< Lucas 11 >

1 Y anacó, que sinando beqelando andré yeque stano, pur achinóse a mui, penó á ó yeque es discipules de ó. Erañó, bedela amangue a manguelar á Un-debél, sasta tambien Juan bedó á desqueres discipules.
Tsiku lina Yesu amapemphera pamalo ena. Atamaliza, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Ambuye tiphunzitseni kupemphera, monga momwe Yohane anaphunzitsira ophunzira ake.”
2 Y les penó: Pur manguelareis, penelad: Amaro Dada, oté andré o Tarpe, majarificable sinele tun nao. Abillele tun chim. Sinele querdi tun pesquital andré a jolili, sasta andré o Tarpe.
Yesu anawawuza kuti, “Pamene mukupemphera muzinena kuti: “‘Atate, dzina lanu lilemekezedwe, ufumu wanu ubwere.
3 Diñamangue achibes amaro manro de cada chibes.
Mutipatse chakudya chathu chalero,
4 Y amangue ertina amarias visabas, andiar sasta mu ertinamos á os sares, sos debisarelen amangue buchi. Y na enseeles amangue andré o chungalo y choro.
mutikhululukire machimo athu, monga ifenso timakhululukira aliyense amene watilakwira. Ndipo musalole kuti tigwe mʼmayesero.’”
5 Les penó tambien: Coin de sangue terela yeque monro, y chalará á ó á pas-rachi, y le penará: Monro, prestelamangue trin manres,
Kenaka anawawuza kuti, “Tiyerekeze: Mmodzi mwa inu atakhala ndi bwenzi lake, ndipo iye nʼkupita ku nyumba yake pakati pa usiku, nakanena kuti, ‘Mnzanga, bwereke malofu atatu abuledi,
6 Presas monro de mangue ha bigoreado del drun, y na terelo buchi que chitar anglal de ó.
chifukwa ndalandira bwenzi langa amene ali pa ulendo ndipo ine ndilibe choti ndimupatse.’
7 Y o aver rudelase de enrun, penando: Na sinele á mangue trajatoso, ya sinela pandada a bundal, y minres lacrés sinelan tambien sasta menda andré a cheripen, n’astis que menda me costunase somia diñartelos.
“Ndipo yerekezani kuti amene ali mʼnyumbamo ndi kuyankha kuti, ‘Usandivutitse ine, ndatseka kale chitseko, ndipo ine ndi ana anga tagona. Ine sindingadzukenso kuti ndidzakupatse.’
8 Y si o aver perseverase araquerando á la bundal, penelo á sangue, que ya que na se costunase á diñarselos por sinelar desquero quiribo; aromali por desqueres goles se costunaria, y le diñaria sares os manres hubiese menester.
Ine ndikukuwuzani kuti adzadzuka ndi kumupatsa bulediyo, osati chifukwa ndi bwenzi lake, koma chifukwa cha liwuma la munthu wopemphayo, ndipo kudzamupatsa zonse zimene akuzifuna.
9 Y menda penelo á sangue: Manguelad, y se os diñará: orotelad, y alachalareis: araquelad, y se os pendrabará.
“Choncho Ine ndikunena kwa inu kuti: Pemphani ndipo adzakupatsani. Funafunani ndipo mudzapeza. Gogodani ndipo adzakutsekulirani.
10 Presas o saro sos manguela, ustilela: y ó sos orotela, alachela: y al sos araquela, se le despandará.
Pakuti aliyense amene amapempha amalandira. Munthu amene amafunafuna amapeza. Iye amene amagogoda amamutsekulira.
11 ¿Y si yeque de sangue manguelare manro á desquero batu, le diñara ó yeque bar? ¿ó si yeque macho, por baji le diñará yeque julistraba en lugar e macho?
“Ndani mwa inu abambo, kodi mwana wanu atapempha nsomba, mʼmalo mwake mungamupatse njoka?
12 ¿O si le manguelare yeque anro, por baji le bucharará yeque escorpion?
Kapena atapempha dzira, kodi mungamupatse chinkhanira?
13 Pues si sangue, sinando chorés, chanelais diñar lachias diñipenes á jires chabores ¿cuanto butér jire Dada del Tarpe diñara suncai lachi á junos sos se lo manguelaren?
Tsono ngati inu, anthu oyipa, mumadziwa kupereka mphatso zabwino kwa ana anu, koposa kotani Atate anu akumwamba, angalephere bwanji kupereka Mzimu Woyera kwa amene awapempha!”
