< Uafisawa 4 >

1 Bara nanin meng fa, nafo kucin ncikilari ndin fo minu nachara, sun ucin imusun nllenge na yicila munu.
Ine monga wamʼndende chifukwa chotumikira Ambuye, ndikukulimbikitsani kuti mukhale moyo woyenera mayitanidwe amene munalandira.
2 Nin toltinu liti ichang, Ayi ashew, iseru anit vat nin suu.
Mukhale odzichepetsa kwathunthu ndi ofatsa; mukhale oleza mtima, ololerana wina ndi mnzake mwachikondi.
3 Suing ille imon na iba suu vat inan iso ligawe nan nya nbolu Kutellẹ nin lisosin limang.
Muyesetse kusunga umodzi wa Mzimu; umodzi umene umatimangirira pamodzi mu mtendere.
4 Kidowo kirum, duku, infip milau mirum, nafo na iwa yicilla munu nin likara kibineyi nin tikibineyi nyicilu.
Pali thupi limodzi ndiponso Mzimu mmodzi, monganso pali chiyembekezo chimodzi chimene anakuyitanirani.
5 Tidin cikilariuwa rum, uyinnu sa uyenu urum, usul sunu ulau urum,
Pali Ambuye mmodzi, chikhulupiriro chimodzi, ubatizo umodzi;
6 Kutellẹ kurum uchifing nvat, ame ulle na adi kitene vat, nan nya nvat a imon vat.
Mulungu mmodzi ndi Atate a onse, ndipo ali mwa onse.
7 Ina ni kogha ku nan nya bite, udu diu gbardang nafo na Kristi na guchu.
Koma aliyense wa ife wapatsidwa chisomo molingana ndi muyeso wa mphatso ya Khristu.
8 Nafo na uliru Kutellẹ na belling, kubi ko na awa ghana kitene kani, apizira ligozin nancin na idi nanya licin asuu anit mafilzunu filzunu.
Nʼchifukwa chake akunena kuti, “Iye atakwera kumwamba, anatenga chigulu cha a mʼndende ndipo anapereka mphatso kwa anthu.”
9 Ulle ullire pa, “Awa ghana kitene kani,” din nnufi nworu, se akuru a pira nan nya nchachom kutina?
Kodi mawu akuti, “Iye anakwera” akutanthauza chiyani, ngati Iyeyo sanatsikire kunsi kwa dziko lapansi?
10 Ame ullenge na ana tolu nchanchom kitin amere ullenge na anakuru aghana kitene nitene anan kullo imon vat.
Iye amene anatsika ndi yemweyo anakwera koposa mʼmayiko a kumwamba onse, ndi cholinga choti zinthu zonse zikhale zodzaza ndi Iye.
11 Yisa wasu nafilzinu filzinu fone: among nono kadura, anan nliru nin nnu Kutellẹ, anan nuchu nbellin uliru Kutellẹ, anan libiya, nin nan dursuzu.
Iye ndiye amene anapereka mphatso kwa ena kuti akhale atumwi ndi ena aneneri, ena alaliki, ndi ena abusa ndi aphunzitsi.
12 Bara inan kulo nanin nin nimon katah Kutellẹ bara kye kidowon Kristi.
Ntchito yawo ndi kukonza oyera mtima kuti agwire ntchito ya utumiki kuti thupi la Khristu lilimbikitsidwe.
13 Udu kubi ko na tima se umunu nati nan nya nyinnu sa uyenu nin yina ngonoo Kutellẹ. Tiduru likulung nnit nafo allenge ikuno nin yiru ngono Kutellẹ.
Izi zidzatifikitsa tonse ku umodzi wachikhulupiriro, kumudziwa Mwana wa Mulungu, kukhwima msinkhu ndi kufika pa muyeso wangwiro weniweni wopezeka mwa Khristu.
14 Udina ni natiwa libuung lisosin nafo nono. Allenge na ufunu din killu kiti nu ghinu anan yiru nbellu nliru nwultunu kiti.
Motero sitidzakhalanso makanda, ogwedezekagwedezeka ndi mafunde, otengekatengeka ndi mphepo iliyonse ya chiphunzitso ndi kuchenjera kwa anthu achinyengo amene amasocheretsa anthu ndi kuchenjera kwawo.
15 Tima bellu kidegen nan nya nsuu me, tinau kuno nan nya mme na amere liteh, amere Kristi.
Mʼmalo mwake, poyankhula choonadi mwachikondi, tidzakula mu zinthu zonse ndi kukhala thupi la Khristu, amene ndi Mutu, omwe ndi mpingo.
16 Ulle na nidowe nanan ndortine dofin kitine vat, nidowo mine munno tafat nan nati, naffo na kokome kubiri na ina fuloghe katane nan nya kitin nkunju kidowo, bare ukye nanit vat nan nya nsu.
