< Apostlagärningarna 2 >

1 Och då Pingesdagen fullkomnad var, voro de alle endrägteliga tillsammans.
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 Och vardt hastigt ett dön af himmelen, såsom ett mägtigt stort väder kommit hade; och uppfyllde allt huset, der de såto.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 Och dem syntes sönderdelada tungor, såsom af eld; och blef sittandes på kvar och en af dem.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 Och de vordo alle uppfyllde af den Helga Anda, och begynte till att tala med annor tungomål, efter som Anden gaf dem att tala.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 Så voro i Jerusalem boende Judar, gudfruktige män af allahanda folk, som under himmelen är.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 Då nu denna rösten skett hade, kom tillsammans mycket folk, och vordo förhäpne; ty de hörde dem tala kvar och en med sitt eget mål;
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 Och vordo alle förskräckte, och förundrade sig, sägande emellan sig: Si, äro icke alle desse, som tala, Galileiske?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 Huru höre vi då hvar och en sitt tungomål, der vi uti födde äre?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parther och Meder, och Elamiter, och de som bo uti Mesopotamien, och i Judeen, och Cappadocien, Ponto och Asien;
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 Phrygien och Pamphylien, Egypten, och i de Libye landsändar vid Cyrenen, och de utländningar af Rom;
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 Judar och Proselyter, Creter och Araber; vi höre dem med våra tungor tala Guds dråpeliga verk.
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 Och förskräckte de sig alle, och förundrade sig, sägande emellan sig: Hvad månn detta vilja vara?
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 Och somlige gjorde gack af dem, och sade: Desse äro fulle med sött vin.
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 Då stod Petrus upp, med de ellofva, och hof upp sin röst, och talade till dem: I Judiske män, och I alle som bon i Jerusalem; detta skall eder vetterligit vara, och anammer min ord uti edor öron;
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 Ty desse äro icke druckne, såsom I menen; efter det är tredje timmen på dagen;
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 Utan det är det som sagdt är genom Propheten Joel:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 Och det skall ske uti de yttersta dagarna, säger Gud: Jag skall utgjuta af minom Anda öfver allt kött; och edre söner och edra döttrar skola prophetera; och edre ynglingar skola se syner, och edre äldste skola drömma drömmar.
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 Och öfver mina tjenare, och öfver mina tjenarinnor skall jag i de dagar utgjuta af minom Anda; och de skola prophetera.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 Och jag skall gifva under ofvan i himmelen, och tecken neder på jordene; blod och eld, och rökdamb.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 Solen skall vändas i mörker, och månen i blod, förr än den store och uppenbarlige Herrans dag kommer.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 Och skall ske, att hvar och en som åkallar Herrans Namn, han skall blifva salig.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 I män af Israel, hörer dessa orden: Jesum af Nazareth, den man, som när eder af Gudi bevisad är, med krafter, och under, och tecken, som Gud hafver gjort genom honom ibland eder; såsom I ock sjelfve veten.
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 Honom, efter han af Guds betänkta råd och försyn utgifven var, hafven I tagit genom onda mäns händer, korsfäst och dödat.
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 Den hafver Gud uppväckt, och lossat dödsens sveda; efter omöjeligit var, att han skulle behållas af honom.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 Ty David säger om honom: Jag hafver alltid föresatt Herran för min ögon; ty han är mig på högra handene, att jag icke skall rörd varda.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Fördenskull är mitt hjerta gladt, och min tunga fröjdar sig; skall också mitt kött hvilas i förhoppning.
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 Ty du öfvergifver icke mina själ i helvete, och tillstäder icke att din Helige skall se förgängelse. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 Du hafver mig kungjort lifsens vägar; du skall uppfylla mig med fröjd för ditt ansigte.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 I män och bröder, man må fritt tala med eder om den Patriarchen David; han är död och begrafven, och hans graf är när oss intill denna dag.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 Efter han nu var en Prophet, och visste att Gud hade lofvat honom med en ed, att han af hans länds frukt skulle efter köttet uppväcka Christum, till att sitta på hans säte;
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 Såg han det framföreåt, och talade om Christi uppståndelse, att hans själ icke är öfvergifven uti helvete; icke heller hans kött hafver sett förgängelse. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 Denna Jesum hafver Gud uppväckt, der vi alle vittne till äro.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Medan han nu med Guds högra hand upphöjd är, och löfte fått hafver af Fadrenom om den Helga Anda, hafver han utgjutit detta I nu sen och hören.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 Ty icke hafver David uppfarit i himmelen; men han säger: Herren sade till min Herra: Sätt dig på mina högra hand;
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 Tilldess jag nedlägger dina ovänner dig till en fotapall.
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 Så skall nu hela Israels hus veta förvisso, att denna Jesum, som I korsfäst hafven, hafver Gud gjort till en Herra och Christ.
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 Då de detta hörde, fingo de ett styng i hjertat; och sade till Petrum, och till de andra Apostlarna: I män och bröder, hvad skole vi göra?
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 Sade Petrus till dem: Görer bättring, och hvar och en af eder låte sig döpa i Jesu Christi Namn, till syndernas förlåtelse; och I skolen undfå den Helga Andas gåfvo.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 Ty eder är löftet gjordt, och edrom barnom, och allom dem som fjerran äro, hvilka Herren, vår Gud, härtill kallandes varder.
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 Betygade han ock med mång annor ord, och förmanade dem, sägandes: Låter hjelpa eder ifrå detta onda slägtet.
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 De som då gerna anammade hans tal, de läto sig döpa; och kommo till hopen, på den dagen, vid tretusend själar.
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 Och blefvo de stadigt ståndande uti Apostlarnas lärdom, och i delaktighet, och i bröds brytelse, och i böner.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 Och en fruktan kom uppå hvarjo och ena själ; och mång under och tecken gjordes af Apostlarna.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 Och alle de, som trodde, voro tillsammans, och hade all ting menlig.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 Sina ägodelar och håfvor sålde de, och delade dem med alla, såsom hvar och en behöfde.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 Och hvar dag voro de stadigt och endrägteliga i templet; och bröto bröd här och der i husen, ätandes med hvarannan i fröjd; och lofvade Gud i deras hjertans enfaldighet.
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 Och de hade ynnest när allt folket. Och Herren förökade hvar dag församlingen med dem som salige vordo.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Apostlagärningarna 2 >