< 2 Bitrus 3 >

1 Nene, In nyerten minu, anan su nayi ning, kongo kubaga ni nyerte kun ba kunan ghantina nibinai nicine mine,
Inu okondedwa, iyi ndi kalata yanga yachiwiri kwa inu. Ine ndalemba makalata onse awiri kuti ndikukumbutseni ndi kukutsitsimutsani ndi cholinga choti muzilingalira moyenera.
2 bara inan lizino ulirue na iwa belin minu uworsu tinuu na nan nliru nin nuu Kutelle mbeleng ndukan Cikilari nin nan tucu unuzun nono kadura fe.
Ndikufuna kuti mukumbukire mawu amene anayankhulidwa kale ndi aneneri oyera mtima ndiponso lamulo limene Ambuye ndi Mpulumutsi wathu analipereka kudzera mwa atumwi.
3 Tun yinnon ilele, anan rusuzu kiti ma dak ida rusuzu minu nan nya nayiru nimalin, ima dortu imon ntok nibinai mine,
Poyamba mudziwe kuti mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, adzanyoza ndi kutsata zilakolako zawo zoyipa.
4 ima woru, “Ani uciu nliru nkuru nkpillu me din we? A cif bite na kuzu, ama imon du nafo ubur nu nkye in yie.”
Iwo adzati, “Kodi suja Ambuye analonjeza kuti adzabweranso? Nanga ali kuti? Lija nʼkale anamwalira makolo athu, koma zinthu zonse zili monga anazilengera poyamba paja.”
5 Ina shawa ilele nin su nibinai mine, nworu i wa kye kitene kane nin kutyin ne unuzu nan nya nmyenari nin myen, uworsu, nin liri nnuu Kutelle,
Koma iwo akuyiwala dala kuti Mulungu atanena mawu, kumwamba kunakhalapo ndipo analenga dziko lapansi ndi madzi.
6 a ubellu nnuu me nin myen uyie kubi kone, nmyen wa hiru, uwa nana.
Ndi madzinso achigumula, dziko lapansi la masiku amenewo linawonongedwa.
7 Kitene kane urume, ina ceo bara ula unuzuri bellun nliru urume, ina ceo bara lirin shara nin molu na nan salin dortu Kutelle.
Dziko la kumwamba ndi lapansi la masiku ano akulisunga ndi mawu omwewo kuti adzalitentha ndi moto. Akuzisunga mpaka tsiku limene adzaweruza ndi kuwononga anthu onse osapembedza Mulungu.
8 Na ulele nwa nuzu nibinai mine ba, anan su nayi ning, liri lirun kiti Ncikilare masin akus limui yari, a akus limui nafo liri lirun mari.
Koma abale okondedwa, musayiwale chinthu chimodzi ichi: Kuti pamaso pa Ambuye tsiku limodzi lili ngati zaka 1,000, ndipo zaka 1,000 zili ngati tsiku limodzi!
9 Na Cikilare di shankalong nbelen nciu nliri me ba, nafo na among din su adi shankalong, ama adi nin kune kuneari nin ghinu. Na adi nin su umon mine nana ba, ama adi nin su ani kubi nwooru vat sun alapi mine.
Ambuye sazengereza kuchita zimene analonjeza, monga ena amaganizira. Iwo akukulezerani mtima, sakufuna kuti aliyense awonongeke, koma akufuna kuti aliyense alape.
10 Vat nani, liri Ncikilare din cinu na udak nkiri. Kiitene Kutelle ma katu nin liwui ligberere. Imon vat ima juju nin la, uyie nin nitwa nnin ima su unin ushara.
Koma tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala. Pa tsikuli zinthu zakumwamba zidzachoka ndi phokoso lalikulu. Zinthu zonse zidzawonongedwa ndi moto, ndipo dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzapsa.
11 Andi ima musuzu imon ilele vat nane, imus na yapin anitari i kamata i yita? bara lissosin lilau nin katwa kacine.
Popeza kuti zinthu zonse zidzawonongedwa motere, kodi inu muyenera kukhala anthu otani? Muyenera kukhala moyo wachiyero ndi opembedza Mulungu
12 Tizan mas nan nya nca liri Kutelle, na kitene Kutelle ima juju nin la a vat nimon ile na idiku ma nutuzu nin piu nle.
pamene mukuyembekezera tsiku la Mulungu ndi kufulumiza kufika kwake. Pa tsiku limeneli zinthu zakumwamba zidzawonongedwa ndi moto, ndipo zidzasungunuka ndi kutentha.
13 Vat nani, nan tissu uca Kutelle kupesse nin yii upesse na ana ceo nari uliru mun, ulenge na anan katwa kacine ma so ku.
Koma ife tikudikira kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano, zimene Mulungu analonjeza, mʼmene chilungamo chidzakhalamo.
14 Bara nani, anan su kibinai ning, tun da na idin ca nile imone, yitan nin kanyir kang ise minu na nin na lap sa ndinong ba, inin se minu issosin mang nan ghe.
Chomwecho okondedwa, popeza inu mukudikira zimenezi, chitani changu kuti mukhale wopanda chilema kuti mukhale pa mtendere ndi Iye.
15 Yiran ayi asheu Ncikilari bite, unan kadura Kutelle Bulus na nyerten minu, nan nya kujinjing ko na iwa nighe.
Zindikirani kuti kuleza mtima kwa Ambuye kukutanthauza chipulumutso, monga momwe mʼbale wathu wokondedwa Paulo anakulemberaninso ndi nzeru zimene Mulungu anamupatsa.
16 Bulus nasu uliru nilenge imone nan nya ninyerte me vat, nan nya imong imon na yitu nin likara nworu iyining. Ale na nono katwa wari ba a na nibinai mine di kiti kirum ba ma shogulu ile imone, nafo na ina su umong uliru Kutelle udu ukul mine.
Iye walemba chimodzimodzi makalata ake onse, kuyankhula za zinthu izi. Mʼmakalata ake mumakhala zinthu zina zovuta kuzimvetsa, zimene anthu osadziwa ndi osakhazikika amazipotoza, monga amachita ndi malemba ena onse, potero akudziwononga okha.
17 Bara nani, anan su kibinai ning, tun da na iyiru ile imone, minon ati mine gegeme bara iwa wulttun minu nin liru kinu na nan salin lanzu fiu kutelle i fillo un min uyinnu sa nyenue.
Nʼchifukwa chake, abale okondedwa, popeza mukuzidziwa kale zimenezi, chenjerani kuti musatengeke ndi zolakwa za anthu osaweruzika, mungagwe ndi kuchoka pamalo otetezedwa.
18 Ama kunjon nan nya nbolu Kutelle nin yirun Ncikilari bite a unan tucu biite Yisa Kristi. Na ngongong so min me nene udi duru saligang. Uso nani! (aiōn g165)
Koma kulani mu chisomo ndi mʼchidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. Kwa Iye kukhale ulemerero tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)

< 2 Bitrus 3 >

The World is Destroyed by Water
The World is Destroyed by Water