< Katwa Nono Katwa 19 >

1 Na Apolos wadi korint, Bulus cino Firiziya nin Galantiya anin kata udu u Asia, amini wa kwilin udu Efisus. Anin zuro nin namong i woroghe inin ma anan yinusauyenuri.
Apolo ali ku Korinto, Paulo anadutsa mʼmayiko a ku mtunda ndipo anafika ku Efeso. Kumeneko anapeza ophunzira ena.
2 Atirino nani, “Inaseru Ufunu Ulau kubi kona ina yinin nin liru Kutellẹ? Inanin wa kwanghe iworo natina seru ba. Na tina lanza Ufunu Ulau ba”
Iye anawafunsa kuti, “Kodi munalandira Mzimu Woyera pamene munakhulupirira?” Iwo anayankha kuti, “Ayi, ife sitinamvepo kuti kuli Mzimu Woyera.”
3 Bulus tirino, “Na iwa shintin minu ushitunu ulauwe, iyaghari iwa yinin?” Inanin wa belinghe,”Tina yinin nin ilemon na Yohana unan su baptiszima na dursuzo”
Tsono Paulo anawafunsa kuti, “Nanga munabatizidwa ndi ubatizo wotani?” Iwo anati, “Ubatizo wa Yohane.”
4 Bulus woro(belle), “Yohana na sulsun(baptizpsima) anit alena ina chinu matiza ma nanzan. Amini wa belin anite i yinin nin lena ama dak amini na malin da ninkidun uleli unite amare wa di Yesu.”
Paulo anati, “Ubatizo wa Yohane unali wa kutembenuka mtima. Iye anawuza anthu kuti akhulupirire amene amabwera, ameneyo ndiye Yesu.”
5 Na anit ane lanza, inani wa su nanin ushitunu nmyen nanya lissan Cikilari Yesu.
Atamva zimenezi, anabatizidwa mʼdzina la Ambuye Yesu.
6 Na isunani, Bulus tarda acarame kitene nati mine, likara Nruhu Ulau tolo nati mine. Uruhu Ulau nanani likara liru nin ton tilem to na inayiruba, inani tutung wa bellu kadura kanga na Uruhu Ulauwe wa belle nanin.
Pamene Paulo anawasanjika manja, Mzimu Woyera anadza pa iwo ndipo anayankhula mʼmalilime ndipo ananenera.
7 Iwadi anit likure nin nan waba na Bulus wa shintin nani nmyen (Ubaptisima) isere Uruhu Ulau.
Anthu onsewo analipo khumi ndi awiri.
8 Tipui titat wa kata, Bulus pira kitin zursu na Yahudawa nanya Afisus ko ayame Asabbat a dursuzo nani nin risu nani kitenen Yesu nin yizari Kutellẹ ma dursu litime amere Ugo.
Paulo analowa mʼsunagoge ndipo anayankhula molimba mtima kwa miyezi itatu, kuwatsutsa mowakopa za ufumu wa Mulungu.
9 Na among a Yahudawa wa yinin nin kadure ba, na iwa di ninsu ilanza tutung ba. Inani wa yitan gwondulu nbellu nimong inanzan kitene nimon ile na Bulus wadi dursuzu nani. Bara nanin Bulus cino nanin ayira anan bi ninghe idi zuro kitin zursun Tiranus.
Koma ena anawumitsa mitima; anakana kukhulupirira ndipo ananyoza Njirayo pa gulu la anthu. Kotero Paulo anawasiya. Iye anatenga ophunzirawo ndipo amakambirana tsiku ndi tsiku mʼsukulu ya Turano.
10 Bulus tah akus aba ndursuzu nanite kikane. Nanya nani, ngbardang na Yahudawa ni nalege na iwadi a Yahudawaba, arika na iwa sosin nanya kusarin Asiya inin lanza kadura kitenen Cikilari Yesu.
Izi zinachitika kwa zaka ziwiri, kotero kuti Ayuda onse ndi Agriki amene amakhala ku Asiya anamva Mawu a Ambuye.
11 Kutellẹ tutung wa ni Bulus ku likara su nimong izikiki.
Mulungu anachita zodabwitsa zapadera kudzera mwa Paulo.
12 Alena iwa dinin tikonu na ise udak kitin Bulus ba, vat kupori ko na Bulus ndudo, asa iyira idi tarda kitenen nan konu, iba shinu uruhu unanzanghe sun nani.
