< ១ ករិន្ថិនះ 3 >

1 ហេ ភ្រាតរះ, អហមាត្មិកៃរិវ យុឞ្មាភិះ សមំ សម្ភាឞិតុំ នាឝក្នវំ កិន្តុ ឝារីរិកាចារិភិះ ខ្រីឞ្ដធម៌្មេ ឝិឝុតុល្យៃឝ្ច ជនៃរិវ យុឞ្មាភិះ សហ សមភាឞេ។
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 យុឞ្មាន៑ កឋិនភក្ឞ្យំ ន ភោជយន៑ ទុគ្ធម៑ អបាយយំ យតោ យូយំ ភក្ឞ្យំ គ្រហីតុំ តទា នាឝក្នុត ឥទានីមបិ ន ឝក្នុថ, យតោ ហេតោរធុនាបិ ឝារីរិកាចារិណ អាធ្វេ។
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 យុឞ្មន្មធ្យេ មាត្សយ៌្យវិវាទភេទា ភវន្តិ តតះ កិំ ឝារីរិកាចារិណោ នាធ្វេ មានុឞិកមាគ៌េណ ច ន ចរថ?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 បៅលស្យាហមិត្យាបល្លោរហមិតិ វា យទ្វាក្យំ យុឞ្មាកំ កៃឝ្ចិត៑ កៃឝ្ចិត៑ កថ្យតេ តស្មាទ៑ យូយំ ឝារីរិកាចារិណ ន ភវថ?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 បៅលះ កះ? អាបល្លោ រ្វា កះ? តៅ បរិចារកមាត្រៅ តយោរេកៃកស្មៃ ច ប្រភុ រ្យាទ្ឫក៑ ផលមទទាត៑ តទ្វត៑ តយោទ៌្វារា យូយំ វិឝ្វាសិនោ ជាតាះ។
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 អហំ រោបិតវាន៑ អាបល្លោឝ្ច និឞិក្តវាន៑ ឦឝ្វរឝ្ចាវទ៌្ធយត៑។
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 អតោ រោបយិត្ឫសេក្តារាវសារៅ វទ៌្ធយិតេឝ្វរ ឯវ សារះ។
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 រោបយិត្ឫសេក្តារៅ ច សមៅ តយោរេកៃកឝ្ច ស្វឝ្រមយោគ្យំ ស្វវេតនំ លប្ស្យតេ។
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 អាវាមីឝ្វរេណ សហ កម៌្មការិណៅ, ឦឝ្វរស្យ យត៑ ក្ឞេត្រម៑ ឦឝ្វរស្យ យា និម៌្មិតិះ សា យូយមេវ។
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 ឦឝ្វរស្យ ប្រសាទាត៑ មយា យត៑ បទំ លព្ធំ តស្មាត៑ ជ្ញានិនា គ្ឫហការិណេវ មយា ភិត្តិមូលំ ស្ថាបិតំ តទុបរិ ចាន្យេន និចីយតេ។ កិន្តុ យេន យន្និចីយតេ តត៑ តេន វិវិច្យតាំ។
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 យតោ យីឝុខ្រីឞ្ដរូបំ យទ៑ ភិត្តិមូលំ ស្ថាបិតំ តទន្យត៑ កិមបិ ភិត្តិមូលំ ស្ថាបយិតុំ កេនាបិ ន ឝក្យតេ។
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 ឯតទ្ភិត្តិមូលស្យោបរិ យទិ កេចិត៑ ស្វណ៌រូប្យមណិកាឞ្ឋត្ឫណនលាន៑ និចិន្វន្តិ,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 តហ៌្យេកៃកស្យ កម៌្ម ប្រកាឝិឞ្យតេ យតះ ស ទិវសស្តត៑ ប្រកាឝយិឞ្យតិ។ យតោ ហតោស្តន ទិវសេន វហ្និមយេនោទេតវ្យំ តត ឯកៃកស្យ កម៌្ម កីទ្ឫឝមេតស្យ បរីក្ឞា ពហ្និនា ភវិឞ្យតិ។
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 យស្យ និចយនរូបំ កម៌្ម ស្ថាស្នុ ភវិឞ្យតិ ស វេតនំ លប្ស្យតេ។
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 យស្យ ច កម៌្ម ធក្ឞ្យតេ តស្យ ក្ឞតិ រ្ភវិឞ្យតិ កិន្តុ វហ្នេ រ្និគ៌តជន ឥវ ស ស្វយំ បរិត្រាណំ ប្រាប្ស្យតិ។
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 យូយម៑ ឦឝ្វរស្យ មន្ទិរំ យុឞ្មន្មធ្យេ ចេឝ្វរស្យាត្មា និវសតីតិ កិំ ន ជានីថ?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 ឦឝ្វរស្យ មន្ទិរំ យេន វិនាឝ្យតេ សោៜបីឝ្វរេណ វិនាឝយិឞ្យតេ យត ឦឝ្វរស្យ មន្ទិរំ បវិត្រមេវ យូយំ តុ តន្មន្ទិរម៑ អាធ្វេ។
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 កោបិ ស្វំ ន វញ្ចយតាំ។ យុឞ្មាកំ កឝ្ចន ចេទិហលោកស្យ ជ្ញានេន ជ្ញានវានហមិតិ ពុធ្យតេ តហ៌ិ ស យត៑ ជ្ញានី ភវេត៑ តទត៌្ហំ មូឍោ ភវតុ។ (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 យស្មាទិហលោកស្យ ជ្ញានម៑ ឦឝ្វរស្យ សាក្ឞាត៑ មូឍត្វមេវ។ ឯតស្មិន៑ លិខិតមប្យាស្តេ, តីក្ឞ្ណា យា ជ្ញានិនាំ ពុទ្ធិស្តយា តាន៑ ធរតីឝ្វរះ។
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 បុនឝ្ច។ ជ្ញានិនាំ កល្បនា វេត្តិ បរមេឝោ និរត៌្ហកាះ។
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 អតឯវ កោៜបិ មនុជៃរាត្មានំ ន ឝ្លាឃតាំ យតះ សវ៌្វាណិ យុឞ្មាកមេវ,
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 បៅល វា អាបល្លោ រ្វា កៃផា វា ជគទ៑ វា ជីវនំ វា មរណំ វា វត៌្តមានំ វា ភវិឞ្យទ្វា សវ៌្វាណ្យេវ យុឞ្មាកំ,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 យូយញ្ច ខ្រីឞ្ដស្យ, ខ្រីឞ្ដឝ្ចេឝ្វរស្យ។
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< ១ ករិន្ថិនះ 3 >