ᏥᎷᏏᎵᎻ ᎯᎠ ᏕᏅᏙᎥ ᎠᏂᏁᎢᏍᏗᏍᎩ? ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎢᏳᏍᏗ ᎠᏂ ᎤᎷᏨᎩ, ᎾᏍᎩ ᏧᎸᏍᏗ ᏫᏚᏘᏃᎮᏗᏱ ᏄᏂᎬᏫᏳᏒ ᎠᏥᎸ-ᎠᏁᎶᎯ.
Onse amene anamva iye akulalikira anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene anayambitsa kuzunza okhulupirira ku mpingo wa ku Yerusalemu? Kodi siwabwera kuno kuti awamange ndi kuwapereka kwa akulu a ansembe?”
22 ᎠᏎᏃ ᏐᎳ ᎧᏁᏉᎨᏉ ᎤᎵᏂᎪᏍᎬᎢ, ᎠᎴ ᎠᏂᏬᏂᏍᎬ ᏚᎪᎾᏛᏔᏁ ᎠᏂᏧᏏ ᏕᎹᏍᎦ ᎠᏁᎯ, ᎬᏂᎨᏒ ᏂᎬᏁᎮ ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎦᎶᏁᏛ ᎨᏒᎢ.
Koma mphamvu za Saulo zinali kukulirakulira ndipo anathetsa nzeru Ayuda okhala ku Damasiko powatsimikizira kuti Yesu ndi Mpulumutsi.
23 ᏰᎵᏃ ᎤᏬᎯᏨ ᎠᏂᏧᏏ ᎤᏂᏃᎮᎴ ᎤᏂᎯᏍᏗᏱ.
Patapita masiku ambiri, Ayuda anapangana zoti aphe Saulo,
24 ᎠᏎᏃ ᎾᏍᎩ ᏚᏄᎪᏔᏅᎢ ᎤᏛᎦᏁ ᏐᎳ. ᏂᎪᎯᎸᏃ ᎢᎦ ᎠᎴ ᏒᏃᏱ ᏗᎦᎶᎯᏍᏗᏱ ᏚᏂᎭᎷᏁ ᎤᏂᎯᏍᏗᏱ.
koma iye anadziwa za chiwembucho. Anthu ankadikirira usana ndi usiku pa zipata za mzindawo kuti amuphe.
25 ᎠᏎᏃ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᎤᏂᏯᏅᎮ ᏒᏃᏱ ᎠᎴ ᏔᎷᏣ ᎤᏂᏲᏔᏁ ᎤᎾᏠᎥᏔᏁ ᎠᏐᏴᎢ.
Koma ophunzira ake anamutenga usiku, namutsitsira kunja kwa mpandawo mʼdengu.
26 ᏐᎳᏃ ᏥᎷᏏᎵᎻ ᎤᎷᏨ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᏧᎵᎪᏁᏗᏱ ᎤᏰᎸᏁᎢ. ᏂᎦᏛᏃ ᎬᏩᏍᎦᎢᎮᎢ, ᎠᎴ ᎥᏝ ᏯᏃᎯᏳᎲᏍᎨ ᏧᏁᎶᏗ ᎨᏒᎢ.
Saulo atafika ku Yerusalemu, anayesetsa kulowa mʼgulu la ophunzira koma onse anamuopa chifukwa sanakhulupirire kuti anali wophunziradi.
27 ᎠᏎᏃ ᏆᏂᏆ ᏭᏯᏅᎲ ᏚᏘᏃᎮᎴ ᎨᏥᏅᏏᏛ, ᎠᎴ ᏚᏃᏁᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎤᎪᎲᎢ ᎠᎢᏒᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎩ ᎤᏬᏁᏔᏅᎢ, ᎠᎴ ᎾᏍᎦᎢᎲᎾ ᏥᏌ ᏕᎤᏙᎥ ᎤᏁᎢᏍᏔᏅᎢ ᏕᎹᏍᎦ.
Koma Barnaba anamutenga napita naye kwa atumwi. Iye anawafotokozera iwo za mmene Saulo anaonera Ambuye pa njira paja, ndi kuti Ambuye anamuyankhula, ndi momwe analalikira ku Damasiko mʼdzina la Yesu mosaopa.
28 ᎾᏍᎩᏃ ᎢᏧᎳᎭ ᎠᏁᏙᎮ ᏥᎷᏏᎵᎻ.
Kotero Saulo anakhala nawo nayendayenda mwaufulu mu Yerusalemu akulalikira molimba mtima mʼdzina la Ambuye.
29 ᎾᏍᎦᎢᎲᎾᏃ ᎧᏁᎢᏍᏗᏍᎨ ᏕᎤᏙᎥ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᏥᏌ, ᎠᎴ ᎠᏂᎪᎢ ᎤᏂᏬᏂᏍᏗ ᎠᏂᏬᏂᏍᎩ ᎠᎾᏗᏒᎯᎮ ᎠᏂᏬᏂᏍᎬᎢ. ᎠᏎᏃ ᎤᎾᏁᎶᏔᏁ ᎬᏩᎯᏍᏗᏱ.
