< 2 Utasalonika 1 >

1 Bulus, Silvanus, nin Timoti udu kutii kulau nTassulinika nya Kutelle Uchif nin Cikilari Yesu kristi.
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Kulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu.
2 Na nshew nin mang se kiti kutellle uchif bit nin cikilari n isa kristi.
Chisomo ndi mtendere kwa inu kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.
3 Ti ba godo kutelle ko kishii bara anun, linuana, uchaun. Bara kidegen mine din kunju kang, tutung usuu mine bara linuana karin kan.
Ife tiyenera kuyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu abale. Ndipo tiyenera kutero chifukwa chikhulupiriro chanu chikukulirakulirabe, ndiponso chikondi chimene aliyense wa inu ali nacho pa mnzake chikuchulukirachulukirabe.
4 Arik din fo nigiri nin nanun nya natii alau Kutelle bara unonku nibinei nin kidegen mine nyan nieu we na itere nibinei mine.
Nʼchifukwa chake, timayankhula monyadira mʼmipingo yonse ya Mulungu za kupirira kwanu ndi chikhulupiriro chanu pakati pa masautso onse ndi mayesero amene mukudutsamo.
5 Ilele udursun sharaa Kutelle ulau, nin nilee imon na iba dak lbata minu nya na iba piru kilari Kutelle na idin nieu bara kinin.
Zonsezi zikutsimikiza kuti Mulungu amaweruza molungama. Zotsatira zake ndi zakuti mudzatengedwa kukhala oyenera kulowa mu ufumu wa Mulungu umene mukuwuvutikira.
6 Udi lau Kutelle kurtun unieu udu alenge na ita minu uniew,
Mulungu ndi wolungama ndipo adzalanga amene amakusautsaniwo
7 nin fi-nu alenge na ina nieu nan nari, asa Cikilari ta dak nin nono ka taah me nya na kara.
ndikukupatsani mpumulo amene mukusautsidwa, pamodzi ndi ifenso. Izi zidzachitika Ambuye Yesu akadzaoneka mʼmalawi amoto kuchokera kumwamba pamodzi ndi angelo ake amphamvu.
8 Nya la aba kurtunu alenge na iwa yiru Kutelle kuba, nin na lenge na iwa seru kadura kamang Cikilari Yesu ba.
Iye adzalanga amene sadziwa Mulungu ndi amene samvera Uthenga Wabwino wa Ambuye athu Yesu.
9 Iba nieu ukpizu nin kul sa ligan nbun Cikilari nin zazinu na kara me. (aiōnios g166)
Adzalangidwa ndi chiwonongeko chamuyaya ndipo sadzaonanso nkhope ya Ambuye ndi ulemerero wamphamvu zake (aiōnios g166)
10 Asa adaa nloli liri na alau ba zazin gne, alenge na iwa yinin nin gne iba punu tinuu vat bara ile inom na tiwa belin iwa yinin.
pa tsiku limene iye adzabwera kudzalemekezedwa mwa oyera mtima ndi kuyamikidwa ndi onse amene anakhulupirira. Inu mudzakhala nawo mʼgulumo chifukwa munakhulupirira umboni wathu.
11 Bara nene ti di minu nlira ko kishii, Kutelle bite seru uyi chilu mine, a nin kulo imon ichine na idin piziru nya kataah kidegen nin na kara.
Nʼchifukwa chake timakupemphererani nthawi zonse, kuti Mulungu wathu akusandutseni oyenera mayitanidwe ake, ndi kuti mwa mphamvu zake akwaniritse cholinga chanu chilichonse chabwino ndi chilichonse chochitika mwachikhulupiriro.
12 Bara lisan Cikilari bite isa se uzazinu mine, bara ame, bara nshew Kutelle bite nin Cikilari Yesu Kristi.
Ife timapempherera zimenezi kuti dzina la Ambuye athu Yesu lilemekezedwe mwa inu, ndi inu mulemekezedwe mwa Iyeyo. Zonsezi zidzachitika chifukwa cha chisomo cha Mulungu wathu ndi Ambuye Yesu Khristu.

< 2 Utasalonika 1 >