< زکریا 9 >

وحی کلام خداوند بر زمین حدراخ (نازل می شود) و دمشق محل آن می‌باشد، زیراکه نظر انسان و نظر تمامی اسباط اسرائیل بسوی خداوند است. ۱ 1
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
و بر حمات نیز که مجاور آن است و بر صور و صیدون اگر‌چه بسیار دانشمندمی باشد. ۲ 2
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
و صور برای خود ملاذی منیع ساخت و نقره را مثل غبار و طلا را مانند گل کوچه هاانباشت. ۳ 3
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
اینک خداوند او را اخراج خواهد کردو قوتش را که در دریا می‌باشد، تلف خواهدساخت و خودش به آتش سوخته خواهد شد. ۴ 4
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
اشقلون چون این را بیند خواهد ترسید و غزه بسیار دردناک خواهد شد و عقرون نیز زیرا که اعتماد او خجل خواهد گردید و پادشاه از غزه هلاک خواهد شد و اشقلون مسکون نخواهدگشت. ۵ 5
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
و حرام زاده‌ای در اشدود جلوس خواهدنمود و حشمت فلسطینیان را منقطع خواهم ساخت. ۶ 6
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
و خون او را از دهانش بیرون خواهم آورد و رجاساتش را از میان دندانهایش؛ و بقیه اونیز به جهت خدای ما خواهد بود و خودش مثل امیری در یهودا و عقرون مانند یبوسی خواهدشد. ۷ 7
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
و من گرداگرد خانه خود به ضد لشکر اردوخواهم زد تا کسی از آن عبور و مرور نکند و ظالم بار دیگر از میان آنها گذر نخواهد کرد زیرا که حال به چشمان خود مشاهده نموده‌ام. ۸ 8
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
‌ای دختر صهیون بسیار وجد بنما و ای دختر اورشلیم آواز شادمانی بده! اینک پادشاه تونزد تو می‌آید. او عادل و صاحب نجات و حلیم می‌باشد و بر الاغ و بر کره بچه الاغ سوار است. ۹ 9
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
و من ارابه را از افرایم و اسب را از اورشلیم منقطع خواهم ساخت و کمان جنگی شکسته خواهد شد و او با امت‌ها به سلامتی تکلم خواهدنمود و سلطنت او از دریا تا دریا و از نهر تا اقصای زمین خواهد بود. ۱۰ 10
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
و اما من اسیران تو را نیز به واسطه خون عهد تو از چاهی که در آن آب نیست رها کردم. ۱۱ 11
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
‌ای اسیران امید، به ملاذ منیع مراجعت نمایید. امروز نیز خبر می‌دهم که به شما(نصیب ) مضاعف رد خواهم نمود. ۱۲ 12
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
زیرا که یهودا را برای خود زه خواهم کرد و افرایم راتیرکمان خواهم ساخت و پسران تو را‌ای صهیون به ضد پسران تو‌ای یاوان خواهم برانگیخت و تورا مثل شمشیر جبار خواهم گردانید. ۱۳ 13
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
و خداوند بالای ایشان ظاهر خواهد شد وتیر او مانند برق خواهد جست و خداوند یهوه کرنا را نواخته، بر گردبادهای جنوبی خواهدتاخت. ۱۴ 14
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
یهوه صبایوت ایشان را حمایت خواهد کرد و ایشان غذا خورده، سنگهای فلاخن را پایمال خواهند کردو نوشیده، مثل از شراب نعره خواهند زد و مثل جامها و مانند گوشه های مذبح پر خواهند شد. ۱۵ 15
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
و یهوه خدای ایشان ایشان را در آن روز مثل گوسفندان قوم خودخواهد رهانید زیرا که مانند جواهر تاج بر زمین اوخواهند درخشید. ۱۶ 16
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
زیرا که حسن و زیبایی اوچه قدر عظیم است. گندم جوانان را و عصیر انگور دوشیزگان را خرم خواهد ساخت. ۱۷ 17
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.

< زکریا 9 >