< Йов 8 >

1 Тогава шуахецът Валдад в отговор каза:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 До кога ще говориш така, И думите на устата ти ще бъдат като силен вятър?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Бог променя ли съда? Или Всемогъщият променя правдата?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Ако Му са съгрешили чадата ти, И Той ги е предал на последствията от беззаконието им;
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Ако би ти прилежно потърсил Бога, Ако би се помолил на Всемогъщия,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Тогава, ако беше ти чист и праведен, Непременно сега Той би се събудил да работи за тебе, И би направил да благоденствува праведното ти жилище;
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 И при все да е било малко началото ти, Пак сетнините ти биха се уголемили много.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Понеже, попитай, моля, предишните родове, И внимавай на изпитаното от бащите им;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (Защото ние сме вчерашни и не знаем нищо, Тъй като дните на земята са сянката);
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Не щат ли те да те научат и да ти явят, И да произнесат думи от сърцата си?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Никне ли рогоза без тиня? Расте ли тръстиката без вода?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Догде е зелена и неокосена Изсъхва преди всяка друга трева.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Така са пътищата на всички, които забравят Бога; И надеждата на нечестивия ще загине.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Надеждата му ще се пресече; Упованието му е паяжина.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Той ще се опре на къщата си, но тя не ще устои; Ще се хване за нея, но не ще утрае.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Той зеленее пред слънцето, И клончетата му се простират в градината му;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Корените му се сплитат в грамадата камъни; Той гледа на камъните като дом;
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Но пак, ако го изтръгне някой от мястото му, Тогава мястото ще се отрече от него, казвайки: Не съм те видял.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ето, това е радостта на пътя му! И от пръстта други ще поникнат.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Ето, Бог няма да отхвърли непорочния, Нито ще подири ръката на злотворците.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Все пак ще напълни устата ти със смях И устните ти с възклицание.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Ония, които те мразят, ще се облекат със срам; И шатърът на нечестивите няма вече да съществува.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Йов 8 >