Kotero kuti mipango yopukutira thukuta ndi yovala pogwira ntchito, zomwe zinakhudza thupi la Paulo amapita nazo kwa odwala ndipo amachiritsidwa ndiponso mizimu yoyipa mwa iwo imatuluka.
13 Kikane tutung among a Yahudawa wadi diku na iwacinu nigbiri nigbiri, inanin wa ko tiruhu tinanzanghe nanya nani nite. Among a Yahudawa wa belu tiruhu tinanzanghe nuzun nanya nanite inin din bellu, “Indin bellu minu nuzun nanya likaran Cikilari Yesu, ulena Bulus na dursuzo nari kiteneme!”
Ayuda ena amene ankayendayenda kutulutsa mizimu yoyipa anayesa kugwiritsa ntchito dzina la Ambuye Yesu pa amene anali ndi ziwanda. Iwo popemphera amati, “Ine ndikulamulira utuluke, mʼdzina la Yesu amene Paulo amamulalikira.”
14 Iwadi anit kuzora katwa kane. Asaun nmong unitari lissame wadi Sikava, ku Yahudawa, ulena awadin yiccu litime udya na prist.
Amene ankachita zimenezi anali ana asanu ndi awiri a Skeva, mkulu wa ansembe wa Chiyuda.
15 Nlonliri ileo ubun kata kane, uruhu unanzanghe nari unuzu kitin nute. Uruhu unanzan woro nanin,”In yiru Yesu ku, nyiro Bulus ku, tutun na umong nani likara ida ti imong imong ba!”
Tsiku lina mzimu woyipa unawayankha kuti, “Yesu ndimamudziwa ndiponso Paulo ndimamudziwa, nanga inu ndinu ndani?”
16 Nin belu nanin, kwak unit ulena awa dinin uruhu unazanghe tinna ayina adeu kitenen na saun Sikeve. Amini wa fọ nanin kap a lanza nanin ukule. Anin wa jarza nani imon. Ilanza fiu itina inuzu kilare icoo.
Pamenepo munthu amene anali ndi mzimu woyipa anawalumphira nawagwira onse. Iye anawamenya kwambiri, kotero kuti anathawa mʼnyumbamo ali maliseche, akutuluka magazi.
17 Kap nanit alena iwa sosin nan nya Ephisus, vat a Yahudawa nin nalena a Yahudawa iwa lanza ulemone. Imini wa tinna ilaza fiu bar unit ulena ufunu unanzan wa di nan nya me awa dinin likara kan. nin kubi kurume, iwa zazin lisa Ugo Isa.
Ayuda ndi Agriki okhala ku Efeso atamva zimenezi, anachita mantha, ndipo anthu anachitira ulemu dzina la Ambuye Yesu koposa.
18 Nan nya kubi kone, among anan yinnusauyenu iwa latisze, anan yinusauyenu gbardan benle ilemong inanzan na idin suzu.
Ambiri a iwo amene tsopano anakhulupirira anafika ndi kuvomereza poyera ntchito zawo zoyipa.
19 Among anite na iwa di anidibere tina inutuzuno umon kata mine itinna i juju kika na koghe mayen. Dana anit munu ikurfun ilena imong zuzu nikulume ikurfun duru amui akuta atau.
Ambiri amene amachita za matsenga anasonkhanitsa mabuku awo pamodzi nawatentha pamaso pa anthu onse. Atawonkhetsa mtengo wa mabukuwo, unakwanira ndalama zasiliva 50,000.
20 Nan nya nanin, anit gbardan lanza tipipin kitenen Ugo Isa inanin wa yininsauyenu.
Kotero Mawu a Ambuye anapitirira kufalikira ndipo anagwira ntchito mwamphamvu.
21 Unuzu kidun Bulus mala katame nan nya ifisus, Ufunu Ulau yira ghe ayinin udu Urshalima, tutun nin funu a pira kusarin Macidonia nin Achaia anan yene anan yinusauyenu. Bulus woro, “Nin kidun andin duo Urshalima, ma kuru iduo Uroma tutun”
Zonsezi zitachitika Paulo anatsimikiza zopita ku Yerusalemu kudzera ku Makedoniya ndi ku Akaya. Iye anati, “Kuchokera kumeneko, ndiyenera kukafikanso ku Roma.”
