< Lucas 5 >

1 Y anacó que abillando a sueti en plastañías somia junelar a varda de Debél, sinaba ó á la cunara de la pani de Genesareth.
Tsiku lina Yesu anayima mʼmbali mwa nyanja ya Genesareti, gulu la anthu litamuzungulira likumvetsera mawu a Mulungu.
2 Y dicó dui berdés, sos sinaban á la cunara de la pani: y os machadores habian ardiñado en chiquen, y muchobelaban desqueres redes.
Iye anaona mabwato awiri ali mʼmphepete mwa nyanja, asodzi amene ankachapa makhoka awo atawasiya pamenepo.
3 Y chalando andré yeque de oconas berdés, sos sinaba de Simon, le mangó, que le guillase yeque fremi de la chiquen. Y sinando bestelado, bedaba á la sueti desde o berdo.
Iye analowa mʼbwato limodzi limene linali la Simoni, ndi kumupempha kuti alikankhire mʼkati mwa nyanja pangʼono. Kenaka Iye anakhala pansi nayamba kuphunzitsa anthu ali mʼbwatomo.
4 Y yescotria que acabó de chamuliar, penó á Simon: Chala butér andré, y chibela jires redes somia machorar.
Atatha kuyankhula anati kwa Simoni, “Kankhirani kwa kuya ndipo muponye makhoka kuti mugwire nsomba.”
5 Y rudelando Simon, le penó: Duquendio, sari a rachi hemos sinado machorando, bi ustilar chichi: tami en tiri varda chibaré a red.
Simoni anayankha kuti, “Ambuye, tagwira ntchito molimbika usiku wonse, koma sitinagwire kanthu. Koma pakuti mwatero, ndiponya makhoka.”
6 Y pur tereláron querdi ocolo, ustiláron tan baró numero de maches, que se asparababa a red de junos.
Atachita izi, anagwira nsomba zambiri kotero kuti makhoka awo anayamba kungʼambika.
7 Y quereláron simaches á os averes manuces sos sinaban andré o aver berdo, somia que abillasen á ayudarlos. Ocolas abilláron, y de tal beda pereláron os dui berdes, que casi chalaban abajines.
Choncho anakodola anzawo a bwato linalo kuti abwere ndi kuwathandiza, ndipo anabwera nadzaza mabwato onse awiri mpaka kuyamba kumira.
8 Y pur dicó Simon Pedro ocolo, se chibó á os pindrés de Jesus, penando: Erañó, chatucue de mangue, que sinelo manu choro.
Simoni Petro ataona izi, anagwa pa mawondo a Yesu nati, “Chokani kwa ine Ambuye: Ine ndine munthu wochimwa!”
9 Presas ó, y os sares sos sat ó sinaban, sináron atonitos de os butres maches, que terelaban ustilado:
Iye ndi anzake onse anadabwa ndi nsomba zimene anagwira,
10 Yandiar matejo Santiago, y Juan, chabores del Zebedéo, sos sinaban candones de Simon: Y penó Jesus á Simon: Na darañeles: desde ocona chiros sinarás machador de manuces.
chimodzimodzinso Yakobo ndi Yohane, ana a Zebedayo, anzake a Simoniyo. Kenaka Yesu anati kwa Simoni, “Musachite mantha; kuyambira tsopano ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
11 Y lliguerando os berdes á chiquen, mequeláron o saro, y le plastañáron.
Kenaka anakokera mabwato awo ku mtunda, nasiya zonse namutsata Iye.
12 Y anacó, que sinando andré yeque de ocolas fores, abilló manu perelalo de zarapia, y pur dicó á Jesus, se chibó mui por chiquen, y le mangó, penando: Erañó, si camelas, astisarelas chibarme lacho.
Yesu ali ku mudzi wina, munthu amene anali ndi khate thupi lonse anabwera kwa Iye. Munthuyo ataona Yesu, anagwa chafufumimba ndipo anamupempha Iye kuti, “Ambuye, ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
13 Y ó bucharando la baste le pajabó, penando: Camelo: sinele limpio. Y yescotria chaló de ó a zarapia.
Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo. Iye anati, “Ine ndikufuna, yeretsedwa!” Ndipo nthawi yomweyo khate lake linachoka.
