< مزامیر 116 >
خداوند را محبت مینمایم زیرا که آواز من و تضرع مرا شنیده است. | ۱ 1 |
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
زیرا که گوش خود را به من فرا داشته است، پس مدت حیات خود، او را خواهم خواند. | ۲ 2 |
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
ریسمان های موت مرا احاطه کرد و تنگیهای هاویه مرا دریافت، تنگی و غم پیدا کردم. (Sheol ) | ۳ 3 |
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
آنگاه نام خداوند را خواندم. آهای خداوند جان مرارهایی ده! | ۴ 4 |
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
خداوند رئوف و عادل است و خدای ما رحیم است. | ۵ 5 |
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
خداوند ساده دلان را محافظت میکند. ذلیل بودم و مرا نجات داد. | ۶ 6 |
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
ای جان من به آرامی خود برگرد، زیراخداوند به تو احسان نموده است. | ۷ 7 |
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
زیرا که جان مرا از موت خلاصی دادی و چشمانم را از اشک و پایهایم را از لغزیدن. | ۸ 8 |
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
به حضور خداوند سالک خواهم بود، در زمین زندگان. | ۹ 9 |
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
ایمان آوردم پس سخن گفتم. من بسیار مستمند شدم. | ۱۰ 10 |
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
درپریشانی خود گفتم که «جمیع آدمیان دروغ گویند.» | ۱۱ 11 |
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
خداوند را چه ادا کنم، برای همه احسانهایی که به من نموده است؟ | ۱۲ 12 |
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
پیاله نجات را خواهم گرفت و نام خداوند را خواهم خواند. | ۱۳ 13 |
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
نذرهای خود را به خداوند ادا خواهم کرد، به حضور تمامی قوم او. | ۱۴ 14 |
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
موت مقدسان خداونددر نظر وی گرانبها است. | ۱۵ 15 |
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
آهای خداوند، من بنده تو هستم! من بنده تو و پسر کنیز تو هستم. بندهای مرا گشودهای! | ۱۶ 16 |
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
قربانی های تشکر نزدتو خواهم گذرانید و نام خداوند را خواهم خواند. | ۱۷ 17 |
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
نذرهای خود را به خداوند ادا خواهم کرد، به حضور تمامی قوم وی، | ۱۸ 18 |
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
در صحن های خانه خداوند، در اندرون توای اورشلیم. هللویاه! | ۱۹ 19 |
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.