< 1 Timothawus 1 >

1 Bulus, unan kaduran Yisa nanya nduka Kutellẹ unan tucu bite, nin Yisa likara nibinai bite.
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwa lamulo la Mulungu, Mpulumutsi wathu ndiponso Khristu Yesu chiyembekezo chathu.
2 Udu kitin Timothawus usaun kiden nanya nyinnu sa uyenu, ubolu kutellẹ niin lisosin limmang, unuzu Kutellẹ ucif bite nin Yisa cikilari bite.
Kwa Timoteyo mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro. Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye athu zikhale ndi iwe.
3 Nwa fo minu acara kube na nwa cinu udu makiduniya, so in Afiisus bara uwantin among udursuzu niimomom ugang, barra nani nan nbellu iincizunu sa ligan, nulale ba dak nin salin yinnu sa katuwa Kutellẹ.
Monga ndinakupempha pamene ndinkapita ku Makedoniya, khala ku Efeso komweko kuti uletse anthu ena kuphunzitsa ziphunzitso zonyenga,
4 Na iwa dinja atuf kiti na nan nabin ninn nanan mmbellu ncizinu nimon sa ligan, allenge na idin dasu nin mannyardan nworu ibun ulin mbun katuwa Kutellẹ, nanya inyinnu sa uyenu.
kapena kumangoyika mitima pa nthano zopeka ndi kufufuza za mayina a makolo awo. Zinthu zotere zimapititsa mʼtsogolo mikangano mʼmalo mwa ntchito ya Mulungu yomwe ndi ya chikhulupiriro.
5 Ukullun duka unere usu, ullenge na unuzu kibinai kilau, nanya nkpilizu ucine, nin inyinnu sa uyenu un kidegen.
Cholinga cha lamuloli ndi chikondi, chomwe chimachokera mu mtima woyera, chikumbumtima chabwino ndi chikhulupiriro choona.
6 Among in nanya ntanni na lasin inn nanya nile imone inani din liru hem.
Anthu ena anapatuka pa zimenezi ndipo anatsata nkhani zopanda tanthauzo.
7 Idinin su iso anan dursuzu nduka, vat nin woru na iyiru ille imon na iidin belle ba, sa ille imon na iinug in yisinaku.
Iwo amafuna kukhala aphunzitsi amalamulo, koma sadziwa zimene akunena, kapena zimene akufuna kutsimikiza.
8 Tiyiru uduka chaun, unit nwa suu kata nin nin.
Tikudziwa kuti Malamulo ndi abwino ngati munthu awagwiritsa ntchito bwino.
9 Ti yiru nani uduka na ina ti unin bara unan kibinai kilau ba, bara anan nsalin dartu nduke nin nanit agbas, bara anan salin dortu kutellẹ nin nan kulapi, bara anan indinong nin na nan nyassu Kutellẹ, bara anan mollusu nacif nan na nnah, bara anan mollusu nanit,
Tikudziwanso kuti Malamulo sakhazikitsidwa chifukwa cha anthu olungama, koma ophwanya lamulo ndi owukira, osaopa Mulungu ndi ochimwa, wopanda chiyero ndi osapembedza; amene amapha abambo awo ndi amayi awo, kapena anthu ena.
10 bara anan suzu nzina, nin nanlime anan nnozu nan nanlime, anan tuzuzu nanit udu licin, anann kinu, bara anan nisilin kinu, nin vat nimon inanzang,
Malamulo amayikidwa chifukwa cha anthu achigololo ndi ochita zadama ndi amuna anzawo, anthu ogulitsa akapolo, abodza ndi olumbira zabodza, ndi ochita chilichonse chotsutsana ndi chiphunzitso choona.
11 bara uliru ugongon Kutellẹ un mari, ullenge na ina ti ku nanya nyinnu.
Chiphunzitso chimene chimagwirizana ndi Uthenga Wabwino wonena za ulemerero wa Mulungu wodala, umene Iye mwini anandisungitsa.
12 Inmini din godu Yisa Kristi cikilari bite, ullenge na atayi agang, bara na ana yene unan nyinnu ninghe amini na ceyi nanya katuwa me.
Ndikuthokoza Khristu Yesu Ambuye athu, amene anandipatsa mphamvu pa ntchitoyi. Iye ananditenga kukhala wokhulupirira, nandipatsa ntchito mu utumiki wake.
13 Meng, na nwandi unan tizogo Kutellẹ, unan tizu nanit ineau, nin nan nnanzu. In mini na se nkunekune Kutellẹ bara na nwadi nsue nanya ntanni, nin salin nyinnu sa uyenu.
Ngakhale kuti kale ndinali wachipongwe, wozunza ndi wankhanza, anandichitira chifundo chifukwa ndinkachita mwaumbuli ndi mopanda chikhulupiriro.
14 Bara ngbardang nbolu Ncikilari bit nin nyinnu sa uyenu a usü in Yisa Kristi.
Chisomo cha Ambuye athu chinatsanulidwa pa ine mochuluka, pamodzi ndi chikhulupiriro ndi chikondi zimene zili mwa Khristu Yesu.
15 Ule ulirue ucinari ubatin iseru unin vat, bara Yisa na dak nanya nyulele ada tucu anan kulapi. Nanya mine miyari udiawe.
Mawu odalirika ndi woyenera kuwavomereza kwathunthu ndi awa: Yesu Khristu anabwera pa dziko lapansi kudzapulumutsa ochimwa, ndipo mwa iwowo ine ndiye wochimwitsitsa.
16 Vat nin nani, nwan buru nse nkunekune, bara nnanzang midiya nigh Kristi Yisa duro ngbardang nayi ashau me, vat, bara nso umuro kiti nalenge na iba yinnu nin ghe udu ulai sa ligang. (aiōnios g166)
Ndipo pa chifukwa chimenechi, Mulungu anandichitira chifundo, kuti mwa ine, wochimwitsitsa, Khristu Yesu aonetse kuleza mtima kwake konse kuti ndikhale chitsanzo cha omwe angathe kumukhulupirira ndi kulandira moyo wosatha. (aiōnios g166)
17 Nene udu kiti ngo nayiri vat, unan salin nkul, ulenge na idin yenju ghe ba, amere Kutellẹ cas, uzazinu ni ngongon udu kitime sa ligan. uso nani. (aiōn g165)
Tsopano kwa Mfumu yamuyaya, yosafa, yosaoneka, amene Iye yekha ndiye Mulungu, kukhale ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)
18 Timothy, usaun nin, nnafi ka kadure, bara imon ile na Kutellẹ wa bellin uworsu litife, bara ille imone yisina unan su Likum Licine!
Mwana wanga Timoteyo, ndikukupatsa langizo ili molingana ndi maulosi amene aneneri ananena za iwe. Pamene ukumbukira mawu amenewa udzatha kumenya bwino nkhondo
19 Bara uyita nin nyinnu sa uyenu nin kibinai kicine. Ule imon na amon na nari inin uyinnu mine sa uyenu una nana.
utagwiritsitsa chikhulupiriro ndi chikumbumtima chabwino. Ena anazikana zimenezi motero chikhulupiriro chawo chinawonongeka.
20 An Haminiyus nin Alekzanda, allenghe na nwa nakpa shintan ku bara inan duro nani nnanzan tizogo Kuutellẹ
Ena mwa amenewa ndi Humenayo ndi Alekisandro, amene ndinawapereka kwa Satana kuti aphunzire kusachita chipongwe Mulungu.

< 1 Timothawus 1 >