< یوہَنَح 18 >

تاح کَتھاح کَتھَیِتْوا یِیشُح شِشْیانادایَ کِدْرونّامَکَں سْروتَ اُتِّیرْیَّ شِشْیَیح سَہَ تَتْرَتْیودْیانَں پْراوِشَتْ۔ 1
Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.
کِنْتُ وِشْواسَگھاتِیِہُوداسْتَتْ سْتھانَں پَرِچِییَتے یَتو یِیشُح شِشْیَیح سارْدّھَں کَداچِتْ تَتْ سْتھانَمْ اَگَچّھَتْ۔ 2
Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko.
تَدا سَ یِہُوداح سَینْیَگَنَں پْرَدھانَیاجَکاناں پھِرُوشِنانْچَ پَداتِگَنَنْچَ گرِہِیتْوا پْرَدِیپانْ اُلْکانْ اَسْتْرانِ چادایَ تَسْمِنْ سْتھانَ اُپَسْتھِتَوانْ۔ 3
Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.
سْوَں پْرَتِ یَدْ گھَٹِشْیَتے تَجْ جْناتْوا یِیشُرَگْریسَرَح سَنْ تانَپرِچّھَتْ کَں گَویشَیَتھَ؟ 4
Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”
تے پْرَتْیَوَدَنْ، ناسَرَتِییَں یِیشُں؛ تَتو یِیشُرَوادِیدْ اَہَمیوَ سَح؛ تَیح سَہَ وِشْواسَگھاتِی یِہُوداشْچاتِشْٹھَتْ۔ 5
Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.” Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo).
تَداہَمیوَ سَ تَسْیَیتاں کَتھاں شْرُتْوَیوَ تے پَشْچادیتْیَ بھُومَو پَتِتاح۔ 6
Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.
تَتو یِیشُح پُنَرَپِ پرِشْٹھَوانْ کَں گَویشَیَتھَ؟ تَتَسْتے پْرَتْیَوَدَنْ ناسَرَتِییَں یِیشُں۔ 7
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?” Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”
تَدا یِیشُح پْرَتْیُدِتَوانْ اَہَمیوَ سَ اِماں کَتھامَچَکَتھَمْ؛ یَدِ مامَنْوِچّھَتھَ تَرْہِیمانْ گَنْتُں ما وارَیَتَ۔ 8
Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.”
اِتّھَں بھُوتے مَہْیَں یالّوکانْ اَدَداسْتیشامْ ایکَمَپِ ناہارَیَمْ اِماں یاں کَتھاں سَ سْوَیَمَکَتھَیَتْ سا کَتھا سَپھَلا جاتا۔ 9
Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”
تَدا شِمونْپِتَرَسْیَ نِکَٹے کھَنْگَلْسْتھِتیح سَ تَں نِشْکوشَں کرِتْوا مَہایاجَکَسْیَ مالْکھَنامانَں داسَمْ آہَتْیَ تَسْیَ دَکْشِنَکَرْنَں چھِنَّوانْ۔ 10
Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).
تَتو یِیشُح پِتَرَمْ اَوَدَتْ، کھَنْگَں کوشے سْتھاپَیَ مَمَ پِتا مَہْیَں پاتُں یَں کَںسَمْ اَدَداتْ تیناہَں کِں نَ پاسْیامِ؟ 11
Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”
تَدا سَینْیَگَنَح سیناپَتِ رْیِہُودِییاناں پَداتَیَشْچَ یِیشُں گھرِتْوا بَدّھوا ہانَنّامْنَح کِیَپھاح شْوَشُرَسْیَ سَمِیپَں پْرَتھَمَمْ اَنَیَنْ۔ 12
Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga.
سَ کِیَپھاسْتَسْمِنْ وَتْسَرے مَہایاجَتْوَپَدے نِیُکْتَح 13
Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho.
سَنْ سادھارَنَلوکاناں مَنْگَلارْتھَمْ ایکَجَنَسْیَ مَرَنَمُچِتَمْ اِتِ یِہُودِییَیح سارْدّھَمْ اَمَنْتْرَیَتْ۔ 14
Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.