14 Y le penó, que na lo penase á cayque: Tami chatucue, le penó, y muestrate al erajai, y díñela por tiri limpieza ma mandó Moyses, en machiria á junos.
Kenaka Yesu anamulamula kuti, “Usawuze wina aliyense, koma pita, kadzionetse kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose anakulamulirani za kuyeretsedwa kwanu monga umboni kwa iwo.”
15 Y trincho butér se voltisaraba desquero chimusolano: y abillaba en plastañias a sueti somia junelarle, y somia que nicobelase de junos desqueres merdipénes.
Koma mbiri yake inafalikirabe kwambiri kotero kuti magulu a anthu anabwera kudzamvetsera ndi kuti achiritsidwe ku matenda awo.
16 Tami ó se chaló al desierto á manguelar á Un-debél.
Koma Yesu nthawi zambiri ankachoka kupita ku malo a yekha kukapemphera.
17 Y anacó, que yeque chibes ó sinaba bestelado bedando. Y sinaban tambien bestelados oté yeques Phariseyes, y Chandés de la Eschastra, sos abilláron de sares os gaues e Galiléa, y de Judéa, y de Jerusalém: y a sila e Erañoro sinaba randiñando somia chibarlos lacho.
Tsiku lina pamene ankaphunzitsa, Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, amene anachokera ku midzi yonse ya Galileya ndi ku Yudeya ndi Yerusalemu, anakhala pansi pomwepo. Ndipo mphamvu ya Ambuye inalipo yakuti Iye achiritse odwala.
18 Y abilláron yeques manuces sos ligueraban opré cheripen yeque manu, sos sinaba paralitico, y le camelaban sinchitar andré, y chibarle anglal de ó.
Amuna ena anabwera atanyamula munthu wofa ziwalo pa mphasa ndipo anayesa kumulowetsa mʼnyumba kuti amugoneke pamaso pa Yesu.
19 Tami na rachelando por anduque astisar sinchitarlo por la plastañi e sueti, costunáron opré o techo y pre ó tejado le deschindaron sat a cheripen, sinchitandolo en medio anglal de Jesus.
Atalephera kupeza njira yochitira zimenezi chifukwa cha gulu la anthu, anakwera naye pa denga ali pa mphasa pomwepo ndi kumutsitsira mʼkati pakati pa gulu la anthu, patsogolo penipeni pa Yesu.
20 Y pur dicó a fé de junos, penó: Manu, ertinados á tucue sinelan os grecos.
Yesu ataona chikhulupiriro chawo, anati, “Mnzanga, machimo ako akhululukidwa.”
21 Y os Libanes, y Phariseyes se chibaron á penchabar, y penar: ¿Coin sinela ocona sos chamulia solajais: Coin astisarela ertinar grecos, sino Un-debél colcoro?
Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anayamba kuganiza mwa iwo okha kuti, “Kodi munthu uyu ndi ndani amene ayankhula zamwano? Kodi ndani amene angakhululukire machimo kupatula Mulungu?”
22 Y Jesus, sasta jabilló as suncais de junos, les rudeló, y penó: ¿Qué penchabais andré jirés carlochines?
Yesu anadziwa zomwe iwo amaganiza ndipo anafunsa kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukuganiza zimenezi mʼmitima mwanu?
23 ¿Qué sinela mas astis, penar: Ertinados á tucue sinelan os grecos; o penar: Costunate y pirela?
Kodi chapafupi ndi chiti: kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa,’ kapena kunena kuti, ‘Nyamuka ndipo yenda?’”
24 Pues somia que chaneleis, que o Chaboro e manu terela sila opré la pu de ertinar grecos, penó al Paralitico: A tucue penelo, costunatucue, ustila tun cheripen, y chatucue á tun quer.
Koma kuti inu mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko lapansi wokhululukira machimo, Iye anati kwa munthu wofa ziwaloyo, “Ine ndikuwuza iwe kuti, ‘Imirira, nyamula mphasa ndipo uzipita kwanu.’”
25 Y se costunó yescotria anglal de as aquias de junos, y ustiló a cheripen, andré que sinaba: y se chaló a desquero quer, diñando chimusolano á Debél.
Nthawi yomweyo anayimirira patsogolo pawo, nanyamula mphasa yake ndipo anapita kwawo akuyamika Mulungu.