14 Y sinaba Jesus bucharando abri yeque bengue: y ocona sinaba musilé, y pur hubó bucharado al bengue, chamulió o musilé, y sares se zibáron.
Yesu amatulutsa chiwanda chimene chinali chosayankhula. Chiwandacho chitatuluka, munthu wosayankhulayo anayankhula, ndipo gulu la anthu linadabwa.
15 Tami yeques de junos penáron: André sila de Beelzebub Manclay es bengues, bucharela os bengues.
Koma ena mwa iwo anati, “Iye akutulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mfumu ya ziwanda.”
16 Y averes somia pesquibarle, le manguelaban simache del Tarpe.
Ena anamuyesa pomufunsa chizindikiro chochokera kumwamba.
17 Y pur dicó os carlochines de junos, les penó: Saro chim chingarando contra sí matejo, sinará chibado andré najipen; y perará quer opré quer.
Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse wogawikana udzawonongeka, ndipo nyumba yogawikana idzapasuka.
18 Pues si Satanas sinele tambien en billa contra sí matejo, ¿como sinará en pindré o chim de ó? presas penelais que menda bucharelo abrí bengues por sila de Beelzebub.
Ngati Satana adziwukira yekha, ufumu wake ungalimbe bwanji? Ine ndikunena izi chifukwa inu mukuti Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu.
19 Pues si menda por sila de Beelzebub bucharelo os bengues, ¿jirés chabores por coin os bucharelan? Por ocono sinarán junos jueces de sangue.
Tsopano ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu, nanga ophunzira anu amazitulutsa ndi mphamvu ya ndani? Choncho, iwowo ndiye adzakhala oweruza anu.
20 Tami si sat l’angusti de Debél bucharelo os bengues, aromalí o chim de Debél ha bigoreado á sangue.
Koma ngati ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Mulungu, ndiye kuti ufumu wa Mulungu wafika pakati panu.
21 Pur o manusalo ujarela desquero quer, andré trifusco sinelan sarias as buchias que terela.
“Munthu wamphamvu, amene ali ndi zida, akamalondera nyumba yake, katundu wake amatetezedwa.
22 Tami si abillando aver butér manusalo que ó, le venciere, le nicobará sarias as armas de ó, andré que pachibelaba, y sicobará desquero jayere.
Koma pakabwera wina wamphamvu zoposa namugonjetsa, amalanda zida zimene munthuyo amazidalirazo ndi kugawa katundu wake.
23 O sos na sinela con-a-mangue, contra mangue sinela: O sos na ustilela con-a-mangue, najibela.
“Munthu amene sali mbali yanga ndi wotsutsana nane. Ndipo wosandithandiza kusonkhanitsa, ameneyo ndi womwaza.
24 Pur o bengue jindo ha chalado abrí de yeque manu, pirela por stanes bipaniosos orotando paratuté: y pur no lo alachela, penela: Mangue limbidiare á minrio quer, d’uque chalé abrí.
“Mzimu woyipa ukatuluka mwa munthu, umakayendayenda ku malo owuma, kufunafuna malo opumulirako ndipo suwapeza. Kenaka umati, ‘Ndibwerera ku nyumba kwanga kumene ndachokera.’
25 Y pur limbidiela, lo alachela julabado y chito.
Ukafika umapeza mʼnyumba mosesedwa bwino ndi mokonza.
26 Entonces chala, y ustilela sat ó averes efta bengues, butér chores que ó, y chalan andré, y socabelan oté. Y lo segriton de ocola manu sinela butér choro que lo brotobo.
Pamenepo umakatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa iwowo ndipo imakalowa ndi kukhala mʼmenemo. Ndipo makhalidwe otsiriza a munthuyo amakhala oyipa kuposa oyamba aja.”
27 Y anacó, que penando ó ocono, yeque cadchi de enré a sueti ardiñó a voz, y le garló: Majari a poria sos te chindó, y as chuchais sos mamaste.
Pamene Yesu ankanena zonsezi, mayi wina mʼgulu la anthuwo anafuwula nati, “Ndi wodala amayi amene anakubalani ndi kukulerani!”
28 Y ó rudeló: Nanai! antes majares junos sos junelan a varda de Debél y l’ujarelan.
Koma Yesu anayankha kuti, “Odala ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kuwasunga.”