تَدا شِمونْپِتَرونْیَیکَشِشْیَشْچَ یِیشوح پَشْچادْ اَگَچّھَتاں تَسْیانْیَشِشْیَسْیَ مَہایاجَکینَ پَرِچِتَتْواتْ سَ یِیشُنا سَہَ مَہایاجَکَسْیاٹّالِکاں پْراوِشَتْ۔ 15
Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe
کِنْتُ پِتَرو بَہِرْدْوارَسْیَ سَمِیپےتِشْٹھَدْ اَتَایوَ مَہایاجَکینَ پَرِچِتَح سَ شِشْیَح پُنَرْبَہِرْگَتْوا دَووایِکایَے کَتھَیِتْوا پِتَرَمْ اَبھْیَنْتَرَمْ آنَیَتْ۔ 16
koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.
تَدا سَ دْوارَرَکْشِکا پِتَرَمْ اَوَدَتْ تْوَں کِں نَ تَسْیَ مانَوَسْیَ شِشْیَح؟ تَتَح سووَدَدْ اَہَں نَ بھَوامِ۔ 17
Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
تَتَح پَرَں یَتْسْتھانے داساح پَداتَیَشْچَ شِیتَہیتورَنْگارَے رْوَہْنِں پْرَجْوالْیَ تاپَں سیوِتَوَنْتَسْتَتْسْتھانے پِتَرَسْتِشْٹھَنْ تَیح سَہَ وَہْنِتاپَں سیوِتُمْ آرَبھَتَ۔ 18
Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.
تَدا شِشْییشُوپَدیشے چَ مَہایاجَکینَ یِیشُح پرِشْٹَح 19
Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.
سَنْ پْرَتْیُکْتَوانْ سَرْوَّلوکاناں سَمَکْشَں کَتھامَکَتھَیَں گُپْتَں کامَپِ کَتھاں نَ کَتھَیِتْوا یَتْ سْتھانَں یِہُودِییاح سَتَتَں گَچّھَنْتِ تَتْرَ بھَجَنَگیہے مَنْدِرے چاشِکْشَیَں۔ 20
Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri.
مَتَّح کُتَح پرِچّھَسِ؟ یے جَنا مَدُپَدیشَمْ اَشرِنْوَنْ تانیوَ پرِچّھَ یَدْیَدْ اَوَدَں تے تَتْ جانِنْتَ۔ 21
Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”
تَدیتّھَں پْرَتْیُدِتَتْواتْ نِکَٹَسْتھَپَداتِ رْیِیشُں چَپیٹیناہَتْیَ وْیاہَرَتْ مَہایاجَکَمْ ایوَں پْرَتِوَدَسِ؟ 22
Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”
تَتو یِیشُح پْرَتِگَدِتَوانْ یَدْیَیَتھارْتھَمْ اَچَکَتھَں تَرْہِ تَسْیایَتھارْتھَسْیَ پْرَمانَں دیہِ، کِنْتُ یَدِ یَتھارْتھَں تَرْہِ کُتو ہیتو رْمامْ اَتاڈَیَح؟ 23
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?”
پُورْوَّں ہانَنْ سَبَنْدھَنَں تَں کِیَپھامَہایاجَکَسْیَ سَمِیپَں پْرَیشَیَتْ۔ 24
Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.
شِمونْپِتَرَسْتِشْٹھَنْ وَہْنِتاپَں سیوَتے، ایتَسْمِنْ سَمَیے کِیَنْتَسْتَمْ اَپرِچّھَنْ تْوَں کِمْ ایتَسْیَ جَنَسْیَ شِشْیو نَ؟ تَتَح سوپَہْنُتْیابْرَوِیدْ اَہَں نَ بھَوامِ۔ 25
Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?” Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”
تَدا مَہایاجَکَسْیَ یَسْیَ داسَسْیَ پِتَرَح کَرْنَمَچّھِنَتْ تَسْیَ کُٹُمْبَح پْرَتْیُدِتَوانْ اُدْیانے تینَ سَہَ تِشْٹھَنْتَں تْواں کِں ناپَشْیَں؟ 26
Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?”
کِنْتُ پِتَرَح پُنَرَپَہْنُتْیَ کَتھِتَوانْ؛ تَدانِیں کُکُّٹورَوتْ۔ 27
Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.
تَدَنَنْتَرَں پْرَتْیُوشے تے کِیَپھاگرِہادْ اَدھِپَتے رْگرِہَں یِیشُمْ اَنَیَنْ کِنْتُ یَسْمِنْ اَشُچِتْوے جاتے تَے رْنِسْتاروتْسَوے نَ بھوکْتَوْیَں، تَسْیَ بھَیادْ یِہُودِییاسْتَدْگرِہَں ناوِشَنْ۔ 28
Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska.