26 Y sináron os sares pasmados, y majarificaban á Debél: y perelales de dal, penaban: Achibes hemos dicado zibos.
Aliyense anadabwa ndi kuchita mantha ndipo anayamika Mulungu. Iwo anadabwa kwambiri ndipo anati, “Lero taona zinthu zosayiwalika.”
27 Y despues de ocono chaló abrí, y dicó a yeque Publicano araquerado Levi, sos sinaba bestelado á la quejeña, y le penó: Plastañamangue.
Zitatha izi, Yesu anachoka ndipo anaona wolandira msonkho dzina lake Levi atakhala mʼnyumba ya msonkho. Yesu anati kwa iye, “Nditsate Ine.”
28 Y ardiñelandose mecó sarias desquerias buchias: y le plastañó.
Ndipo Levi anayimirira, nasiya zonse ndi kumutsata Iye.
29 Y le queró Levi yeque jachipen bari andré desquero quer, y abilló oté yeque plastañi bari de Publicanes, y de averes, sos sinaban bestelados sat junos á la mensalle.
Kenaka Levi anakonzera Yesu phwando lalikulu ku nyumba yake ndipo gulu lalikulu la amisonkho ndi ena ankadya naye pamodzi.
30 Tami os Phariseyes, y os Libanes sinaban ululés, y penaban á os discipules de Jesus: ¿Presás jamais, y piyais sat os Publicanes y chores?
Koma Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo amene anali a gulu lawo anadandaula kwa ophunzira ake, “Kodi ndi chifukwa chiyani mukudya ndi kumwa pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
31 Y Jesus les rudeló, y penó: A ocolas sos sinelan mistos, salamito no les sinela necesario, sino á ocolas sos sinelan merdés.
Yesu anawayankha kuti, “Amene sakudwala safuna singʼanga, koma odwala.
32 Na he abillado á araquerar á os laches á penitencia, sino á os chores.
Ine sindinabwere kudzayitana olungama, koma ochimwa kuti atembenuke mtima.”
33 Y ocolas le penáron: ¿Presas os discipules de Juan ayunan tanto, y manguelan, y tambien os es Phariseyes, y os de tucue jamelan y piyelan?
Iwo anati kwa Iye, “Ophunzira a Yohane amasala kudya ndi kupemphera kawirikawiri, monganso ophunzira a Afarisi, koma anu amangodya ndi kumwa.”
34 O penó á junos: ¿Por baji astisarelas querelar, que os chabores e Rom ayunen, o chiros que o Rom sinela sat junos?
Yesu anawayankha kuti, “Kodi alendo a mkwati angasale kudya pamene mkwati ali pakati pawo?
35 Tami abillarán chibeses, andré que o Rom les sinará nicabado, y ayunarán andré ocolas chibeses.
Koma nthawi ikubwera pamene mkwati adzachotsedwa pakati pawo. Masiku amenewo adzasala kudya.”
36 Y les penó yeque semejanza: Na chibela cayque remiendo de chan nebó andré plata puri: presas de aver beda o nebó parabela al puro: y ademas na nichobela mistos remiendo nebó sat o puro.
Iye anawawuza fanizo ili: “Palibe amene amangʼamba chigamba kuchokera pa chovala chatsopano ndi kuchisokerera pa chakale. Ngati atatero, ndiye kuti adzangʼamba chovala chatsopanocho, ndipo chigamba chochokera pa chovala chatsopano chija sichidzagwirizana ndi chakale.
37 Y cayque chibela mol nebó andré pigotes purés, presas de aver beda o mol nebó parabelará á os pigotes, o mol se butanará, y se chibelarán a najabar os pigotes.
Ndipo palibe amene amakhuthulira vinyo watsopano mʼmatumba a vinyo akale. Ngati atatero, vinyo watsopanoyo adzaphulitsa zikopazo, vinyo adzatayika ndipo zikopa za vinyozo zidzawonongeka.
38 Tami jomte chibar o mol nebó andré pigotes nebés, y o yeque y o aver se conserva.
Ayi, vinyo watsopano ayenera kuthiridwa mʼmatumba a vinyo azikopa zatsopano.
39 Y cayque sos piyela o puro camela yescotria o nebó, presas penela: fetér sinela o puro.
Ndipo palibe amene atamwa vinyo wakale amafuna watsopano, pakuti amati, ‘Wakale ndi okoma.’”

< Lucas 5 >