< داوران 14 >

و شمشون به تمنه فرود آمده، زنی ازدختران فلسطینیان در تمنه دید. ۱ 1
Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti.
وآمده، به پدر و مادر خود بیان کرده، گفت: «زنی ازدختران فلسطینیان در تمنه دیدم، پس الان او رابرای من به زنی بگیرید.» ۲ 2
Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”
پدر و مادرش وی راگفتند: «آیا از دختران برادرانت و در تمامی قوم من دختری نیست که تو باید بروی و از فلسطینیان نامختون زن بگیری؟» شمشون به پدر خود گفت: «او را برای من بگیر زیرا در نظر من پسند آمد.» ۳ 3
Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?” Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.”
اما پدر و مادرش نمی دانستند که این از جانب خداوند است، زیرا که بر فلسطینیان علتی می‌خواست، چونکه در آن وقت فلسطینیان براسرائیل تسلط می‌داشتند. ۴ 4
(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli).
پس شمشون با پدر و مادر خود به تمنه فرودآمد، و چون به تاکستانهای تمنه رسیدند، اینک شیری جوان بر او بغرید. ۵ 5
Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye.
و روح خداوند بر اومستقر شده، آن را درید به طوری که بزغاله‌ای دریده شود، و چیزی در دستش نبود و پدر و مادرخود را از آنچه کرده بود، اطلاع نداد. ۶ 6
Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo.
و رفته، باآن زن سخن گفت وبه نظر شمشون پسند آمد. ۷ 7
Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.
وچون بعد از چندی برای گرفتنش برمی گشت، ازراه به کنار رفت تا لاشه شیر را ببیند و اینک انبوه زنبور، و عسل در لاشه شیر بود. ۸ 8
Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake.
و آن را به دست خود گرفته، روان شد و در رفتن می‌خورد تابه پدر و مادر خود رسیده، به ایشان داد وخوردند. اما به ایشان نگفت که عسل را از لاشه شیر گرفته بود. ۹ 9
Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.
و پدرش نزد آن زن آمد و شمشون در آنجامهمانی کرد، زیرا که جوانان چنین عادت داشتند. ۱۰ 10
Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata.
و واقع شد که چون او را دیدند، سی رفیق انتخاب کردند تا همراه او باشند. ۱۱ 11
Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.
و شمشون به ایشان گفت: «معمایی برای شما می‌گویم، اگر آن را برای من در هفت روز مهمانی حل کنید و آن رادریافت نمایید، به شما سی جامه کتان و سی دست رخت می‌دهم. ۱۲ 12
Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero.
و اگر آن را برای من نتوانید حل کنید آنگاه شما سی جامه کتان و سی دست رخت به من بدهید.» ایشان به وی گفتند: «معمای خود را بگو تا آن را بشنویم.» ۱۳ 13
Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.” Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”
به ایشان گفت: «از خورنده خوراک بیرون آمد، و اززورآور شیرینی بیرون آمد.» و ایشان تا سه روزمعما را نتوانستند حل کنند. ۱۴ 14
Iye anati, “Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake; ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.” Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.
و واقع شد که در روز هفتم به زن شمشون گفتند: «شوهر خود را ترغیب نما تا معمای خودرا برای ما بیان کند مبادا تو را و خانه پدر تو را به آتش بسوزانیم، آیا ما را دعوت کرده‌اید تا ما راتاراج نمایید یا نه.» ۱۵ 15
Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”
پس زن شمشون پیش اوگریسته، گفت: «به درستی که مرا بغض می‌نمایی و دوست نمی داری زیرا معمایی به پسران قوم من گفته‌ای و آن را برای من بیان نکردی.» او وی راگفت: «اینک برای پدر و مادر خود بیان نکردم، آیابرای تو بیان کنم.» ۱۶ 16
Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.” Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?”
و در هفت روزی که ضیافت ایشان می‌بود پیش او می‌گریست، و واقع شد که در روز هفتم چونکه او را بسیار الحاح می‌نمود، برایش بیان کرد و او معما را به پسران قوم خودگفت. ۱۷ 17
Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.
و در روز هفتم مردان شهر پیش از غروب آفتاب به وی گفتند که «چیست شیرین تراز عسل و چیست زورآورتر از شیر.» او به ایشان گفت: «اگر با گاو من خیش نمی کردید، معمای مرادریافت نمی نمودید.» ۱۸ 18
Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti, “Chozuna nʼchiyani choposa uchi? Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?” Samsoni anawawuza kuti, “Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono, simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”
و روح خداوند بر وی مستقر شده، به اشقلون رفت و از اهل آنجا سی نفر را کشت، و اسباب آنها را گرفته، دسته های رخت را به آنانی که معما را بیان کرده بودند، داد وخشمش افروخته شده، به خانه پدر خودبرگشت. ۱۹ 19
Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu.
و زن شمشون به رفیقش که او رادوست خود می‌شمرد، داده شد. ۲۰ 20
Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

< داوران 14 >