Mwa Iye thupi lonse lalumikizidwa ndi kugwirana pamodzi ndi mitsempha yothandizira. Likukula ndi kudzilimbitsa lokha mwachikondi, pomwe chiwalo chilichonse chikugwira ntchito yake.
17 Bara nanere imon ille nan belling munu, indin dursu minu nan nya ncikilari: na iwaa lawan ncine nafo awurme ba nan nya katah mine kalan.
Tsono ine ndikukuwuzani izi, ndipo ndikunenetsa mwa Ambuye, kuti musayendenso monga amachitira anthu a mitundu ina potsata maganizo awo opanda pake.
18 Anan kpilizu nan nya nsirti. Alle na ina ina nutun nanin nan nya nlai kutellẹ bara utani ulle na udin nan nya mine nin gbas nibineyi mine.
Maganizo awo ndi odetsedwa, ndi osiyanitsidwa ndi moyo wa Mulungu chifukwa cha umbuli umene uli mwa iwo chifukwa cha kuwuma mtima kwawo.
19 Alle na itah gbas inani nnapka ati mine nan nya nimon izenzen nan nya nsuu nimon vat bara litime.
Popeza sazindikiranso kanthu kalikonse, adzipereka okha kuti akhumbe zonyansa, kuti achite mtundu uliwonse wa zoyipa ndi zilakolako zosatha.
20 Na nanere ina piziru uyinnu mbellen nKristi ba.
Koma inu simunadziwe Khristu mʼnjira yotere.
21 Andi ina lanza ikuru idursuzo minu ubelleng ise, nafo na kidegen di nan nya nKristi.
Zoonadi munamva za Iye ndipo munaphunzitsidwa mwa Iye molingana ndi choonadi chimene chili mwa Yesu.
22 Sa iyinin sa inari kalan unit ukuse ullenge na udi nin lidu likuse, na idin kpilzinu unanuzu nanya nrusuzu kiti nin suu liti.
Inu munaphunzitsidwa molingana ndi moyo wanu wakale, kuchotsa umunthu wakale, umene ukupitirira kuwonongeka ndi zilakolako zachinyengo;
23 Bara inan so apese nan nya nfulu ulau nibineye mine.
kuti mukonzedwe mwatsopano mʼmitima mwanu;
24 Shonon unit upese, ullenge na Kutellẹ. Nakye ghe libo nfiu Kutellẹ nin lau kidegen.
ndi kuti muvale umunthu watsopano, wolengedwa kuti ufanane ndi Mulungu mu chilungamo chenicheni ndi chiyero.
25 Bara nani, sunan kinu belleng atti kidigen, arik tigap kidowo kirumari.
Chifukwa chake, aliyense wa inu aleke kunama ndipo ayankhule zoona kwa mʼbale wake, pakuti ife tonse ndife ziwalo za thupi limodzi.
26 Assa ayi nnana munu na iwa ti kulapi ba, “Na iwa yinin uwui diu a iyita nin tinana naye ba.”
Kwiyani koma musachimwe. Dzuwa lisalowe mukanali chikwiyire.
27 Bara iwa ni shitan ku kiti.
Musamupatse mpata Satana.
28 Ullenge na adin suu likiri na awa kura asuu likire ba, nani na asuu katah katah kacine nin nachara me, anan se abuno unan diru.
Iye amene wakhala akuba asabenso, koma agwire ntchito ndi kuchita kenakake kaphindu ndi manja ake, kuti akhale ndi kenakake kogawana ndi amene akusowa.
29 Na uliru unanza nwa nuchu tinu mine ba, nworu nani, tigulang ticine to na tiba kye among alle na idin pizure, anan lanze nanse ubolu Kutellẹ.
Mʼkamwa mwanu musatuluke mawu aliwonse onyansa, koma okhawo amene ndi othandiza kulimbikitsa ena molingana ndi zosowa zawo, kuti athandize amene akawamve.
30 Na iwa lanza ufunu alau Kutellẹ ayi ba, ullenge na ina yaci minu ninge udu lirin tuchu.
Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu amene mwasindikizidwa naye chizindikiro cha tsiku la kuwomboledwa.
31 Nutunon vat ngbagbai nayi, tinan nayi tikhang, ughantizunu tiwui tinanza nin tizogo nutunong imon ine vat nin katahh kananzang.
Chotsani kuzondana, ukali ndi kupsa mtima, chiwawa ndi kuyankhula zachipongwe, pamodzi ndi choyipa chilichonse.
32 Suuug ayi asheu nin nati mine, nin ni beneyi ni nese, ishauza nin na lapi nati, nafo na Kutelle nan nyan nKristi na shawa nin na lapi bite sa ubizu.
Mukomerane mtima ndi kuchitirana chifundo wina ndi mnzake. Khululukiranani wina ndi mnzake, monga momwe Mulungu anakukhululukirani mwa Khristu.

< Uafisawa 4 >