< 1 Utasalonika 1 >

1 Bulus, Silvanus nin Timothy, uchin du kuti kulau nTassulinika nanya Kutelle Uchif nin Chikilari Yesu Kristi. Nshew nin mang udu kitimine.
Paulo, Silivano ndi Timoteyo. Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu.
2 Tidin nizu Kutelle ugodo bara anun ka kishi, nyan lira bit asa ti belle ubellen mine.
Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu.
3 Tidin lizunu sa ligagng katah kidegen mine uniu nsuu nin ti reu kibinei bara ubun nya Chikilari Yesu Kristi unbun Kutelle nin Chif bit.
Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 Linwana na Kutelle dinin suuwe, tiyiru nin yichilu mine.
Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani,
5 na abing amang wa da minu na tigbulang chas ba nya na kara, Ufunu ulau nin yinnu udiya vat nin yiru arik imusu na yapi anitarinya mine bara anun.
chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni.
6 Ina so bara arik nin Chikilari nafo na iwa seru ligulan nin nya neu nya liburi libo nfunu ulau.
Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera.
7 bara Yesu imon guru vat nyan Makaduniya nin Akaia udu alenge na idi nin kidegen.
Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya.
8 Na kitimere ligulang Chikilari na nuzu ku chas ba, na Makaduniya nin Akaia ma ba - udo kiti vat na kidegen mine nya Kutelle na do-o, bara nani tiba bellu imon ba.
Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu,
9 Bara inun na mun bellu imusin nati wa se kitimine, a nafo na anun atelle a bebene udu Kutelle lai nin kun kiden.
pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona.
10 A u chaah Ngono me na ana nuzu kitene kane ulenge na awa fya gne nya na nan kul, Yesu, ulengena adin tuchu nari tinana nayin chinu.
Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.

< 1 Utasalonika 1 >