< Lucas 13 >

1 Y andré ocona matejo chiros sinaban oté yeques, sos le penaban nuevas es Galileyes, cuya rati habia bucharado Pilato andré la es sacrificios de junos.
Nthawi yomweyo panali ena amene analipo omwe amamuwuza Yesu za Agalileya amene magazi awo Pilato anawasakaniza ndi nsembe zawo.
2 Y Jesus les rudeló, penando: ¿Penchabelais, que ocolas Galileyes sináron chorés butér que sares os averes, por terelar padecido buchias oconas?
Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuganiza kuti Agalileya amenewa anali ochimwa kwambiri kuposa Agalileya ena onse chifukwa anavutika mʼnjira iyi?
3 Sangue penelo, que nanai: Tami si na querelareis penitencia, os sares merareis andré a mateja beda.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.
4 Andiar sasta tambien ocolas deque y otor manuces, opré coines peró o quer baro andré Siloé, y los maró: ¿penchabelais, que junos debisáron butér qus os sares manuces sos socabelaban andré Jerusalém?
Kapena anthu 18 aja amene anafa nsanja ya Siloamu itawagwera, kodi mukuganiza kuti iwo aja anali ochimwa kwambiri kuposa onse amene amakhala mu Yerusalemu?
5 Sangue penelo, que nanai: tami si na querelareis penitencia, os sares merareis andré a mateja beda.
Ine ndikuti, ayi! Koma ngati inu simutembenuka mtima, inunso mudzawonongeka nonse.”
6 Y penelaba tambien ocona parabola: Manu terelaba carschta chabéra chitalada andré sun resis, y chaló á orotar mibao andré siró, y na le alachó.
Kenaka Iye anawawuza fanizo kuti, “Munthu wina anali ndi mtengo wamkuyu, umene anadzala mʼmunda wamphesa, ndipo Iye anapita kukayangʼana zipatso, koma sanazipeze.
7 Y penó al paillo sos randiñó a resis: Diquela; trin berjis sinela que abillelo a orotar mibao andré ocona carschta chabera, y na lo alachó: velala pues: ¿para qué terela de ucharar aun a chiquen?
Tsono kwa munthu amene amasamalira munda wamphesawo anati, ‘Kwa zaka zitatu tsopano ndakhala ndikubwera kudzafuna chipatso pa mtengo uwu ndipo sindinachipeze. Udule! Nʼchifukwa chiyani ukuwononga nthaka?’
8 Tami ocola rudeló y le penó: Erañó: mequelela aun ocona berji, y la cavaré al crugos, y le chibaré groñi:
“Munthuyo anayankha kuti, ‘Bwana, tawusiyani kwa chaka chimodzi chokha ndipo ine ndikumba ngalande mozungulira ndi kuthira manyowa.
9 Astis sat ocono diñare mibao: y si nanai, la velarás despues.
Ngati udzabale zipatso chaka chamawa, zili bwino! Koma ngati sudzabala, pamenepo mudzawudule.’”
10 Y sinaba bedando andré a Synagoga de junos as Canchés.
Pa Sabata Yesu ankaphunzitsa mʼsunagoge ina,
11 Y he acoi yeque cadchi, sos terelaba bengui de merdipen deque y otor berjis habia: y sinaba encorbada que na le astis dicar acia opré.
ndipo momwemo munali mayi amene anali ndi mzimu woyipa umene unamudwalitsa zaka 18. Iye anali wokhota msana ndipo samatha kuweramuka ndi pangʼono pomwe.
12 Pur la dicó Jesus, la araqueró á siró, y la penó: Cadchi, libre sinelas de tun merdipén.
Yesu atamuona anamuyitana kutsogolo ndipo anati kwa iye, “Amayi, mwamasulidwa ku mavuto.”
13 Y chibó opré siró as bastes, y yescotria se ardiñó, y diñaba chimusolano á Debél.
Kenaka anasanjika manja ake pa iye, ndipo nthawi yomweyo anawongoka nayamika Mulungu.
