< 2 Bitrus 1 >

1 Simon Bitrus kucin nin gono kadura in Yesus Kristi, uncindu kita na lenge na ina seru uyinnu sa uyenu ucine urume nan ghiruk, uyinnu sa uyenu nan nya katwa kacine Kutelle in Yesus Kristi.
Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
2 Na ubunu Kutelle so nan ghinu, na lissosin limang in yiru Kutelle kpin nan nya mine nnuzu in Yesu cikilari bit.
Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
3 Nafo imon likara Kutelle vat in lai nin fiu Kutelle in niari unuzu in yiru Kutelle, ulenge na ana yicila nari nan nya ngigibg nin lidu licine.
Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
4 Nan nyan ni lele, ana niari ucinu nnuu un likara ucine. ana su nani ti nan so anan se nikop nan nya nidowo kitene, kimal na ina se usurtu nnuzu likara linanzang nin su nimon yii.
Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
5 Bara imon irum ilele, shonon ati nsu nimon icine nan nyan in yinnu sa uyenu nin su katwa kacine nin yinu.
Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
6 Nan nya in yru seu uminu nati, nan nya nminu nati sen uteru nayi nan nyan teru nayi, yitan nin fiu Kutelle,
Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
7 nan nya fiu Kutelle yitan nin su linuana, nan nya nsu linuana yitan nin su nati.
Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
8 Asa ile imone di nan nya mine, idin kunju nan nya mine, na ima yitu are ba sa anan sali mumat nan nyan in yirun in cikilari Yesu Kristi.
Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
9 Ama ulenge na a dira ilenge imone, adin yenju imon ile na idi susutari cas; adi udu. Ame nshawa ukusu nalapia kuse me.
Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
10 Bara nani, linuana, shonon ati it uyiculu mine nin feru mine durso nati mine. Asa idn ile imone, na ima tirzu ba.
Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
11 Bara nani mmari midya wari mma niminu nan nya kilari tigo. Ncikalari bite nin nan tucu Yesu Kristi. (aiōnios g166)
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios g166)
12 Bara nani, ko nin shi mma lizizin muni ile imone, in yiru iyiru inin, idi nin nakara nan nya kidegene nene.
Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
13 Ndin yenju kubi nda dert nzunzun minue nlizun minu nbelen nile imone, ligang lissosin ning nan nya kudanga kone.
Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
14 Bara meng yiru nine men ma kalu kadanga nghe, nafo na cikilari bite Yesus Kristi na dursoi.
chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
15 Meng ba su ligan. ....? nighe, bara anughe inan lizizino ilenge imone kimal nnyiu nighe.
Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
16 Bara na arik wa dortu ti beliu minu gegeme ba ubeleng likara nin dak ncikilari bite Yesu Kristi, ama ti wa ti iyizi nba in yenun gongong me.
Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
17 Bara awa seru kiti Kutelle ucife uzazunu nin gongong na liwui wa nuzu kitene kani nin likara nin gongong li woro, “Ulengene usaun nighari, unan su nayi ning, ulenge na ayi ning di nin su me kang.”
Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
18 Ti wa lanza liwui tone na liwa nuzu kitene Kutelle: na tiwa di ligowe nan ghe kitene kikup liau.
Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
19 Ti di nin lirun anabci ulenge na uso kidegen, ulenge na ucara i ceo unin umasin nafo ula na uta kanan nan nyan kitin sirti na kwuidinding nda fiini nkwuidinding nta nkanang nibinai mine.
Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
20 Tun cizinan i yining ulele, nworu anabci ale nainyertine na udin nuzu nkpilizu nnan liru nin nin Kutellere litime ba.
Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
21 Bara na amon anabci na dak unuzu nkpilizu unit ba, ama anitari Uruhu din dortu nin ghinu i pila ulirue i bele uning.
Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

< 2 Bitrus 1 >