< Lucas 9 >

1 Y araquerando a os duideque Apostoles, les diñó silo y potestad, opré sares os bengues, y que chibelasen lacho merdipénes.
Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda.
2 Y os bichabó á garlar o chim de Debél, y á chibar lacho os merdes.
Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala.
3 Y les penó: Na lliguereles chichi para o drun, ni cáste, ni manroña, ni manro, ni jayere, ni tereleis dui coneles.
Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera.
4 Y saro quer andré que chalareis oté permaneced, y na chaleis abrí de oté.
Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo.
5 Y sares junos sos na ustilasen sangue: al chalar abrí de ocola foros, bucharelad o pracos de jires pindrés andré machiria contra junos.
Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.”
6 Y chalando abrí, guillaban de gau andré gau, garlando ó Evangelio, y chibando lacho por sarias aricatas.
Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.
7 Y bigoreó á as canes de Herodes o Tetrarcha o saro sos querelaba Jesus, y peró andré zibó, presas penaban
Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa,
8 Yeques: Que Juan ha ardiñado de enrun os mules: y averes: Que Elias habia abillado: y averes: Que yeque propheta es pures habia ardiñado.
ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.
9 Y penó Herodes: Menda amulé á Juan: ¿Coin pues sinela ocona, de coin junelo tales buchias? Y camelaba dicarlo.
Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.
10 Y limbiados os Apostoles, le penáron o saro sos terelaban querdi: y ustilandolos sat o aparte, se chaló á yeque stano desierto, sos sinela del chim de Bethsaidá.
Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida.
11 Y pur os manuces lo chaneláron, lo plastañáron: Y Jesus os ustiló, y les chamuliaba del chim de Debél, y chibaba mistos á junos sos lo terelaban menester.
Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.
12 Y o chibes se habia chibado á bejelarse: pur bigoreandose á ó os duideque, le penáron: Bichaba á ocona sueti, somia que chalen á os gaues, y sosias sunparal, se chibelen á sobelar, y alachalen que jamar: presas acoi sinamos andré yeque desierto.
Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”
13 Y les penó: Diñadles sangue de jamar: y junos penáron: Na terelamos butér de pansch manres y dui maches: á no sinar que mu chalamos á quinar jachipen para sari ocona sueti.
Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.” Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.”
14 Presas sinaban sasta yeques pansch jazare manuces. Y ó penó á desqueres discipules: Quereladlos bestelar andré plastañias de cincuenta en cincuenta.
(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000). Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.”
15 Y andiar lo quereláron: y os sares se besteláron.
Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi.
16 Y ustilando os pansch manres, y os dui maches, ardiñó as aquias al Tarpé, os majarificó, y asparabó: y diñó á desqueres discipules, somia que os childasen anglal de la sueti.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu.
17 Y jamáron os sares, y se pereláron. Y ustiláron ma les sobró, duideque cornichas de cotores.
Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.
18 Y anacó, que sinando ó colcoro bedando, se alachaban sat ó desqueres discipules: y os puchabó, y penó: ¿Coin penela a sueti que sinela menda?
Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
19 Y junos rudeláron, y penáron: Juan o Bautista, y averes Elias, y averes que se ardiñó yeque es purés Prophetas.
Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”
20 Y les penó: ¿Y sangue coin penelais, que sinelo menda? Rudelando Simon Pedro, penó: O Christo de Debél.
Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”
21 O yescotria os amenazó, y penó, que na lo penasen á cayque,
Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi.
22 Penandoles: Jomte, que o Chaboro e Manu padezca baribustrias buchias, y que sinele desechado de los purés, y de los Manclayes es erajais, y de los libanés: y que sinele diñado á la meripen, y que ardiñele al trino chibes.
Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”
23 Y penaba á sares: O sos palal de mangue camela abillar, nieguese á sí matejo, y ustile desquero trijul saro chibes, y plastañe mangue.
Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine.
24 Presas ó sos camelare salvar, desqueri ochi, a najará: y o manu sos najare desqueri ochi por camelar mangue la alachará.
Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa.
25 ¿Presas que aprovechasarela á yeque manu, si ustilare sari a chiquen, y si najela ó á sí matejo, y se caquerela á sí matejo?
Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini?
26 Presas ó sos se afrentare de mangue, y de minrias vardas, se afrentará de ó o Chaboro e Manu, pur abillará sat desquero chimusolano, y sat o del Dada, y es majarés Manfarieles.
Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera.
27 Tami penelo sangue en chachipen: que yeques sinelan acoi, sos na penchararán meripen, disde que diquelen o chim de Debél.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”
28 Y anacó sasta otor chibases despues de oconas vardas, que ustiló sat ó á Pedro, y á Santiago, y á Juan, y costunó á yeque bur á manguelar á Un-debél.
Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera.
29 Y o chiros que manguelaba, a figura de desqueri chiché se quereló aver: y os talarores de ó se tornáron parnes, y resplandecientes.
Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri.
30 Y he acoi que chamuliaban sat ó dui gaches. Y oconas sinaban Moysés y Elias,
Anthu awiri, Mose ndi Eliya,
31 Que se mequeláron dicar andré chimusolano: y chamuliaban de la meripen de ó, sos terelaba de cumplir andré Jerusalém.
anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu.
