< مزامیر 116 >

خداوند را محبت می‌نمایم زیرا که آواز من و تضرع مرا شنیده است. ۱ 1
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
زیرا که گوش خود را به من فرا داشته است، پس مدت حیات خود، او را خواهم خواند. ۲ 2
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
ریسمان های موت مرا احاطه کرد و تنگیهای هاویه مرا دریافت، تنگی و غم پیدا کردم. (Sheol h7585) ۳ 3
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
آنگاه نام خداوند را خواندم. آه‌ای خداوند جان مرارهایی ده! ۴ 4
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
خداوند رئوف و عادل است و خدای ما رحیم است. ۵ 5
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
خداوند ساده دلان را محافظت می‌کند. ذلیل بودم و مرا نجات داد. ۶ 6
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
‌ای جان من به آرامی خود برگرد، زیراخداوند به تو احسان نموده است. ۷ 7
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
زیرا که جان مرا از موت خلاصی دادی و چشمانم را از اشک و پایهایم را از لغزیدن. ۸ 8
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
به حضور خداوند سالک خواهم بود، در زمین زندگان. ۹ 9
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
ایمان آوردم پس سخن گفتم. من بسیار مستمند شدم. ۱۰ 10
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
درپریشانی خود گفتم که «جمیع آدمیان دروغ گویند.» ۱۱ 11
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
خداوند را چه ادا کنم، برای همه احسانهایی که به من نموده است؟ ۱۲ 12
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
پیاله نجات را خواهم گرفت و نام خداوند را خواهم خواند. ۱۳ 13
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
نذرهای خود را به خداوند ادا خواهم کرد، به حضور تمامی قوم او. ۱۴ 14
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
موت مقدسان خداونددر نظر وی گرانبها است. ۱۵ 15
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
آه‌ای خداوند، من بنده تو هستم! من بنده تو و پسر کنیز تو هستم. بندهای مرا گشوده‌ای! ۱۶ 16
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
قربانی های تشکر نزدتو خواهم گذرانید و نام خداوند را خواهم خواند. ۱۷ 17
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
نذرهای خود را به خداوند ادا خواهم کرد، به حضور تمامی قوم وی، ۱۸ 18
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
در صحن های خانه خداوند، در اندرون تو‌ای اورشلیم. هللویاه! ۱۹ 19
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< مزامیر 116 >