Anayankhula ndi kutsutsana ndi Ayuda a Chihelene, koma iwo ankafuna kumupha.
30 ᎠᎾᎵᏅᏟᏍᎩᏂ ᎾᏍᎩ ᎤᎾᏛᎦᏅ, ᏏᏌᎵᏱ ᏭᎾᏘᏃᎴᎢ, ᎿᎭᏉᏃ ᏓᏌ ᏭᏂᏅᏎᎢ.
Abale atadziwa zimenezi, anamutenga Saulo ndi kupita naye ku Kaisareya, ndipo anamutumiza ku Tarisisi.
31 ᎿᎭᏉᏃ ᏧᎾᏁᎶᏗ ᎤᎾᏓᏡ Ꭼ ᏅᏩᏙᎯᏯᏛ ᏄᎾᎵᏍᏓᏁᎴ ᏂᎬᎾᏛ ᏧᏗᏱ ᎠᎴ ᎨᎵᎵ ᎠᎴ ᏌᎺᎵᏱ, ᎠᎴ ᎨᎦᎵᏂᎪᎯᏍᏔᏁᎢ, ᎠᎴ ᎠᎾᎢᏎ ᎾᎿᎭᎦᎾᏰᎯᏍᏗ ᎨᏒ ᎤᎬᏫᏳᎯ, ᎠᎴ ᎣᏍᏛ ᎤᏂᎦᎵᏍᏓᏗᏍᎬ ᎦᎸᏉᏗᏳ ᎠᏓᏅᏙ, ᎠᏂᏁᏉᎨᎢ.
Pamenepo mpingo wa ku Yudeya konse, ku Galileya ndi ku Samariya unakhala pamtendere, unalimbikitsidwa; ndi kupatsidwa mphamvu ndi Mzimu Woyera, unakula mʼchiwerengero, ndi kukhala moopa Ambuye.
32 ᎯᎠᏃ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᏈᏓ ᏂᎬᎾᏛ ᎤᏪᏙᎸ ᎾᏍᏉ ᏫᏚᎷᏤᎴ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎵᏓ ᎠᏁᎯ.
Pamene Petro amayendera mpingo, anapita kukachezera oyera mtima a ku Luda.
33 ᎾᎿᎭᏃ ᎤᏩᏛᎮ ᎩᎶ ᎢᏳᏍᏗ ᎠᏍᎦᏯ ᎢᏂᏯ ᏧᏙᎢᏛ, ᏧᏁᎳ ᎢᏧᏕᏘᏴᏛ ᎬᏩᏂᏏᏅᎯ ᎨᏎ ᎦᏂᏟ ᎤᎸᏓᎸᎥᏍᎨᎢ.
Kumeneko anakapeza munthu dzina lake Eneya, wofa ziwalo amene anagona pa mphasa kwa zaka zisanu ndi zitatu.
34 ᏈᏓᏃ ᎯᎠ ᏄᏪᏎᎴ ᎾᏍᎩ; ᎢᏂᏯ, ᏥᏌ ᎦᎶᏁᏛ ᏣᏅᏮᎦ; ᏔᎴᎲᎦ, ᎠᎴ ᎯᏰᏍᏛᎢᏌ ᏣᏂᏏᏗᏱ. ᎩᎳᏉᏃ ᎢᏴᏛ ᏚᎴᏁᎢ.
Petro anati kwa iye, “Eneya, Yesu Khristu akukuchiritsa iwe, dzuka ndipo yalula mphasa yako.” Nthawi yomweyo Eneya anayimirira.
35 ᏂᎦᏛᏃ ᎵᏓ ᎠᎴ ᏎᎶᏂ ᎠᏁᎯ ᎬᏩᎪᎮᎢ, ᎠᎴ ᎤᎬᏫᏳᎯ ᎢᏗᏢ ᏭᎾᎦᏔᎲᏍᏔᏁᎢ.
Anthu onse amene anakhala ku Luda ndi ku Sharoni anamuona ndipo anatembenukira kwa Ambuye.
36 ᏦᏈᏃ ᎡᎮ ᎩᎶ ᎢᏳᏍᏗ ᎠᎨᏴ ᏧᏁᎶᏗ, ᏓᏈᏗ ᏧᏙᎢᏛ, ᎾᏍᎩ ᎠᏁᏢᏔᏅᎯ ᏓᎩ ᎦᏛᎦ, ᎾᏍᎩ ᎯᎠ ᎤᎧᎵᏨᎯ ᎨᏎ ᎣᏍᏛ ᏚᎸᏫᏍᏓᏁᎲᎢ ᎠᎴ ᎠᏓᏁᎸᎥᏍᎬᎢ.
Ku Yopa kunali wophunzira wina dzina lake Tabita (mʼChigriki amati Dorika) amene nthawi zonse ankachita zachifundo ndiponso kuthandiza osauka.