29 Y sasta a sueti abillase de sarias aricatas, se chibó a penar: Ocona rati, rati sungali sinela, simache manguela, y simache na le sinará diñada, sino a simache e Propheta Jonás.
Pamene gulu la anthu limachuluka, Yesu anati, “Uno ndi mʼbado oyipa. Umafuna kuona chizindikiro chodabwitsa. Koma sadzachiona kupatula chizindikiro chija cha Yona.
30 Presas sasta Jonás sinaba simache a junos de Ninive; andiar tambien o Chaboro e manu la sinará á ocona rati.
Monga Yona uja anali chizindikiro kwa anthu ku Ninive, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala chizindikiro kwa anthu a mʼbado uno.
31 La Crallisa e Pas-chibe se ardiñará andré juicio contra os manuces de ocona rati, y os saplará, presas abílló de os fines de la pu á junelar a chaneleria de Salomon; y he acoi butér que Salomon andré ocona stano.
Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi anthu a mʼbado uno ndipo idzawatsutsa, chifukwa iyo inachokera kumapeto a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Solomoni.
32 Os manuces de Ninive se ardiñarán contra ocona rati andré juicio, y la saplarán: presas quereláron penitencia á los goles de Jonás; y he acoi buter que Jonás andré ocona stano.
Anthu a ku Ninive adzayimirira tsiku lachiweruzo pamodzi ndi mʼbado uno ndipo adzawutsutsa, pakuti anatembenuka mtima ndi ulaliki wa Yona. Ndipo tsopano pano pali wina woposa Yona.
33 Cayque urdiflela á yeque mermellin, y la chitela andré yeque stano escondido, ni ostely de yeque melalo; sino opré yeque dendesquero, somia que junos sos abillelan andré diquelen a dut.
“Palibe amene amayatsa nyale ndi kuyiika pa malo poti sionekera, kapena pansi pa mtsuko. Mʼmalo mwake amayika pa choyikapo chake, kuti iwo amene akulowamo aone kuwunika.
34 A mermellin de tun trupos sinela tun aqui. Si tun aqui sinare lachi, saro tun trupos sinará dutoso: tami si sinare chori, tambien tun trupos sinará bi dut.
Diso lanu ndi nyale ya thupi lanu. Pamene maso anu ali bwino, thupi lanu lonse limadzaza ndi kuwunika. Koma ngati ali oyipa, thupi lanunso ndi lodzaza ndi mdima.
35 Diquela pues, que a dut andré tucue, na sinela rachi.
Onetsetsani tsono, kuti kuwunika kuli mwa inu si mdima.
36 Y andiar si saro tun trupos sinare dutoso, bi terelar yeque aricata de rachi, o saro sinará dutoso, y te diñará dut sasta yeque mermellin de dut.
Choncho, ngati thupi lanu lonse ndi lodzaza ndi kuwunika, ndiye kuti palibe dera lina lili mdima, lonselo lidzakhala kuwunika, monga momwe kuwunika kwa nyale kumakuwalirani.”
37 Y pur sinaba chamuliando, le mangó yeque Phariséo, que chalase á jamar sat ó, y habiendo chalado andré, se besteló á la mensalle.
Yesu atamaliza kuyankhula, Mfarisi wina anamuyitana kuti akadye naye. Tsono Yesu analowa mʼnyumba ndi kukhala podyera.
38 Y o Phariséo se chitó á penchabar, y penar andré de sí, presas na se había chobelado antes de jamar.
Mfarisiyo anadabwa atazindikira kuti Yesu anayamba kudya wosatsata mwambo wawo wakasambidwe ka mʼmanja.
39 Y o Eraño penó: Acana sangue os Phariseyes chobelais lo de abrí e gote, y e plato; tami sangue de enrun sinelais perelalés de randipen y de choripen.
Kenaka Ambuye anamuwuza kuti, “Inu Afarisi mumatsuka kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkati mwanu ndi modzaza ndi kudzikonda ndi zoyipa.
40 Dineles, ¿O sos quereló ma sinela de abrí, na quereló tambien ma sinela de enrun?
Anthu opusa inu! Kodi amene anapanga zamʼkati sanapangenso zakunja?
41 Ocono no obstante, diñelad limosna: y sarias as buchias os sinelan limpias.
Koma popereka kwa osauka, perekani chimene chili mʼkati ndipo chilichonse chidzakhala choyera.
