< مزامیر 45 >

برای سالار مغنیان بر سوسنها. قصیده بنی قورح. سرود حبیبات دل من به کلام نیکو می‌جوشد. انشاءخود را درباره پادشاه می‌گویم. زبان من قلم کاتب ماهر است. ۱ 1
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati. Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu; lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.
تو جمیل تر هستی ازبنی آدم و نعمت بر لبهای تو ریخته شده است. بنابراین، خدا تو را مبارک ساخته است تا ابدالاباد. ۲ 2
Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika, popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.
‌ای جبار شمشیر خود را بر ران خود ببند، یعنی جلال و کبریایی خویش را. ۳ 3
Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu; mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.
و به کبریایی خودسوار شده، غالب شو به جهت راستی و حلم وعدالت و دست راستت چیزهای ترسناک را به توخواهد آموخت. ۴ 4
Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo; dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.
به تیرهای تیز تو امت‌ها زیر تومی افتند و به دل دشمنان پادشاه فرو می‌رود. ۵ 5
Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu, mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.
‌ای خدا، تخت تو تا ابدالاباد است؛ عصای راستی عصای سلطنت تو است. ۶ 6
Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi; ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.
عدالت را دوست وشرارت را دشمن داشتی. بنابراین خدا خدای توتو را به روغن شادمانی بیشتر از رفقایت مسح کرده است. ۷ 7
Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa; choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.
همه رختهای تو مر و عود و سلیخه است، از قصرهای عاج که به تارها تو را خوش ساختند. ۸ 8
Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya; kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.
دختران پادشاهان از زنان نجیب توهستند. ملکه به‌دست راستت در طلای اوفیرایستاده است. ۹ 9
Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka; ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.
‌ای دختر بشنو و ببین و گوش خود را فرادار. و قوم خود و خانه پدرت رافراموش کن، ۱۰ 10
Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu; iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.
تا پادشاه مشتاق جمال تو بشود، زیرا او خداوند تو است پس او را عبادت نما. ۱۱ 11
Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako; mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.
ودختر صور با ارمغانی. و دولتمندان قوم رضامندی تو را خواهند طلبید. ۱۲ 12
Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso, amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.
دختر پادشاه تمام در اندرون مجید است و رختهای او با طلا مرصع است. ۱۳ 13
Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake, chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.
به لباس طرازدار نزد پادشاه حاضر می‌شود. باکره های همراهان او در عقب وی نزد تو آورده خواهند شد. ۱۴ 14
Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu; anamwali okhala naye akumutsatira ndipo abweretsedwa kwa inu.
به شادمانی وخوشی آورده می‌شوند و به قصر پادشاه داخل خواهند شد. ۱۵ 15
Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo; akulowa mʼnyumba yaufumu.
به عوض پدرانت پسرانت خواهند بود و ایشان را بر تمامی جهان سروران خواهی ساخت. ۱۶ 16
Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako; udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.
نام تو را در همه دهرها ذکرخواهم کرد. پس قوم‌ها تو را حمد خواهند گفت تا ابدالاباد. ۱۷ 17
Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse; choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

< مزامیر 45 >