< 1 Ukorintiyawa 11 >

1 Sun lisosin limang nafo men, nafo na men din su lisosin nafo Kristi.
Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.
2 Nene in di liru mine bara na idin lizunu nin mi nan nya nimon vat tutun inin yisin gangang nan nya nadadu alenge na inani munu.
Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani.
3 Nene ndinin su iyinin Kristiari unan nbu nko kame gankilime, a gakilime ubun nwani, a Kutellẹ amere unan bun nKristi.
Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu.
4 Gakilime ka na ata nlira sa ayene ubun a litime kirno na ana litime ngongon ba.
Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo.
5 Nani vat uwani ule na ata nlira sa a yene ubun sa ukirrunu litime na nà litime ngongon ba. Bara usosin imon irumere nin woru apele titime.
Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake.
6 Asa na uwani ma kiru litime ba, na awarin titime cot. Andi imon cingharib uwani werin sa apelu titime, nbara a kiru litime.
Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.
7 Naneri na gankilime wa kiru litime ba, bara na ame kuyeleri nin gongon Kutellẹ. Ame uwani ngogon ngankilimeri.
Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna.
8 Bara na iwa ke gankilime unuzu kitin nwani ba, uwaneri iwa keghe unuzu kitin gankilime.
Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna.
9 Na iwa ke gankilime bara uwani ba, iwana ke uwani bara gankilimeri.
Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna.
10 Unere nta uwani cau ayita nin litappa tigo litime, bara nono kadura Kutellẹ.
Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake.
11 Vat nin nani, kitin Cikilari, uwani sosin lisosin litime ugan nin gankilime ba, a na gankilime wang sosin lisosin litime ugan nin wani ba.
Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi.
12 Nafo na uwani na dak unuzu kitin gankilime, nanare gankilime na dak unuzu kitin nwani. A imon vat unuzu kiti Kutellẹ.
Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.
13 Sun asarawe ikosu ulire nin natimine, udi dert uwani ti nlira udu kiti Kutellẹ. nin litime fwangha?
Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu?
14 Ani na makeke litime ndurso minu nenge, asa gankilime di nin titi jakaka imon ncighari kitime,
Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali,
15 Ani na makeke ndurso minu nwo asa uwani di nin titi ti jakaka na imon ngogon mere ba?
koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu.
16 Asa umon di nin mong uliru ugang nin lele, na arik dinin namong al ada ugang ba, sa nan nya niti nlira Kutellẹ wang.
Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.
17 Nan nya nale adue, na ndin liru mine ba, bara asa izuro ligowe, na idin dazu nin nimon icine ba sai inanzan.
Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino.
18 Nin cizune, nna lanza au asa izuro ligowe kuti nlira, usali munu nati din nan nya mine, na nyina nin lirumine vat ba.
Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona.
19 Uso gwas na ise naissin nan nya mine, bara alenge na iyinna nin liyissin mine inan se useru nan nya mine.
Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu.
20 Bara iwa zuro ligowe na idin li ujibin NCikilare ba.
Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye.
21 Asa idin le, kogha mine dirtinu nli ninme imonli, a amon dutu nin kukpon, a umon na yita nin kushiton ntoro.
Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera.
22 Na idi nin nilari na imali iso nan nye ba? din yassu kilari Kutellẹ ini tizza anan likimon ilanza ncingha? Nyaghari nba bellin minu? Meng nrù munua? Na nma zazun minu kitene lile imone ba!
Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.
23 Bara nna seru kitin Ncikilari ilenge imon na meng wang nani minu, Cikilari Yisa, nin kitike na iwa nari ame, ayauna ufungule.
Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi.
24 Kimal ntin lira, apuco uni aworo, “ilele kidowo nigharidi, ka naki di bara anung, man suzun nani ilizizin ninmi”
Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.”
25 Nanere tutung awa yaun kakukke kimal jibe, aworo, “kakkuk kane kan ciu nliru upese ari nannya nmī ning. Suzun nani kubi kongo na idin sonē nin kakukke inan lizino nin me.''
Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.”
26 Bara vat kubi ko na ileo ufungal ulele nin kakkuk kane, idin girzunu nkul Ncikilarere udu lirin same.
Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.
27 Vat nlege na adin li ufungalle sa adin so kakkuk Ncikilare a ayita likara linanzang ama yitu nin kulapi kiti kidowo nin mī Ncikilare.
Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye.
28 Na unit tu adumun litime, ma anin li ufungal ani sono kakukke.
Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi.
29 Vat ulenge na adin li aso sa uyenun ngongong kidowo Ncikilare adin li aso usharawari litime.
Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe.
30 Unnare nta among mine gbardan di nin sali nakara a tikonu, among mine wang nkuzu.
Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo.
31 Bara asa ti dumuzuna atibite, iba sunari ushara ba.
Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso.
32 Nani asa idin su nari ushara, ti dinse ugwaru kitin Ncikilare, bara iwa da walin nari ligowe nin yih.
Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.
33 Bara nani nuana ning, asa ida zuro ligowe kiti kileowe son ncà nati.
Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane.
34 Asa umon din lanzu kukpon, na ali kilari, bara iwa da zuro ligowe nan da so ushara kubi ko nan nda nma bellun minu imn ilenge na idin nbun.
Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo. Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.

< 1 Ukorintiyawa 11 >