42 ¡Tami ysna de sangue, Phariseyes, sos chibelais andré deque aricatas a cha-lachi, y a Romani cha, y sari hortaliza, y na querelaís bajin e lachiria, y e amor de Debél! Pues sinaba mistos querelar oconas buchias, y na mequelar ocolas.
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumapereka kwa Mulungu chakhumi cha timbewu tonunkhira, ndi timbewu tokometsera chakudya ndi mbewu zina zonse za mʼmunda, koma mumakana chilungamo ndi chikondi cha Mulungu. Mumayenera kuchita zomalizirazi osalekanso kuchita zoyambazi.
43 ¡Ysna de sangue Phariseyes, sos camelais as brotoborias bestés andré as Synagogas, y sinelar saludados andré os maasqueres!
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa mumakonda mipando yofunika kwambiri mʼmasunagoge ndi malonje mʼmalo a pa msika.
44 ¡Ysna de sangue, sos sinelais sasta os sepulchres, sos na se diquela, y na lo chanelan os manuces, que pirelan por opré!
“Tsoka kwa inu Afarisi, chifukwa muli ngati manda osawaka, amene anthu amangoyendapo, osawadziwa.”
45 Y rudelando yeque es Chandés e Eschastra, le penó: Duquendio, chamuliando oconas buchias, tucue afrentas tambien á amangue.
Mmodzi mwa akatswiri a Malamulo anamuyankha Iye nati, “Aphunzitsi, pamene mukunena zinthu izi, mukutinyoza ifenso?”
46 Y ó penó: Y ysna de sangue Chandes e Eschastra: sos cargais os manuces de cargas, sos n’astis lliguerar, y sangue ni aun sat yeque de jiresias angustias pajabelais as cargas!
Yesu anayankha kuti, “Tsoka kwa inunso akatswiri a Malamulo chifukwa mumawalemetsa anthu ndi mtolo umene iwo sangathe kunyamula, ndipo inu eni ake simutenga chala chanu kuti muwathandize.
47 ¡Ysna de sangue, sos querelais os sepulchres es Prophetas: y jires batuces os maráron!
“Tsoka kwa inu, chifukwa mumawaka manda a aneneri, komatu ndi makolo anu amene anawapha.
48 Aromali diñelais á chanelar, que camelais ma quereláron jires batuces: ocolas os maráron, chachipén; tami sangue querelais desqueres sepulchres.
Tsono potero mumachitira umboni za zimene makolo anu anachita. Anapha aneneri, ndipo inu mumawaka manda awo.
49 Por ocono penó tambien a chaneleria de Debél: Les bichabaré Prophetas y Apóstoles, y de junos mararán, y plastañarán para marar:
Chifukwa cha ichi, Mulungu mu nzeru zake anati, ‘Ine ndidzawatumizira aneneri ndi atumwi, ena mwa iwo adzawapha ndipo ena adzawazunza.’
50 Somia que sinele pedida á ocona sueti a rati de sares os Prophetas, que sinaba chibada desde o principio de chiros.
Choncho mʼbado uwu udzasenza magazi a aneneri onse amene anakhetsedwa kuyambira pachiyambi cha dziko,
51 Desde a rati de Abel, disde a rati de Zacharias, sos meró entre o altar, y a cangri. Andiar os penelo, que pedida sinará á ocona sueti.
kuyambira magazi a Abele kufikira magazi a Zakariya amene anaphedwa pakati pa guwa lansembe ndi malo opatulika. Inde, Ine ndikuwuzani inu, mʼbado uno udzasenza zonsezi.
52 ¡Ysna de sangue, Chandés e Eschastra, sos ardiñasteis sat a clichi de chaneleria! sangue na chalasteis andré, y na mequelasteis á ocolas sos chalaban andré.
“Tsoka kwa inu akatswiri a Malamulo, chifukwa mwachotsa kiyi wachidziwitso inu eni akenu musanalowemo, ndipo mwatsekerezanso iwo amene amalowa.”
53 Y penando oconas buchias, os Phariseyes, y os Chandés e Eschastra se chibáron á chingarar con ó sat sila, y á trajatarle sat baribustrias preguntas,
Pamene Yesu anachokamo, Afarisi ndi aphunzitsi a Malamulo anayamba kumamutsutsa koopsa ndi kumupanikiza ndi mafunso,
54 Chibandole lazos, y orotando de sicobar de desquero sonsi yeque buchi somia astisar saplarle.
pofuna kumukola muchina chilichonse chimene Iye angayankhule.

< Lucas 11 >