< ایّوب 27 >
و ایوب دیگرباره مثل خود را آورده، گفت: | ۱ 1 |
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
«به حیات خدا که حق مرابرداشته و به قادرمطلق که جان مرا تلخ نموده است. | ۲ 2 |
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
که مادامی که جانم در من باقی است ونفخه خدا در بینی من میباشد، | ۳ 3 |
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
یقین لبهایم به بیانصافی تکلم نخواهد کرد، و زبانم به فریب تنطق نخواهد نمود. | ۴ 4 |
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
حاشا از من که شما راتصدیق نمایم، و تا بمیرم کاملیت خویش را ازخود دور نخواهم ساخت. | ۵ 5 |
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
عدالت خود را قایم نگاه میدارم و آن را ترک نخواهم نمود، و دلم تازنده باشم، مرا مذمت نخواهد کرد. | ۶ 6 |
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
دشمن من مثل شریر باشد، و مقاومت کنندگانم مثل خطاکاران. | ۷ 7 |
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
زیرا امید شریر چیست هنگامی که خدا او را منقطع میسازد؟ و حینی که خدا جان اورا میگیرد؟ | ۸ 8 |
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
آیا خدا فریاد او را خواهد شنید، هنگامی که مصیبت بر او عارض شود؟ | ۹ 9 |
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
آیا درقادرمطلق تلذذ خواهد یافت، و در همه اوقات ازخدا مسالت خواهد نمود؟ | ۱۰ 10 |
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
«شما را درباره دست خدا تعلیم خواهد دادو از اعمال قادرمطلق چیزی مخفی نخواهم داشت. | ۱۱ 11 |
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
اینک جمیع شما این را ملاحظه کردهاید، پس چرا بالکل باطل شدهاید. | ۱۲ 12 |
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
این است نصیب مرد شریر از جانب خدا، و میراث ظالمان که آن را از قادرمطلق مییابند. | ۱۳ 13 |
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
اگرفرزندانش بسیار شوند شمشیر برای ایشان است، و ذریت او از نان سیر نخواهند شد. | ۱۴ 14 |
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
بازماندگان او از وبا دفن خواهند شد، و بیوهزنانش گریه نخواهند کرد. | ۱۵ 15 |
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
اگرچه نقره را مثل غبار اندوخته کند، و لباس را مثل گل آماده سازد. | ۱۶ 16 |
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
او آماده میکند لیکن مرد عادل آن را خواهد پوشید، وصالحان نقره او را تقسیم خواهند نمود. | ۱۷ 17 |
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
خانه خود را مثل بید بنا میکند، و مثل سایبانی که دشتبان میسازد | ۱۸ 18 |
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
او دولتمند میخوابد اما دفن نخواهد شد. چشمان خود را میگشاید و نیست میباشد. | ۱۹ 19 |
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
ترسها مثل آب او را فرو میگیرد، و گردباد او را در شب میرباید. | ۲۰ 20 |
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
باد شرقی او رابرمی دارد و نابود میشود و او را از مکانش دورمی اندازد، | ۲۱ 21 |
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
زیرا (خدا) بر او تیر خواهدانداخت و شفقت نخواهد نمود. اگرچه اومی خواهد از دست وی فرار کرده، بگریزد. | ۲۲ 22 |
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
مردم کفهای خود را بر او بهم میزنند و او را ازمکانش صفیر زده، بیرون میکنند. | ۲۳ 23 |
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”