14 Y ustilando a varda o Manclay e Synagoga, ululé presas Jesus habia chibado lacho andré la Canché, penó á la sueti: Zoi chibeses terelais, andré que astis randiñar: andré oconas pues abillad, y que chibele sangue lacho, y andré la Canché nanai.
Chifukwa cha kuyipidwa kuti Yesu anachiritsa pa Sabata, wolamulira sunagoge anati kwa anthu, “Pali masiku asanu ndi limodzi ogwira ntchito. Choncho bwerani kuti mudzachiritsidwe masiku amenewo osati pa Sabata.”
15 Y rudelando o Erañó penó: Sungales, saro yeque de sangue na despandela andré la Canché desquero goruy, ó desquero gel del olibal y lo lliguerela á piyar.
Ambuye anamuyankha kuti, “Iwe wachiphamaso! Kodi nonsenu simumasula pa Sabata ngʼombe zanu kapena bulu kumuchotsa mʼkhola ndi kupita naye kukamupatsa madzi?
16 ¿Y ocona chai de Abraham, á coin terelaba pandisarado Satanás deque y otor berjis, na sinela mistos despandarla de ocona trajata andré chibes de Canché?
Nanga mayiyu, amene ndi mwana wa Abrahamu, ndipo anamangidwa ndi Satana zaka 18, kodi siwoyenera kuti amasulidwe msinga imeneyi pa tsiku la Sabata?”
17 Y penando oconas buchias se pachibelaban sares os daschmanuces de ó: tami se alendaba sari a sueti de sarias as buchias, que ó querelaba chimusolanamente.
Atanena izi, onse omutsutsa anachititsidwa manyazi, koma anthu anakondwera ndi zodabwitsa zonse zimene Iye anazichita.
18 Penelaba pues: ¿A qué buchi sinela semejante o chim de Debél, y á que buchi lo compararé?
Kenaka Yesu anafunsa kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu uli ngati chiyani? Kodi Ine ndingawufanizire ndi chiyani?
19 Semejante sinela al grano e mostaza, sos lo ustiló yeque manu y lo chitó andré desquero vea, y se queró baro, y se queró carschta udschi; y as ujarres e charos sobeláron opré desqueres senques.
Uli ngati mbewu ya mpiru, imene munthu anatenga ndi kudzala mʼmunda mwake. Inakula, nʼkukhala mtengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinakhala mʼnthambi zake.”
20 Y penó aver chiros: A qué penelaré, que o chim de Debél sinela semejante?
Iye anafunsanso kuti, “Kodi ufumu wa Mulungu ndingawufanizire ndi chiyani?
21 Semejante sinela á la levadura, sos ustiló yeque cadchi, y la chibó andré trin melales de roi, disde que o saro se querase fermentado.
Uli ngati yisiti amene mayi anatenga ndi kusakaniza ndi ufa wambiri mpaka anafufumitsa ufawo.”
22 Y chalaba por foros y gau, bedando y querelando drun ácia Jerusalém.
Ndipo Yesu anayendayenda mʼmizinda ndi mʼmidzi, kumaphunzitsa pamene Iye ankapita ku Yerusalemu.
23 Y le penó yeque manu: ¿Eraño, sinelan frimes junos sos se salvan? Y ó les penó:
Wina anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndi anthu ochepa okha amene adzapulumutsidwe?” Iye anawawuza kuti,
24 Querelad ezor á sicobaros andré por a bundal chinori: presas sangue penelo, que baribustres camelarán chalar andré, y na les astis.
“Yesetsani kulowa pa khomo lopapatiza, chifukwa ndikukuwuzani kuti ambiri adzafuna kulowa koma sadzatha kutero.
25 Y pur o batu e quer terelare chalado andré, y pandado a bundal, sangue sinareis abrí, y os chitareis á araquerar á la bundal, penando: Erañó, pendrabanos: y ó os rudelará, penando: Na chanelo duque sinelais sangue:
Nthawi yomwe mwini nyumba adzayimirira ndi kutseka chitseko, inu mudzayima kunja kugogoda ndi kudandaula kuti, ‘Bwana, tatitsekulirani khomo.’ “Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera.’
