< 1 Coríntios 3 >

1 Irmãos, eu não poderia falar com vocês como espiritual, mas como carnal, como com os bebês em Cristo.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 Eu os alimentei com leite, não com alimentos sólidos, pois vocês ainda não estavam prontos. De fato, vocês ainda não estão prontos,
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 pois ainda são carnais. Pois na medida em que há ciúmes, contendas e facções entre vocês, vocês não são carnais, e não andam nos caminhos dos homens?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 Pois quando um diz: “Eu sigo Paulo”, e outro: “Eu sigo Apolo”, você não é carnal?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Quem então é Apolo, e quem é Paulo, mas servos através dos quais você acreditou, e cada um como o Senhor lhe deu?
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 Eu plantei. Apolo regado. Mas Deus deu o aumento.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 Portanto, nem aquele que planta é nada, nem aquele que rega, mas Deus que dá o aumento.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Agora quem planta e quem rega é o mesmo, mas cada um receberá sua própria recompensa de acordo com seu próprio trabalho.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 Pois somos companheiros de trabalho de Deus. Vocês são a agricultura de Deus, o edifício de Deus.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 De acordo com a graça de Deus que me foi dada, como sábio mestre-de-obras, lancei uma base, e outra se baseia nela. Mas que cada homem tenha cuidado em como constrói sobre ela.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 Pois ninguém pode lançar outro alicerce além daquele que foi lançado, que é Jesus Cristo.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Mas se alguém construir sobre o alicerce com ouro, prata, pedras caras, madeira, feno ou palha,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 o trabalho de cada homem será revelado. Pois o Dia o declarará, porque é revelado no fogo; e o próprio fogo testará que tipo de trabalho é o trabalho de cada homem.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 Se o trabalho de qualquer homem permanecer que ele construiu sobre ele, ele receberá uma recompensa.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 Se o trabalho de qualquer homem for queimado, ele sofrerá perdas, mas ele mesmo será salvo, mas como através do fogo.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Você não sabe que você é o templo de Deus e que o Espírito de Deus vive em você?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 Se alguém destruir o templo de Deus, Deus o destruirá; pois o templo de Deus é santo, o que você é.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Que ninguém se engane. Se alguém pensa que ele é sábio entre vocês neste mundo, deixem-no tornar-se um tolo para que ele se torne sábio. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 Pois a sabedoria deste mundo é tolice com Deus. Pois está escrito: “Ele tomou os sábios em sua astúcia”.
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 E novamente, “O Senhor conhece o raciocínio dos sábios, que ele não vale nada”.
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Portanto, que ninguém se vanglorie nos homens. Pois todas as coisas são suas,
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 seja Paulo, ou Apolo, ou Cephas, ou o mundo, ou a vida, ou a morte, ou as coisas presentes, ou as coisas por vir. Todos são seus,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 e você é de Cristo, e Cristo é de Deus.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Coríntios 3 >