32 Tami Pedro, y junos sos sat ó sinaban, se alachaban cargados de sobindoi; y ostinando dicáron o chimusolano de Jesus, y á os dui gaches, sos sinaban sat ó.
Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye.
33 Y pur se chaláron de ó, penó Pedro á Jesus: Duquendio, mistos sinela que mu sinelemos acoi: y querelemos trin estañas, yeque para tucue, y yeque para Moysés, y aver para Elias, na chanelando, ma se penelaba.
Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).
34 Y pur sinaba ó penando ocono, abilló yeque paros, y os ucharó: y tereláron dal, sinando junos andré o paros.
Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta.
35 Y abilló gole baro abrí e paros, penando: Ocona sinela minrio Chaboro camelado; junelad á ó.
Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.”
36 Y al chalar abrí ocona gole, alacháron colcoro á Jesus; y junos se sonsibeláron, y á cayque penáron andré ocolas chibeses chichi, de o saro que terelaban dicado.
Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.
37 Y aver chibes pejando junos del bur, les abilló á rachelar plastañi bari de sueti.
Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye.
38 Y he acoi yeque manu de la plastañi garló, penando: Duquendio, manguelo tucue, que diqueles a minrio chaboro, presas menda na terelo aver.
Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu.
39 Y he acoi que yeque bengui le ustilela, y yescotria díñela goles; y le bucharela por chiquen, y le asparabela querelandole chibar abrí espuma, y na camela chalar de ó, lliguerandole.
Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga.
40 Y manguelé á tires discipules, que ó bucharasen abrí, y na astisáron.
Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”
41 Y rudelando Jesus, penó: O rati infiel y chori! ¿disde pur sinará con-a-sangue, y sangue urjiyaré? Lanela acoi tun chaboro.
Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”
42 Y pur abilló sunparal, le bucharó o bengui en chiquen, y le caqueró.
Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake.
43 Tami Jesus chamulió al bengui chindó, y chibó lacho al bedoro, y se le diñó á desquero batu.
Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu. Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake,
44 Y se darañelaban sares de la sila bari de Debél: y zibandose sares de sarias as buchias sos querelaba, penó á desqueres discipules: Chibelad andré jires carlés oconas vardas: Jomte que o Chaboro e manu sinele chibado andré bastes es manuces.
“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”
45 Tami junos na jabilláron ocona varda, y les sinaba tan oruni, que na le chanelaban: y darañelaban de puchararle acerca de siró.
Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.
46 Y les abilló tambien a jestia, coin de junos sinaria o fetér.
Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo.
47 Tami Jesus dicando ma penchababan andré desqueres carlés, ustiló yeque chaboro, y lo childó sunparal á sí,
Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake.
48 Y les penó: O sos ustilare á ocona chaboro andré minrio nao, á mangue ustilela: y o saro sos á mangue ustilare, ustilela á ocola, sos mangue bichabó: presas ó sos sinela mendesquero andré sangue sares, ocona sinela o mas baro.
Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”
49 Entonces Juan ustilando a varda, penó: Duquendio, hemos dicado a yeque bucharando abrí os bengues andré tiro nao, y se lo nicobelamos: presas na te plastañela con amangue.
Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”
50 Y Jesus le penó: Na se lo nicobeleis, presas ó sos na sinela contra sangue, por sangue sinela.
Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”
51 Y sasta se abillase sunparal o chiros de desquero Asuncion, quereló silno semblante de chalar á Jerusalém.
Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu,
52 Y bichabó anglal de ó manuces: junos nacáron, y chaláron andré yeque gau es Samaritanes, somia orotarle mesuna.
ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira,
53 Y na le ustiláron, presas quereló semblante de chalar á Jerusalém.
koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu.
54 Y pur lo dicáron Santiago, y Juan discipules de ó, penáron: Erañó: camelas que penelemos, que perele yaque del Charos, y los marele.
Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?”
55 Tami ó, boltañandose acia junos, os chingaró, penando: Na chanelais de que suncai sinelais.
Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula,
56 O chaboro e manu na ha abillado á marelar ochias, sino á listrabarlas. Y se nacáron á aver gau.
ndipo iwo anapita ku mudzi wina.
57 Y anacó que chalando junos por o drun, penó yeque á Jesus: Menda plastañaré tucue aduque que chalares.
Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”
58 Jesus le penó: Os rubasunches terelan turnias, y as pulias e Charos nidos: tami o chaboro e manu na terela duque chibelar o jero.
Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”
59 Y á aver penó: Plastañamangue. Y ó rudeló: Erañó, mejelamangue chalar antes á garabar á minrio batu.
Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.” Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”
60 Y Jesus le penó: Mequela que os mules garaben á desqueres mulés: tami tucue abillel, y pucana o chim de Debél.
Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”
61 Y aver le penó: Plastañaré tucue Erañó: tami brotobo mequelamangue chalar á chitar mistos ma terelo andré minrio quer.
Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”
62 Jesus le penó: Cayque, sos chibela baste andré o caste randiñador, y diquela palal, sinela lacho somia o chim de Debél.
Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”

< Lucas 9 >