اَپَرَں پِیلاتو بَہِراگَتْیَ تانْ پرِشْٹھَوانْ ایتَسْیَ مَنُشْیَسْیَ کَں دوشَں وَدَتھَ؟ 29
Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”
تَدا تے پیتْیَوَدَنْ دُشْکَرْمَّکارِنِ نَ سَتِ بھَوَتَح سَمِیپے نَینَں سَمارْپَیِشْیامَح۔ 30
Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”
تَتَح پِیلاتووَدَدْ یُویَمینَں گرِہِیتْوا سْویشاں وْیَوَسْتھَیا وِچارَیَتَ۔ تَدا یِہُودِییاح پْرَتْیَوَدَنْ کَسْیاپِ مَنُشْیَسْیَ پْرانَدَنْڈَں کَرْتُّں ناسْماکَمْ اَدھِکاروسْتِ۔ 31
Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.” Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.”
ایوَں سَتِ یِیشُح سْوَسْیَ مرِتْیَو یاں کَتھاں کَتھِتَوانْ سا سَپھَلابھَوَتْ۔ 32
Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.
تَدَنَنْتَرَں پِیلاتَح پُنَرَپِ تَدْ راجَگرِہَں گَتْوا یِیشُماہُویَ پرِشْٹَوانْ تْوَں کِں یِہُودِییاناں راجا؟ 33
Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”
یِیشُح پْرَتْیَوَدَتْ تْوَمْ ایتاں کَتھاں سْوَتَح کَتھَیَسِ کِمَنْیَح کَشْچِنْ مَیِ کَتھِتَوانْ؟ 34
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”
پِیلاتووَدَدْ اَہَں کِں یِہُودِییَح؟ تَوَ سْوَدیشِییا وِشیشَتَح پْرَدھانَیاجَکا مَمَ نِکَٹے تْواں سَمارْپَیَنَ، تْوَں کِں کرِتَوانْ؟ 35
Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”
یِیشُح پْرَتْیَوَدَتْ مَمَ راجْیَمْ ایتَجَّگَتْسَمْبَنْدھِییَں نَ بھَوَتِ یَدِ مَمَ راجْیَں جَگَتْسَمْبَنْدھِییَمْ اَبھَوِشْیَتْ تَرْہِ یِہُودِییاناں ہَسْتیشُ یَتھا سَمَرْپِتو نابھَوَں تَدَرْتھَں مَمَ سیوَکا اَیوتْسْیَنْ کِنْتُ مَمَ راجْیَمْ اَیہِکَں نَ۔ 36
Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”
تَدا پِیلاتَح کَتھِتَوانْ، تَرْہِ تْوَں راجا بھَوَسِ؟ یِیشُح پْرَتْیُکْتَوانْ تْوَں سَتْیَں کَتھَیَسِ، راجاہَں بھَوامِ؛ سَتْیَتایاں ساکْشْیَں داتُں جَنِں گرِہِیتْوا جَگَتْیَسْمِنْ اَوَتِیرْنَوانْ، تَسْماتْ سَتْیَدھَرْمَّپَکْشَپاتِنو مَمَ کَتھاں شرِنْوَنْتِ۔ 37
Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!” Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”
تَدا سَتْیَں کِں؟ ایتاں کَتھاں پَشْٹْوا پِیلاتَح پُنَرَپِ بَہِرْگَتْوا یِہُودِییانْ اَبھاشَتَ، اَہَں تَسْیَ کَمَپْیَپَرادھَں نَ پْراپْنومِ۔ 38
Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye.
نِسْتاروتْسَوَسَمَیے یُشْمابھِرَبھِرُچِتَ ایکو جَنو مَیا موچَیِتَوْیَ ایشا یُشْماکَں رِیتِرَسْتِ، اَتَایوَ یُشْماکَں نِکَٹے یِہُودِییاناں راجانَں کِں موچَیامِ، یُشْماکَمْ اِچّھا کا؟ 39
Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’”
تَدا تے سَرْوّے رُوَنْتو وْیاہَرَنْ اینَں مانُشَں نَہِ بَرَبّاں موچَیَ۔ کِنْتُ سَ بَرَبّا دَسْیُراسِیتْ۔ 40
Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.

< یوہَنَح 18 >