22 Amini watu iyichila awa bã anan bungh, Timontawus nin Erastus, udu Macidonia. Tutun Bulus ninsọ nan nya ka gbir, Efisus kusarin Asia.
Iye anatuma anthu awiri amene amamuthandiza, Timoteyo ndi Erasto ku Makedoniya, pamene iye anakhalabe ku Asiya kwa kanthawi.
23 Nin deadai kidun nanin, anit nan nya Efisus chizina ubunkurnu kiti kan bar Isa nin madursuzu kitene me.
Pa nthawi yomweyo panachitika chipolowe chachikulu chifukwa cha Njira ya Ambuye.
24 Kikane umong unit wa diku nin lisa Damarius. Awake kuguinki nin lisa Diana. Damarius wadin sesu ikurfun kiti nanit ka nin kani kata makeke ku guinki asa nin lewe manin.
Mmisiri wantchito zasiliva, dzina lake Demetriyo, amene amapanga mafano asiliva a Atemi ankabweretsa phindu lalikulu kwa amisiri a kumeneko.
25 Darius nin yichila adonkata makeke na guinke. Anin woro nanin,”Anit, iyiru kata kanere tidin sesu ikurfun bit ka.
Iye anasonkhanitsa pamodzi amisiriwo, pamodzinso ndi anthu ena ogwira ntchito yomweyo ndipo anati, “Anthu inu, mukudziwa kuti ife timapeza chuma chathu kuchokera pa ntchito imeneyi.
26 Iyiru Bulus ulena asosin nan nya Efisu ana dursuzo anit gbarde na iwa seru ma guinkibit ba mana tinake. Nene ma anit gbardan unuzu kusari ni gbiri nan nya kusari bit na idu sesu nimong ilena tike ba. Bulus na bellin anite atellẹ alena ti din zazunu ah atellẹ riba nin nanin na tiwa zazu anin ba.
Ndipo inu mukuona ndi kumva kuti munthu uyu Paulo wakopa ndi kusokoneza anthu ambiri a ku Efeso ndiponso pafupifupi dziko lonse la Asiya. Iye akunena kuti milungu yopangidwa ndi anthu si milungu ayi.
27 Andi anit lazaghe imati anit malesu lesu bite yisin. Anite mayenu na idinini su idak kiti bite ba tutun nin dak kuti Diana inan su uzazunume. Anite mayenu Diana di udiah ba. Tutun vat anit kusarin Asia nin uyeh kap ma chinu uzazughe.
Choopsa ndi chakuti sikungowonongeka kwa ntchito yathu yokha ayi, komanso kuti nyumba ya mulungu wamkulu wamkazi Atemi idzanyozedwa ndipo mulungu wamkazi weniweniyo amene amapembedzedwa ku Asiya konse ndi dziko lapansi, ukulu wake udzawonongekanso.”
28 Vat anite kikane tinna ilaza ayi nin Bulus dana ilaza ilemong na Damarius belle. Inani wa tinin jarttiz, “Diana kutellẹ bite Efisu di gbardan”
Atamva zimenezi, anakwiya kwambiri ndipo anayamba kufuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi.”
29 Anite kan nan nya kagbiri ilaza ayi nin Bulus ini tinna jarttizu. Among anit kifọ Gaius nin aAristachus, inin na bąh jnuzu Macidonia iwa di ana chin nin Bulus. Ninnanin anite kap tinna chium, nin wunu nani udu kikana anan ka gbiri asa isu avuku(theater)
Nthawi yomweyo mu mzinda wonse munabuka chipolowe. Anthu anagwira Gayo ndi Aristariko, anzake a Paulo a ku Makedoniya, ndipo anathamangira nawo ku bwalo la masewero.
30 Bulu wadinin su adue nan nya kiti navuh anan lirina nin nanite, vat nin nanin anan yinusauyenu tinna iwantinghe udu kikane.
Paulo anafuna kulowa pakati pa gulu la anthu, koma ophunzira anamuletsa.
31 Among ago kagbiri na iwa di adondon Bulus ilanza ilemon na idin chi. Inanin wa tu umong kitin Bulus na wa dak nan nya kiti kuti navuaba.
Ngakhale olamulira ena aderalo, amene anali abwenzi a Paulo, anatumiza uthenga kumuletsa kuti asayesere kulowa mʼbwalomo.
