< ایّوب 27 >

و ایوب دیگرباره مثل خود را آورده، گفت: ۱ 1
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
«به حیات خدا که حق مرابرداشته و به قادرمطلق که جان مرا تلخ نموده است. ۲ 2
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
که مادامی که جانم در من باقی است ونفخه خدا در بینی من می‌باشد، ۳ 3
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
یقین لبهایم به بی‌انصافی تکلم نخواهد کرد، و زبانم به فریب تنطق نخواهد نمود. ۴ 4
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
حاشا از من که شما راتصدیق نمایم، و تا بمیرم کاملیت خویش را ازخود دور نخواهم ساخت. ۵ 5
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
عدالت خود را قایم نگاه می‌دارم و آن را ترک نخواهم نمود، و دلم تازنده باشم، مرا مذمت نخواهد کرد. ۶ 6
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
دشمن من مثل شریر باشد، و مقاومت کنندگانم مثل خطاکاران. ۷ 7
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
زیرا امید شریر چیست هنگامی که خدا او را منقطع می‌سازد؟ و حینی که خدا جان اورا می‌گیرد؟ ۸ 8
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
آیا خدا فریاد او را خواهد شنید، هنگامی که مصیبت بر او عارض شود؟ ۹ 9
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
آیا درقادرمطلق تلذذ خواهد یافت، و در همه اوقات ازخدا مسالت خواهد نمود؟ ۱۰ 10
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
«شما را درباره دست خدا تعلیم خواهد دادو از اعمال قادرمطلق چیزی مخفی نخواهم داشت. ۱۱ 11
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
اینک جمیع شما این را ملاحظه کرده‌اید، پس چرا بالکل باطل شده‌اید. ۱۲ 12
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
این است نصیب مرد شریر از جانب خدا، و میراث ظالمان که آن را از قادرمطلق می‌یابند. ۱۳ 13
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
اگرفرزندانش بسیار شوند شمشیر برای ایشان است، و ذریت او از نان سیر نخواهند شد. ۱۴ 14
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
بازماندگان او از وبا دفن خواهند شد، و بیوه‌زنانش گریه نخواهند کرد. ۱۵ 15
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
اگر‌چه نقره را مثل غبار اندوخته کند، و لباس را مثل گل آماده سازد. ۱۶ 16
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
او آماده می‌کند لیکن مرد عادل آن را خواهد پوشید، وصالحان نقره او را تقسیم خواهند نمود. ۱۷ 17
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
خانه خود را مثل بید بنا می‌کند، و مثل سایبانی که دشتبان می‌سازد ۱۸ 18
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
او دولتمند می‌خوابد اما دفن نخواهد شد. چشمان خود را می‌گشاید و نیست می‌باشد. ۱۹ 19
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
ترسها مثل آب او را فرو می‌گیرد، و گردباد او را در شب می‌رباید. ۲۰ 20
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
باد شرقی او رابرمی دارد و نابود می‌شود و او را از مکانش دورمی اندازد، ۲۱ 21
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
زیرا (خدا) بر او تیر خواهدانداخت و شفقت نخواهد نمود. اگر‌چه اومی خواهد از دست وی فرار کرده، بگریزد. ۲۲ 22
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
مردم کفهای خود را بر او بهم می‌زنند و او را ازمکانش صفیر زده، بیرون می‌کنند. ۲۳ 23
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< ایّوب 27 >