< Lucas 17 >

1 Y penó á desqueres discipules: N’astis, que na abillelen escandales: ¡Tami ysna de ocola, por coin abillelén!
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 Fetér le sinaria, que le chibasen al querlo bar de asia y le bucharasen andré o moros, que querelar escandalo á yeque de oconas chinores.
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 Diquelad por sangue: si querelare grecos tiro plal contra tucue, corrigele: y si querelare penitencia, ertinale.
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 Y si querelare grecos contra tucue efta begais al chibes, y efta begais al chibes se limbidiare á tucue, penando: He querdi choro, ertinale.
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 Y penáron os Apostoles al Erañó: Din amangue fé butér.
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 Y penó o Érañó: Si terelareis fé, sasta yeque grano de mostaza, y penelareis á ocona moral: Despandate de raiz, y chibelate oté andré o moros: lo querelará.
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 ¿Y coin de sangue terelando yeque lacró, sos randiñela, ó garabela as brajias, pur limbidiela del bur, le penela: Chatucue yescotria, y bestelate á la mensalle?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 Y na le penela gres: Chitelame de jamar, y chitelate á servirme, o chiros que jamelo y piyelo; que despues jamarás y piyarás?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 ¿Pre baji se debisarelan garapatias á ocola lacró presas ocona querela ma le penó?
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 Penchabelo que nanai. Andiar tambien sangue, pur querelareis sarias as buchias que á sangue sinelan penadas, penad: Lacrés sinamos inutiles: Ma debisaramos querelar, querelemos.
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 Y anacó que chalando ó á Jerusalém, nacó por medio de Samaria, y de Galiléa.
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 Y chalando andré yeque gau, chaláron abrí á ó deque manuces zarapiosos, sos se paráron de dur.
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 Y diñaron goles, penando: Jesus duquendio, terela canrea de amangue.
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 O pur dicó junos, penó: Chalad, somia diquelen sangue os erajais. Y anacó, que o chiros que chalaban, sináron chibados lacho.
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 Y yeque de junos, pur dicó que habia sinado chibado lacho, limbidió diñando chimusolano á Debél á goles bares.
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 Y se bucharó en chiquen, á os pindrés de Jesus, diñando garapatias: y ocona sinaba Samaritano.
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 Y rudeló Jesus, y penó: ¿Pre baji na sinelan deque junos sos sináron chibados lacho? ¿Y os nu averes duque sinelan?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 ¿Na sinaba yeque sos limbidiase, y diñase chimusolano á Debél, sino ocana gringó?
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 Y le penó: Costunatucue, chatucue, que tiri fé te ha chibado lacho.
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 Y puchabandole os Phariseyes: ¿Pur abillará o chim de Debél? les rudeló, y penó: O chim de Debél na abillará sat simache de abrí;
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 Ni penelarán: helo acoi, o helo oté: presas o chim de Debél sinela andré de sangue.
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 Y penó á desqueres discipules: Abillarán chibeses, pur camelareis dicar yeque chibes e Chaboro e Manu, y na lo dicareis.
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 Y sangue penarán: Diqueladle acoi, y diqueladle oté. Na cameleis chalar, ni le plastañeis.
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 Presas sasta o maluno, sos diñelando dut andré a region ostely e Charos, voltisarela desde la yeque disde la aver aricata; andiar tambien sinará o Chaboro e manu andré desquero chibes.
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 Tami jomte brotoboro que ó padezca baribu, y que sinele reprobado de ocona sueti.
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 Y sasta sinaba andré os chibeses de Noé, andiar tambien sinará andré os chibeses e Chaboro e manu.
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 Jamaban, y piyaban: os manuces ustilaban romias, y as cadchias romes disde o chibes pur Noé chaló andré á Jestari; y abilló a pani bari, y mulabó á sares.
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 Andiarmatejo sasta sinaba andré os chibeses de Lot; jamaban, y piyaban; quinaban, y binaban; chitaban carschtas, y querelaban querés.
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 Y o chibes, que chaló Lot abrí de Sodoma, peró yaque y azufre de o Charos, y os marabó á sares.
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 Andiar sinará o chibes, pur se mequelará dicar o Chaboro e manu.
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 André ocola ocana o sos sinare opré o tejado, y terelare desqueres coneles andré o quer, na chale ostely á ustilarlos, y ó sos sinare andré o ortalame, andiar matejo na limbidiele palal.
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 Terelad en fácho a romi de Lot.
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 O saro sos camelare salvar sun chipen, la najabará; y ó sos la najabará, la alachará.
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 Sangue penelo, que andré ocola rachi dui sinarán andré yeque cheripen, yéque sinará ustilado, y o aver mequelado.
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 Dui cadchias sinarán nacicando andré a asia catanias; yeque sinará ustilada, a aver mequelada: dui andré l’ortalame; yeque sinará ustilado, y o aver mequelado.
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 Rudeláron, y le penáron: ¿Anduque Erañó?
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 Y ó les penó: Duque sináre o trupos, oté tambien se catanaran as aguilas.
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< Lucas 17 >