< 2 Ukorintiyawa 10 >

1 Meng Bulu, men litinin din fuo minu acar, bara utoltinu liti nin sheu in Kristi na men na kifo kubi kona iwa di nan ghin, bara indin fuo figiri ni ghinu kubi kona indi nan ghinu ba.
Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
2 Idin fuo minu acar, na iwadi nan ghin, na ina yitya in pun figiri nin nayi ale na uca, bara mma yinu ba nin na le na iworo arik tin cin nanya kidawo.
Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
3 BAara na tidin cin nanya kidawo, aina likum bite kin kidawari ba.
Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
4 Bara imong kabung bite in kidawari ba. Bara nanin ti dini nimong likara kitene na nazu adadu likar, na idin dasu nin ma yartdan ma hem '
Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
5 Tutung tidin nanzu vat nimon ile na imafitu kitene Kutell, tiyiru vat nkpilzu usu kucin nruu Kristi.
Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
6 Tidin caa ubucu vat nittwa isalin ni liti iwase ati uni nati mune ukulo
Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
7 ilemong na idi cana ibunmine. Andi umong yina ayita nafo Kristi na yita nafo Kristiare wang.
Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
8 Bara na inwa riu figiri kang mbelin g likara bite lo na Ucif wani ike minu mun na inanza minun b, na mba incin ba
Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
9 Na indi nin su iyene nafo indin ziu minu nin miyert nin ba.
Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
10 Bara amung din belun ''iyert me din ziu nin likr, bara na iyarnu adi nin nagan ba uliru na me lien ulazu ba “
Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
11 Na anite yinin nilemong na tibenle brq nin bung na ti diku b, imong irum mere ti ba suu kubi ko na tidi kikane.
Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
12 Natina duo pii ba ipiru natibite, konin batizu nati bit nin nale na idin foo figi mine. Bara kbi kona idin gwadizu atimine nin namonn, nin nani ima se uyenju seng ba.
Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
13 Na ariki wasa ti foo figiri ti kata likara ni lemong na ti wasa tui suu b, bara na tina cinu kusari ko na Kutelle b, bara na tiduro nani har ti da duru anunku.
Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
14 Bara na tina kata ti kala ati bite ba na tima dak kiti min, arikere wa di anan bunu nse minu nlirun Kristi.
Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
15 Nati din foo figiri tikata likara bite ba barabkatwa na mon, bara na tidin cisu kibinai nafo na uyinu sa uyenu mine din kunju nin min bit ngira katwa we bapunu kidawo gbradan.
Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
16 Ariki wang ba belu uliru Kutelle tikata kika na anung na dur. Nati ma foo figiri mbelen katwa ka na ina su kusarin na mong ba.
kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
17 Bara nanin ule na adin foo figiri na afoo figiri nanya Ucif.
Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
18 Bara na ule na ana uti lidu amere asa so cikilari litime barananin lo na cikilarari na na yinin mu.
Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.

< 2 Ukorintiyawa 10 >