< Ibraniyawa 6 >

1 Nin nani usunu nimon na iwa durso nari nin nburne, kitene kaduran Kiristi, tiba li uban udu tikunag, na tutun utunu litino ndiu katyen nanya katuwa nkul, a uyinnu nin Kutelle,
Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
2 na nlon litino ndursuzu kitene nsulsunu ulau, utardu nacara, utitu na nan nkul, in nshara sa ligan. (aiōnios g166)
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios g166)
3 Arike tutun ba su ulle imone asa Kutelle nyinna.
Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
4 Bara uso gbas, kiti na lenge na iwa tinani iyinno, ule na awa dumun ufillu Kutelle, ule na iwa kuso nin nfip milau.
Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
5 inug alle na iwa dumun tigbulan ticine in Kutelle nin likara kuji ncin dak. (aiōn g165)
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn g165)
6 inug alle na iwa diuwe-udinin nijasi ukpiliya nani tutun udin ndiu kutyin, nanere bara na inghe atimine wa kotin gono Kutelle kitene kuca, tutun itanghe aso imon ncing fong.
Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
7 Bara kutyin na serru uwuru na udi njju kunin, nkoni din nutuzunu ileou isesu uampani inug alle na idi katuwa kunenne, isere nmari kiti Kutelle.
Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
8 Bara as kunutuno imart nin ubarje, ku ba so hem, nin ndre nnti nnu, imalline ba dak nin njujuzu.
Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
9 Vat nin nani tidin nliru nenge, adondong bite tise likara nimon icine, ulenge na idi immine, imon ille na idi in tucue.
Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
10 Bara na Kutelle unan salin adalciari ba, na aba shawu nin katuwa mine nin nsu na ina durso bara lissa me, nanya nanere iwa tumuzun annit alau, udak nene idinsu nani.
Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
11 Nin nani arike ntah nibinayi, nworo kogha nanya mine ba dursu imusu nciu kibinayi udu imalin, nin se ntabas nyinnu.
Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
12 Na tidinin su ilawa shankalong ba, mbara iso anan nsu nimon ule na anan nse ngadu na likawali, bara iyinnu nin nayi ashau.
Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
13 Bara kubi na Kutelle wa su Ibrahim ku likawali, a wa sillo nin litime, tunda na awasa a sillo nin mong ulenge na adi udiya ba.
Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
14 Ame woronghe “meng lallai mba tifi nmari, mba kuru nkpin ngbardang likurafe?”
“Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
15 Nanya nlo libau were Ibrahim nwanse ille imon na iwa su nghe likawali, kubi na awa cicah nanya hankuri.
Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
16 Bara anit dinsu isillin ninle na akatin nani nin gbardang, nanya namusu mine, isillin nnere imaline vat.
Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
17 Kubi na Kutelle wa yinin adurso nkanang udu kiti na nan ngadu nalikawali, imon nsali nsakisu ngegeme, nadlili me, awa ni uyinnu nin nisillin.
Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
18 Awa su nani bara imon ibba illenge na idin sakisu ba, nanya nilenge na udinin nijasi Kutelle su kinnu, arike alenge na tina chum udu kiti nyeshinu tiba se likara kibinayi timin uti nayi ulle na ina ceou bara arike.
Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
19 Tidimu nle uciu kibanayi, nafo ukessu nin likara ntabatu nidowo bite, uti kibinayi na uwa piru nanya kiti kuzeni kibulun.
Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
20 Yisa wa piru kiti kane, nafo unan npunu kibulun bite, amini wa da so upirist udiya sa ligan nin nbellun Malkisadak (aiōn g165)
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn g165)

< Ibraniyawa 6 >