< مزامیر 91 >
آنکه در ستر حضرت اعلی نشسته است، زیر سایه قادرمطلق ساکن خواهد بود. | ۱ 1 |
Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
درباره خداوند میگویم که او ملجاو قلعه من است و خدای من که بر او توکل دارم. | ۲ 2 |
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa, Mulungu wanga amene ndimadalira.”
زیرا که او تو را از دام صیاد خواهد رهانید و ازوبای خبیث. | ۳ 3 |
Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje ndi ku mliri woopsa;
به پرهای خود تو را خواهدپوشانید و زیر بالهایش پناه خواهی گرفت. راستی او تو را مجن و سپر خواهد بود. | ۴ 4 |
Adzakuphimba ndi nthenga zake, ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo; kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
از خوفی درشب نخواهی ترسید و نه از تیری که در روزمی پرد. | ۵ 5 |
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku, kapena muvi wowuluka masana,
و نه از وبایی که در تاریکی میخرامد ونه از طاعونی که وقت ظهر فساد میکند. | ۶ 6 |
kapena mliri umene umayenda mu mdima, kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
هزارنفر بهجانب تو خواهند افتاد و ده هزار بهدست راست تو. لیکن نزد تو نخواهد رسید. | ۷ 7 |
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako, anthu 10,000 kudzanja lako lamanja, koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
فقط به چشمان خود خواهی نگریست و پاداش شریران را خواهی دید. | ۸ 8 |
Udzapenya ndi maso ako ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.
زیرا گفتی توای خداوندملجای من هستی و حضرت اعلی را ماوای خویش گردانیدهای. | ۹ 9 |
Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo; wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
هیچ بدی بر تو واقع نخواهد شد و بلایی نزد خیمه تو نخواهد رسید. | ۱۰ 10 |
Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera, zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
زیرا که فرشتگان خود را درباره تو امر خواهدفرمود تا در تمامی راههایت تو را حفظ نمایند. | ۱۱ 11 |
Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe, kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
تو را بر دستهای خود برخواهند داشت، مباداپای خود را به سنگ بزنی. | ۱۲ 12 |
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
بر شیر و افعی پای خواهی نهاد؛ شیربچه و اژدها را پایمال خواهی کرد. | ۱۳ 13 |
Udzapondaponda mkango ndi njoka, udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.
«چونکه به من رغبت دارد او را خواهم رهانید و چونکه به اسم من عارف است او راسرافراز خواهم ساخت. | ۱۴ 14 |
“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa; ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
چون مرا خواند او رااجابت خواهم کرد. من در تنگی با او خواهم بود واو را نجات داده، معزز خواهم ساخت. | ۱۵ 15 |
Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha; ndidzakhala naye pa mavuto, ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
به طول ایام او را سیر میگردانم و نجات خویش را بدونشان خواهم داد.» | ۱۶ 16 |
Ndidzamupatsa moyo wautali ndi kumupulumutsa.”