< 1 Utasalonika 5 >

1 Nbelen na biri nin na kus, na ubelen woru i nyertin minu imomon diba.
Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
2 Anun atimine yiru chaut lirin Chikilari nofo ukiri nin kitik.
chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
3 Asa iworo, “Mmang nin taup,” umolsu ba dak nani. Nnafo uwan nmaru na asa alanza ukonu. Na nnere na iba nyeshu nu ba.
Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
4 Anun linuana, na idi nyan nsirt ba bari lo lire wa tuu minu nofo ukiri.
Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
5 Bara anun vat nonon nkanangari nin nnonon lirin. Na arik nono kiti kari ba sa nonon sirt.
Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
6 Bara nani, na tiwa sun mmoro nofo nigisine ba na ti yenje kiti tikpilza kidung.
Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
7 Alenge na idin moro idin su nin kitikari, alenge tutung na idin soh idin su nin kitikari.
Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
8 Bara na arik nono liri gnari, na ti kpilza kidung. Na ti shon kuyangi kidegen nin suu, a, kitik, kidegen tuchu uchin dak.
Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
9 Na Kutelle na che na bara tinana nayi mere ba, bara usen tuchu nyan Cikilari Yesu Kristi.
Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
10 Ulenge na aku bara arik, Sa tidin yenju kiti sa ti din moro, ti so ligowe nin ghe.
Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
11 Bara nanitan linuana nofo na ina man su.
Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
12 Ti din belu minu, linuana, yinnan nin na lenge na ina su kataah nyan mine nin nalenge na itaa minu akara.
Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
13 Tikuru tibelin minu minon nani kang nyan suu bara kataah mine. Son mang nya mine.
Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
14 Ti din ti minu akara, linuana: ale na isosin sa ukpadu wunon nani atuf, ale na nibinei mine kete ita nani akara nibinei, wutun kimal na le na idi gugur, nonkon nibinei.
Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
15 Yenje umon wa kurtung imon inan zan nin ni nanzang udu kitin mong. Tenzinen nimon ichine udu linuana nin vat.
Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
16 Suun liburi libo-o kolome liri.
Kondwerani nthawi zonse.
17 Suun nlira sa ligang.
Pempherani kosalekeza.
18 Nya nimon vat nan ugodo. Bara ulelere usu Kutelle nyan Kristi Yesu bara anun.
Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
19 Yenje uwa bicho Ufunu.
Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
20 Yenje uwa nari ni dura.
Musanyoze mawu a uneneri.
21 Dumuna imon vat. Mino ile imon a ichineari.
Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
22 Chino vat nimon inanzan.
Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
23 Na Kutelle mmang litime akusu fi vat, ulai nin kidowo fe so sa ndinon udak Ncikilari Yesu Kristi.
Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
24 Unan kidegen ame ulenge na adin yichu fi, ulenge na aba su.
Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
25 Linuana, sun nlira bara arik.
Abale, mutipempherere.
26 Lison linuana vat nin lulu na kpan nnuu ulau.
Perekani moni wachikondi kwa onse.
27 Ndin for achara nyan Cikilari nworu ikaranta iyert ilele udu linuana vat.
Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
28 Na nshew Cikilari bite Yesu Kristi so nan ghinu anun.
Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

< 1 Utasalonika 5 >