< Katwa Nono Katwa 22 >

1 Bulus woro, “Akune na Yahudwa nan nuana ning, dinang atuf ilanza ile imon na nba bellu alenge na idin vurzi nliru nene!”
Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.”
2 Na ligozin nanite lanza Bulus nlirina nin lilem in Ibranaci, ita tik, itunna nlazughe. Bulus nin woro nani,
Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete. Kenaka Paulo anati,
3 “Meng wang ku Ibraniyawa, nafo anunghe. Iwa marue kipin Tarsus, nanya kusarin Sisiliya, Ama nna kunjo kikane in Urshalima. A ndutu gono, iwa yinnin ti duka to na Musa wani an kabite ku. Gamaliyari wadi unan dursuzui. Nwa dortu ti duka tone bara na nwadi nin su ndortu uliru Kutelle, meng tutung yiru anung vat wang din dortun toni ti duke.
“Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero.
4 Unare wati meng fo kidowo nkpazu nalenge na iyinna nin kadura Kutelle kitenen Yesu. Nwa pisuru tibau nmolsu nani. Vat kubi ko na nse nalilime sa awani alenge na yinna nin kadure, asa nta ito nani kilari licin.
Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende.
5 Udya na Prieste wa yiru nani, nanere wang inung anit alenge na iwadi nanya kudaru kudya na Yahudawa wa yiru. Iwa ni iyerte ndomun kiti nuana mine a Yahudawa na iwa di kipin in Damaskus. Mani ma yerte wa ni likara nwo ndo kikane nkifo kogha ku na ayinna nin Yesu. Asa nkifo nani, nnin yauna nani nafo acin udu Urushalima, inin di funuan.
Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.
6 Inin nya udu u Damaskos. Na nda kupopo Ndamaskus, kubi nikoro likure nin naba nwui, nmong nkanang tunna minuzu kitene susut ninmi.
“Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira.
7 Nkanaghe wadii kang ntunna ndeu kutiin. Ntunna nlanzaa liwui nmong din liru ninmi piit kitene kani, adin du, 'Shawulu! Shawulu! iyaghari nta udin yoyi?'
Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’”
8 In kawaghe, 'Feghari Cikilari?' A worei, 'Menghari Yesu un Nazeret, ulenge na udin yoghe.'
Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.”
9 Anit ale na iwa di nin mi yene nkananghe, ama na ilanza imon ilenge na liwuye wadin belle ba.
Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.
10 Meng tirino, 'Iyaghari udi ninsu nsufi Cikilari?' Cikilare worei, 'Fita upiru nanyan Damaskus. Umong unit di kikane na ama bellin fi vat imon ilenge na uma su.'
Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?” Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.”
11 Nkanang mone wadi kang na nkuru yene kiti ba, nkanang wati iduu. Inung anite naa iwa di nin mi kifo ucara ning inin wonu udu nanyan Daskuse.
Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.
12 Umong unit na lissame wadi Hananiyas da nda yeni. Ame unitari na awadin lanzu fiu Kutelle nin dortu tiduka na Yahudawa. Vat a Yahudawa na iwa sosin Damaskuse belle imon icine kitene me.
“Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu.
13 Ada adayissina kupo ning anin woro, 'udondon ning Shawulu, 'tunna nyenju tutung!' Ntunna yenju, nyeneghe ayissin kupo ning.
Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.
14 Atunna aworoi: 'Kutelle kurika nati dighe nsujada, a kurika na acif bite na sughe usujada na fere fi amanin dursu fi imon ile naa adi nin su usu.
“Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake.
15 A dursofi unan katwa kalau warum, Yesu Umasiya, Uminin kuru ulanzaghe din liru litime.
Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva.
16 Bara nani nene yenje uwa molu kubi? Fita nshitinfi nmyen ushitinu ulau, unin su nlira nanya lissan Yesu Cikilari utiringhe akusufi alapi fe!'”
Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’
17 Na nkpilla Urushalima. Nlonliri ndo kutii nlira kudya, ntunna nlira, na nwadi nanyan lire kikane, nse litining nanya namoro.
“Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka.
18 Cikilare lirina ninmi, aworoi, 'Yenje uwa so kiti kane! Suna Urushalima nene, bara anite kikane mayinnu nin nimon ile na uma bellu nani liti nighe ba!'
Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’”
19 Ama meng woroghe, ' Cikilari, iyiru nwo meng nacinu atii nlira adidya kang in pizuru nalenge na iyinna ninfi. Alenge na nse iyinna ninfi, meng wati itiza nani nilari licin, in wadin fonani wang.
Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu.
20 Idin lizinu nin kubi ko na iwa molu kucin fe Istifanus, meng wayissin kite ndin yenjee nkuru na nani uyinu ning kitene nimon ile na iwadin sue. Meng tutung wang wadi nca nimoon ilenge na anan molume wa kala iceo kusari kurum!'
Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”
21 Ama Cikilare woroi, 'Kayi, yenje uwa so kiti kane! Suna Urushalima, bara meng matufi piit nin kiti kane udu kiti namon anit, na idi a Yahudawa ba!'”
Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”
22 Anite wadin lanzu Bulus ku nlire se na iwa lanza Cikilarin toghe kiti namong anit. Itunna ighanan jartuzu, “Molonghe! Na acaun uso nin lai tutung ba!”
Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”
23 Na iwa di nanya jaartuze, ikalza altuk kitene mine inin fizza lidau kitene kani, uleli ute din durru tinanayi mine.
Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba,
24 Udya mine tunna ata iyaun Bulus ku iteghe nanya kilari licin. Aworo nani ikpizu Bulus ku anan belle imon ile na ata inanza a Yahudawa ayi kang nani.
mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere.
25 Inin tunna inakpa acara me itereghe nnunwo ikpizughe kimal me. Ama Bulus belle kusoja kupome, “Uma patilunu uduka andi ukpizai, kunan Rumawa, urika na umong nsa do ninghe kilarin shara akpaghe nin kulapi ba!”
Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”
26 Na kusoje nlanza nani, ado kitin dya mine adi bellinghe. Aworo ndya nasoje, “Ule unite kunan Rumawari! Iyiru dai na uwasa utanari ti kpizoghe ba!”
Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”
27 Udya nasoje da ada woroghe, “Belli, fe kunan Rumawari?” Bulus woroghe “e-e.”
Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?” Paulo anayankha kuti, “Inde.”
28 Udya nasoje kawaghe aworo, “meng se nin nikufun gbardanghari inase uso kunan Rumawa.” Bulus woroghe, “Meng kumat in Rumawari.”
Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.” Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”
29 Anit ale na iwa cinu udun tirighe tipinpin tunna isughe deidei. Ame udya nadidya nasoje wang fiu wa kifoghe, kube na awal anza Bulus kunan Rumawari, bara na ame wa terughe.
Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.
30 Ukurtunun nkuye, udya nasoje wadi nin su alanza kidegen nvurzun liru ule na a Yahudawe dumun' kitenen Bulus. Bara nani abuku time, anin ta udya na Prieste nin vat kudaru me izuro. Anin da nin Bulus aceughe in kitik mine.
Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.

< Katwa Nono Katwa 22 >