< Lucas 18 >

1 Y les penaba tambien ocona parabola: que jomte manguelar gayere, y na desfalecer,
Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
2 Penando: Sinaba yeque Barander andré foros, sos na darañaba á Un-debél, ni querelaba bajin á manu yeque;
Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
3 Y sinaba andré o matejo foros piuli, sos abillaba á ó y le penaba: Querelame justicia de minrio daschmanu.
Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
4 Y ó pre baribu chiros na camelaba. Tami despues de ocono penó andré sí: Aunque ni darañelo á Debél, ni á manu querelo bajin;
“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
5 Todavia, presas ocona piuli sinela importuna á mangue, le querelaré justicia, que na abillele tantas begais, que al fin mangue trajatela.
koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
6 Y penó o Erañó: Junelad ma penela o Barander choro.
Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
7 ¿Pues Un-debél na querelará bajin de desqueres chabores, sos araquerelan á ó á gole chibes y rachi, y terelará orpachirima andré junos?
Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
8 Sangue penelo, que sigo os listrabará. Tami pur abillará o chaboro e manu, ¿penchabelais que alachará fé andré a sueti?
Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
9 Y penó tambien ocona parabola á yeques, sos pachibelaban á sí matejos, sasta si sinaban laches, y despreciaban á os averes:
Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
10 Dui manuces ardiñeláron á la cangri á manguelar á Un-debél: o yeque Phariséo y o aver Publicano.
“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
11 O Phariséo sinando en pindré, manguelaba andré sun suncai de ocona beda: Un-debél, chimusolano te díñelo, presas na sinelo sasta os averes manuces, randes, chores, pirandes; andiar sasta sinela ocona Publicano.
Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
12 Ayunisarelo dui begais sari semana: diñelo diezmos de o saro que terelo.
Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
13 Tami o Publicano, sinando muy dur, darañaba aun costunar as aquias al Tarpe: sino que curaba sun chepo, penando: Un-debél, terela canrea de mangue choro!
“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
14 Sangue penelo, que ocono, y ocola nanai, chaló justificado á sun quer: presas saro manu, sos se ardiñela, sinará bucharado ostely: y ó sos se chibele ostely, sinará ardiñelado.
“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
15 Y le lanelaban tambien chabores, somia que os pajabase. Y pur lo dicáron os discipules, os chingaraban.
Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
16 Tami Jesus os araqueró, y penó: Mequelad, que abillelen á mangue os chabores, y na os impidais; presas de oconas sinela o chim de Debél.
Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
17 Aromali sangue penelo, que ó sos na ustilase o chim de Debél, sasta chaboro, na chalará andré ó.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
18 Y le puchabó yeque tintin baro, penando: Duquendio lacho, ¿qué querelaré somia alachar a chipen que na marela? (aiōnios g166)
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios g166)
19 Y Jesus le penó: ¿Por qué araquerelas mangue lacho? Cayque sinela lacho, sino Un-debél colcoro.
Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
20 Chanelas os Mandamientos: Na marelarás: Na pirabarás: Na randelarás: Na penelarás jujana: Pachibela á tiro batu, y á tiri dai?
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
21 O penó: Saro ocono he querdi desde que sinaba chinoro.
Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
22 Pur juneló Jesus ocono, le penó: Aun á tucue faltisarela yeque buchi: binela saro que terelas, y dinlo á os chorores, y terelarás manchin andré o Tarpe: y abillel, y plastañamangue.
Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
23 Pur ó juneló ocono, se chito charabaro: presas sinaba baribu balbalo.
Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
24 Y Jesus le penó, pur le dicó charabaro: ¡Quan dificultosamente chalarán andré o chim de Debél junos sos terelan jayere!
Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
25 Presas buchi butér facil sinela nacar brote pre la aqui de yeque jutia, que chalar manu balbalo andré o chim de Debél.
Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
26 Y penáron junos sos juneláron ocolo: ¿Pues coin astisarela salvarse?
Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 Les penó: Ma n’astis para os manuces, astis para Un-debél.
Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
28 Y penó Pedro: Mistos diquelas, que mu terelamos mequelado sarias buchias, y terelamos plastañado tucue.
Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
29 O les penó: Aromali sangue penelo, que cayque sinela, sos terele mequelado quer, ó batuces, ó planes, ó romi, ó chabores pre o chim de Debél,
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
30 Sos na terele de alachar baribu butér andré ocona chiros; y andré o chim que abillele a chipen que na marela. (aiōn g165, aiōnios g166)
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn g165, aiōnios g166)
31 Y ustiló Jesus aparte á os duideque: y os penó: Diquelad, chalamos á Jerusalém, y sinarán querdas sarias as buchias, que randáron os Prophetas del Chaboro e manu.
Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
32 Presas sinará entreguisarado á os Busnés, y sinará caquerado, y curado, y chotiado.
Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
33 Y despues que le curaren, le nicabarán a chipen, y ostinará al trincho chibes.
adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
34 Tami junos na jabilláron chichi de ocono: y ocona varda sinaba pandada á junos; y na jabillaban ma les penaba.
Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
35 Y anacó, que bigoreando sunparal á Jericho, sinaba yeque perpenta bestelado aligatas del drun, mangando limosna.
Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
36 Y pur juneló a chumas e sueti sos nacaba puchabó, qué sinaba ocono.
anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
37 Y le penáron, que nacaba Jesus Nazareno.
Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
38 Y penó á gole gole: Jesus, Chaboro de David, terela canrea de mangue.
Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
39 Y junos sos chalaban anglal le chingaraban, somia que mequelase. Tami ó garlaba baribu butér: Chaboro de David, terela canrea de mangue:
Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
40 Y Jesus parándose, penó que se le lanelasen. Y pur sinaba sunparal, le puchabó,
Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
41 Penando: ¿Qué camelas que te querele? Y ó rudeló: Erañó, que diquele.
“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
42 Y Jesus le penó: Diquela, tun fé te ha chibado lacho.
Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
43 Y yescotria dicó, y le plastañaba chimusolanificando á Debél. Y pur dicó ocono sari a sueti, dinó loor á Debél.
Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.

< Lucas 18 >