26 Entonces os chibareis á penar: Anglal de tucue jamemos y piyemos, y andré amares masqueres bedaste.
“Ndipo inu mudzati, tinkadya ndi kumwa ndi inu ndipo munkaphunzitsa mʼmisewu yathu.
27 Y os penará: Na chanelo duque sangue sinelais: Chalaos de mangue sares os curadores e choripen.
“Koma Iye adzayankha kuti, ‘Ine sindikukudziwani ndipo sindikudziwanso kumene mwachokera. Chokereni inu nonse ochita zoyipa!’
28 Oté sinará o orabar, y o nacicar de danias, pur dicareis á Abraham, y á Isaac, y á Jacob, y á sares os Prophetas andré o chim de Debél, y sangue sinelais bucharados abrí.
“Mudzalira ndi kukuta mano mukadzaona Abrahamu, Isake ndi Yakobo ndi aneneri onse ali mu ufumu wa Mulungu koma inuyo mutaponyedwa kunja.
29 Y abillarán de Boctaro, y de Occidente, y de Aquilón, y de Austro, y se bestelarán á la mensalle andré o chim de Debél.
Anthu adzachokera kummawa ndi kumadzulo, kumpoto ndi kummwera, kudzakhala pa phwando mu ufumu wa Mulungu.
30 Y he acoi que sinelan segritones, junos sos sinarán brotobores, y que brotobores, junos sos sinarán segritones.
Ndithudi otsirizira ndiye adzakhale oyambirira, ndipo oyambirira ndiye adzakhale otsirizira.”
31 Ocona matejo chibes se bigoreáron á ó yeques Phariseyes, y le penáron: Sicobelatucue de acoi, y chatucue, presas Herodes te camela marar.
Pa nthawi imeneyo Afarisi anabwera kwa Yesu ndipo anati kwa Iye, “Chokani malo ano ndipo pitani kumalo ena aliwonse. Herode akufuna kukuphani.”
32 Y les penó: Chalad, y penad á ocola rubasuncha, que menda bucharelo bengues, y chibelo lacho achibes y tasáta, y al trincho chibes sinelo chichi.
Iye anayankha kuti, “Pitani kawuzeni nkhandweyo, Ine ndikutulutsa ziwanda ndi kuchiritsa anthu lero ndi mawa ndipo tsiku lachitatu ndidzakwaniritsa cholinga changa.”
33 Tami jomte, que menda pirele achibes, y tasáta, y aver chibes: Presas n’astis que yeque Propheta merele abrí de Jerusalém.
Mʼnjira ina iliyonse, Ine ndiyenera kupitirira ulendo wanga lero, mawa ndi mkuja. Zoona nʼzakuti mneneri sangafere kunja kwa Yerusalemu.
34 Jerusalém, Jerusalém, sos marelas á os Prophetas, y bucharélas barias á junos sos sinelan bichabados á tucue, ¿quantas begais camelé catanar tires chabores, sasta a cañi desqueres chiricles ostely desquerias alas, y na camelaste.
Iwe Yerusalemu, Yerusalemu! Umapha aneneri ndi kuwagenda miyala anthu amene atumizidwa kwa iwe. Nthawi zambiri ndakhala ndikufuna kusonkhanitsa ana ako pamodzi, monga nkhuku imasonkhanitsira anapiye pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune!
35 He acoi que á tucue sinará mequelada bi sueti tiro quer. Y á tucue penelo que na diquelarás mangue butér, disde que abilleli o chiros, pur penelais: Majarificable sinele ó sos abillele andré o nao e Erañoró.
Taona, nyumba yako yasanduka bwinja. Ine ndikukuwuza kuti, sudzandionanso mpaka pamene udzati, “Wodala amene akubwera mʼdzina la Ambuye!”

< Lucas 13 >