37 ᎯᎠᏃ ᏄᎵᏍᏔᏁ ᎾᎯᏳᎢ, ᎾᏍᎩ ᎤᏢᏨ ᎤᏲᎱᏎᎢ, ᎾᏍᎩᏃ ᎤᎾᏬᎥ ᎦᎸᎳᏗ ᎧᏅᏑᎸ ᎤᏂᏅᏁᎢ.
Nthawi imeneyi anadwala ndipo anamwalira, anasambitsa thupi lake, namugoneka mʼchipinda chammwamba.
38 ᎵᏓᏃ ᎠᎴ ᏦᏈ ᎾᎥ ᏂᏚᏓᎴᎢ, ᎠᏃᎯᏳᎲᏍᎩᏃ ᎤᎾᏛᎦᏅ ᏈᏓ ᎡᏙᎲ ᎵᏓ, ᎠᏂᏔᎵ ᎠᏂᏍᎦᏯ ᏚᏂᏅᏎ ᏭᏂᏔᏲᏎᏗᏱ ᎤᏙᎯᏗᏍᏗᏱ ᏂᎨᏒᎾ ᏂᏙᏓᏳᏩᏛᎲᏍᏗᏱ.
Popeza ku Yopa kunali pafupi ndi Luda; pamene ophunzira anamva kuti Petro anali ku Luda, anatuma anthu awiri kuti akamudandaulire kuti, “Chonde bwerani kuno msanga!”
39 ᏈᏓᏃ ᏚᎴᏅ ᏚᏍᏓᏩᏛᏎᎢ; ᎤᎷᏨᏃ ᎦᎸᎳᏗ ᎧᏅᏑᎸ ᏫᎬᏩᏴᏔᏁᎢ; ᏂᎦᏛᏃ ᎠᏂᎨᏴ ᏧᏃᏑᎶᏨᎯ ᎦᏙᎬ ᎾᎥ ᎠᏂᏙᎾᎡ ᏓᏂᏴᎨᎢ, ᎠᎴ ᏓᏂᎾᏄᎪᏫᏍᎨ ᎭᏫᏂ ᏗᏄᏬ ᎠᎴ ᏧᏓᎴᏅᏛ ᏗᏄᏬ ᎾᏍᎩ ᏓᎩ ᏧᏪᏰᏫᏒᎯ ᎠᏏ ᎤᏁᎳᏗᏙᎮᎢ.
Petro ananyamuka, napita nawo, ndipo atafika anamutengera ku chipinda chammwamba. Amasiye onse anayima momuzungulira akulira ndi kumuonetsa mwinjiro ndi zovala zina zimene Dorika ankapanga akanali moyo.
40 ᏈᏓᏃ ᏂᎦᏛ ᏚᏄᎪᏫᏒ ᏚᎵᏂᏆᏅᏁ ᎠᎴ ᎤᏓᏙᎵᏍᏔᏁᎢ, ᏕᏛᏅᏃ ᎢᏗᏢ ᏭᎦᏔᎲᏍᏔᏅ, ᏓᏈᏗ ᏔᎴᎲᎦ, ᎤᏛᏁᎢ. ᏚᏍᏚᎢᏎᏃ ᏗᎦᏙᎵ, ᏈᏓᏃ ᎤᎪᎲ, ᎤᏗᏛᎮ ᎤᏪᏁᎢ.
Petro anatulutsa anthu onse mʼchipindamo; ndipo anagwada pansi ndi kupemphera. Anatembenukira mtembo uja nati, “Tabita, dzuka,” Tabita anatsekula maso ake, ndipo ataona Petro anakhala pansi.
41 ᎤᏬᏯᏁᏒᏃ ᏕᎤᎴᏔᏁᎢ; ᏫᏚᏯᏅᎲᏃ ᎤᎾᏓᏅᏘ ᎠᎴ ᏧᏃᏑᎶᏨᎯ, ᏕᎤᎾᏄᎪᏫᏎᎴ ᎬᏃᏛ.
Petro anamugwira dzanja, namuyimiritsa. Ndipo anayitana okhulupirira ndi amasiye namupereka wamoyo.
42 ᏦᏈᏃ ᏂᎬᎾᏛ ᎤᎾᏛᎦᏁᎢ, ᎠᎴ ᎤᏂᏣᏖ ᎤᏃᎯᏳᏁ ᎤᎬᏫᏳᎯ.
Zimenezi zinadziwika ku Yopa konse, ndipo anthu ambiri anakhulupirira Ambuye.
43 ᎯᎠᏃ ᏄᎵᏍᏔᏁᎢ, ᏰᎵ ᎤᏬᎯᏤ ᎤᏕᏁ ᏦᏈ, ᏗᏑᏫᏍᎩ ᏌᏩᏂ ᏧᏙᎢᏛ ᎦᏁᎸᎢ.
Petro anakhala ku Yopa kwa masiku ambiri kwa munthu wina, dzina lake Simoni, mmisiri wa zikopa.

< ᎨᏥᏅᏏᏛ ᏄᎾᏛᏁᎵᏙᎸᎢ 9 >