< امثال 12 >

هر‌که تادیب را دوست می‌دارد معرفت را دوست می‌دارد، اما هر‌که از تنبیه نفرت کند وحشی است. ۱ 1
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
مرد نیکو رضامندی خداوند را تحصیل می‌نماید، اما او صاحب تدبیر فاسد را ملزم خواهد ساخت. ۲ 2
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
انسان از بدی استوار نمی شود، اما ریشه عادلان جنبش نخواهد خورد. ۳ 3
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
زن صالحه تاج شوهر خود می‌باشد، اما زنی که خجل سازد مثل پوسیدگی در استخوانهایش می‌باشد. ۴ 4
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
فکرهای عادلان انصاف است، اما تدابیرشریران فریب است. ۵ 5
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
سخنان شریران برای خون در کمین است، اما دهان راستان ایشان را رهایی می‌دهد. ۶ 6
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
شریران واژگون شده، نیست می‌شوند، اماخانه عادلان برقرار می‌ماند. ۷ 7
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
انسان برحسب عقلش ممدوح می‌شود، اماکج دلان خجل خواهند گشت. ۸ 8
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
کسی‌که حقیر باشد و خادم داشته باشد، بهتراست از کسی‌که خویشتن را برافرازد و محتاج نان باشد. ۹ 9
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
مرد عادل برای جان حیوان خود تفکرمی کند، اما رحمتهای شریران ستم کیشی است. ۱۰ 10
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
کسی‌که زمین خود را زرع کند از نان سیرخواهد شد، اما هر‌که اباطیل را پیروی نمایدناقص العقل است. ۱۱ 11
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
مرد شریر به شکار بدکاران طمع می‌ورزد، اما ریشه عادلان میوه می‌آورد. ۱۲ 12
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
در تقصیر لبها دام مهلک است، اما مردعادل از تنگی بیرون می‌آید. ۱۳ 13
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
انسان از ثمره دهان خود از نیکویی سیرمی شود، و مکافات دست انسان به او رد خواهدشد. ۱۴ 14
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
راه احمق در نظر خودش راست است، اماهر‌که نصیحت را بشنود حکیم است. ۱۵ 15
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
غضب احمق فور آشکار می‌شود، اماخردمند خجالت را می‌پوشاند. ۱۶ 16
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
هر‌که به راستی تنطق نماید عدالت را ظاهرمی کند، و شاهد دروغ، فریب را. ۱۷ 17
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
هستند که مثل ضرب شمشیر حرفهای باطل می‌زنند، اما زبان حکیمان شفا می‌بخشد. ۱۸ 18
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
لب راستگو تا به ابد استوار می‌ماند، اما زبان دروغگو طرفه العینی است. ۱۹ 19
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
در دل هر‌که تدبیر فاسد کند فریب است، اما مشورت دهندگان صلح را شادمانی است. ۲۰ 20
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
هیچ بدی به مرد صالح واقع نمی شود، اماشریران از بلا پر خواهند شد. ۲۱ 21
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
لبهای دروغگو نزد خداوند مکروه است، اما عاملان راستی پسندیده او هستند. ۲۲ 22
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
مرد زیرک علم را مخفی می‌دارد، اما دل احمقان حماقت را شایع می‌سازد. ۲۳ 23
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
دست شخص زرنگ سلطنت خواهدنمود، اما مرد کاهل بندگی خواهد کرد. ۲۴ 24
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
کدورت دل انسان، او را منحنی می‌سازد، اما سخن نیکو او را شادمان خواهد گردانید. ۲۵ 25
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
مرد عادل برای همسایه خود هادی می‌شود، اما راه شریران ایشان را گمراه می‌کند. ۲۶ 26
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
مرد کاهل شکار خود را بریان نمی کند، امازرنگی، توانگری گرانبهای انسان است. ۲۷ 27
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
در طریق عدالت حیات‌است، و درگذرگاههایش موت نیست. ۲۸ 28
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< امثال 12 >