< Job 8 >

1 Entonces tomó la palabra Baldad suhita y dijo:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “¿Hasta cuándo hablarás de este modo y serán las palabras de tu boca cual viento tempestuoso?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 ¿Acaso Dios tuerce el derecho, o pervierte el Omnipotente la justicia?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Si tus hijos contra Él pecaron, Él los ha castigado ya a causa de sus transgresiones.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Pero tú, si buscas solícito a Dios, e imploras al Todopoderoso,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 y eres puro y recto, al punto Él velará sobre ti, y prosperará la morada de tu justicia.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Tu anterior estado será poca cosa, pues tu porvenir será muy grande.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Pregunta, si quieres, a las generaciones pasadas, respeta la experiencia de los padres;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 pues de ayer somos y nada sabemos, y nuestros días sobre la tierra pasan como la sombra.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Ellos te instruirán, ellos hablarán contigo, y de su corazón sacarán estas palabras:
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 ¿Puede crecer el papiro sin humedad, el junco elevarse sin agua?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Estando aún en flor, y sin ser cortado se seca antes que cualquier otra hierba.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Así será el fin de todos los que se olvidan de Dios; se desvanecerá la esperanza del impío;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 su seguridad le será cortada, y su confianza va a ser como telaraña.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Se apoya sobre su casa, mas esta no se mantiene, se aferra a ella y no resiste.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Está en su lozanía ante el sol, sus renuevos exceden de su huerto,
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 sus raíces se entrelazan sobre el montón de piedras, hundiéndose hasta donde está la roca;
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 mas cuando se lo arranca de su lugar, este lo desconoce (diciendo): «Nunca te he visto.»
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 No es otro el gozo que está al fin de su camino, y de su polvo nacerán otros.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 He aquí que Dios no desecha al justo, ni da la mano a los malvados.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Algún día rebosará de risa tu boca, y tus labios de júbilo.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Los que te aborrecen se cubrirán de ignominia, y la tienda de los impíos dejará de existir.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >