< مزامیر 91 >

آنکه در ستر حضرت اعلی نشسته است، زیر سایه قادرمطلق ساکن خواهد بود. ۱ 1
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
درباره خداوند می‌گویم که او ملجاو قلعه من است و خدای من که بر او توکل دارم. ۲ 2
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
زیرا که او تو را از دام صیاد خواهد رهانید و ازوبای خبیث. ۳ 3
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
به پرهای خود تو را خواهدپوشانید و زیر بالهایش پناه خواهی گرفت. راستی او تو را مجن و سپر خواهد بود. ۴ 4
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
از خوفی درشب نخواهی ترسید و نه از تیری که در روزمی پرد. ۵ 5
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
و نه از وبایی که در تاریکی می‌خرامد ونه از طاعونی که وقت ظهر فساد می‌کند. ۶ 6
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
هزارنفر به‌جانب تو خواهند افتاد و ده هزار به‌دست راست تو. لیکن نزد تو نخواهد رسید. ۷ 7
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
فقط به چشمان خود خواهی نگریست و پاداش شریران را خواهی دید. ۸ 8
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
زیرا گفتی تو‌ای خداوندملجای من هستی و حضرت اعلی را ماوای خویش گردانیده‌ای. ۹ 9
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
هیچ بدی بر تو واقع نخواهد شد و بلایی نزد خیمه تو نخواهد رسید. ۱۰ 10
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
زیرا که فرشتگان خود را درباره تو امر خواهدفرمود تا در تمامی راههایت تو را حفظ نمایند. ۱۱ 11
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
تو را بر دستهای خود برخواهند داشت، مباداپای خود را به سنگ بزنی. ۱۲ 12
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
بر شیر و افعی پای خواهی نهاد؛ شیربچه و اژدها را پایمال خواهی کرد. ۱۳ 13
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
«چونکه به من رغبت دارد او را خواهم رهانید و چونکه به اسم من عارف است او راسرافراز خواهم ساخت. ۱۴ 14
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
چون مرا خواند او رااجابت خواهم کرد. من در تنگی با او خواهم بود واو را نجات داده، معزز خواهم ساخت. ۱۵ 15
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
به طول ایام او را سیر می‌گردانم و نجات خویش را بدونشان خواهم داد.» ۱۶ 16
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”

< مزامیر 91 >