32 Lipitin nanite nan nya kuti na vua ilebun jarttizu. Among wadin jarttizu ni momong dabam among tutun jarttizu dabam. Tutun among nan nya mine wa yinin umon elena iwa din jarttizumuba.
Munali chisokonezo mʼbwalomo pakuti ena amafuwula zina, enanso zina. Anthu ambiri sanadziwe ngakhale chomwe anasonkhanira.
33 Umong kuYahudawa lisa me wadi Alezanda. Among a Yahudawa turughe udu bun nanite inin tahghe alirin. Alezanda tinna ah antina ucharame anan tah nanin ichin ujattuzu. Aaadinin su a bellin nanin a Yahudawari ba nati macharantki(troble)
Ayuda anamukankhira Alekisandro kutsogolo, ndipo ena anafuwula kumulangiza iye. Iye anatambasula dzanja kuti anthu akhale chete kuti afotokozere anthu nkhaniyo.
34 Tutun among alena iwadi a Yahudawariba iyino Alezanda ku Yahudawari inin yinno a Yahudawa din zazunu Diana kutella ba.”
Koma pamene anthuwo anazindikira kuti ndi Myuda, onse pamodzi kwa maora awiri anafuwula kuti, “Wamkulu ndi Atemi wa ku Efeso!”
35 Nin nanin umong ugo ka gbiria ta lipitnpin nanit chin ujarttizu. Anin belle nanin, “Linananin anan min, koghe yiru nan nya yiulele kutellẹ bite Diana na diu unuzu kitene!
Mlembi wa mzindawo anakhazikitsa bata gulu la anthuwo ndipo anati, “Anthu a ku Efeso, kodi ndani pa dziko lonse lapansi amene sadziwa kuti mzinda wa Efeso umayangʼanira nyumba ya mulungu wamkulu Atemi ndi fanizo lake, limene linagwa kuchokera kumwamba?
36 Koghe yirumu kap, na umong batin aworo ilemonghe kiden ari ba. Bar nanin na kgha ti tik nene. Naiwa su imomong inazan ba.
Chifukwa chake popeza zinthu izi palibe amene angazikane, inu mukuyenera kukhala chete osachita kanthu kalikonse mofulumira.
37 Na iwa danin awa ba ane kikane ba, bar na isu imomong inazan ba. Na idua nan nya na danga bit inin yira imong unuzu kikane, tutun na ilirina imommo inanzan kitene kutellẹbit.
Inu mwabweretsa anthu awa pano, ngakhale kuti iwo sanabe mʼnyumba zathu zamapemphero kapena kunenera chipongwe mulungu wathu wamkazi.
38 Bari nanin, andi Damariu nin na nan katame dininsu i ni kogha ku kulapi su imong nanza, na su libau lichine. kika kitin wuchu kidenghe iwawngha idu, kikane anan wuchu kiden duku na ugamnati na fere nanin. Iwangha kifo koghaku idoamu kikane.
Ngati tsono Demetriyo ndi amisiri anzake ali ndi nkhani ndi munthu wina aliyense, mabwalo a milandu alipo, oweruza aliponso. Akhoza kukapereka nkhaniyo kwa oweruza milanduwo.
39 Tutun andi idinin su tirinu imomong, iwangha itirino ago mine inan yene ilemong na imasu kitene andi izuro kitikirum.
Ngati mukufuna kubweretsa kanthu kali konse, ziyenera kukatsimikizidwa ndi bwalo lovomerezeka.
40 Uzuru ulene uchauba ba! Yiran ubukurnu kiti kane libau lichine bar arik dinisu ti lanza ayi igomnati ba. Adi ago tiri ni majarttizu man, men waghe ikwana nanin gigime ba.”
Monga mmene zililimu, ife titha kuzengedwa mlandu woyambitsa chipolowe chifukwa cha zimene zachitika lerozi. Motero ife sitingathe kufotokoza za chipolowechi popeza palibe nkhani yake.”
41 Nanere ugo ka gbiri wa belin lipitirunu anite. Amini wa belin kogha ku a kwilin kilarime, inanin wa kwilizin nilarimine.
Iye atatha kunena zimenezi anawuza gulu la anthulo kuti libalalike.

< Katwa Nono Katwa 19 >