< ارمیا 40 >

کلامی که از جانب خداوند بر ارمیا نازل شد بعد از آنکه نبوزردان رئیس جلادان او را از رامه رهایی داد و وی را از میان تمامی اسیران اورشلیم و یهودا که به بابل جلای وطن می‌شدند و او در میان ایشان به زنجیرها بسته شده بود برگرفت. ۱ 1
Yehova anayankhula ndi Yeremiya pamene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anamasula Yeremiyayo ku Rama. Anamupeza Yeremiya ali womangidwa ndi unyolo pamodzi ndi amʼndende ena onse a ku Yerusalemu ndi a ku Yuda amene ankapita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
و رئیس جلادان ارمیا را گرفته، وی را گفت: «یهوه خدایت این بلا را درباره این مکان فرموده است. ۲ 2
Mtsogoleriyu anamupeza Yeremiya, anamuwuza kuti, “Yehova Mulungu wako analengeza kale zakuti malo ano adzawonongedwa.
و خداوند برحسب کلام خود این را به وقوع آورده، عمل نموده است. ۳ 3
Ndipo tsopano Yehova wachitadi zimenezi monga mmene ananenera. Izi zonse zachitika chifukwa anthu inu munachimwira Yehova ndipo simunamumvere.
وحال اینک من امروز تو را از زنجیرهایی که بردستهای تو است رها می‌کنم. پس اگر در نظرت پسند آید که با من به بابل بیایی بیا و تو را نیکومتوجه خواهم شد. و اگر در نظرت پسند نیاید که همراه من به بابل آیی، پس میا و بدان که تمامی زمین پیش تو است هر جایی که در نظرت خوش و پسند آید که بروی به آنجا برو.» ۴ 4
Koma tsopano taona, lero ndikukumasula unyolo umene unali mʼmanja mwako. Ngati ukufuna kupita nane ku Babuloni, tiye ndipo adzakusamala bwino. Koma ngati sukufuna kupita, ndiye usapite. Dziko ndi limeneli monga ukulioneramo. Uli ndi ufulu kupita kulikonse kumene ukufuna.”
و وقتی که او هنوز برنگشته بود (وی راگفت ): «نزد جدلیا ابن اخیقام بن شافان که پادشاه بابل او را بر شهرهای یهودا نصب کرده است برگرد و نزد او در میان قوم ساکن شو یا هر جایی که می‌خواهی بروی برو.» پس رئیس جلادان اورا توشه راه و هدیه داد و او را رها نمود. ۵ 5
Yeremiya asanayankhe, Nebuzaradani anamuwuzanso kuti, “Ngati supita ndiye pita, ubwerere kwa Gedaliya, mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, amene mfumu ya ku Babuloni inamusankha kuti akhale bwanamkubwa wa Yuda. Ukakhale naye pakati pa anthu, kapena upite kulikonse ukufuna.” Ndipo mtsogoleri uja anamupatsa Yeremiya chakudya ndi mphatso zina ndi kumulola kuti apite.
و ارمیانزد جدلیا ابن اخیقام به مصفه آمده، نزد او در میان قومی که در زمین باقی‌مانده بودند ساکن شد. ۶ 6
Motero Yeremiya anapita kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu ku Mizipa ndipo anakakhala naye kumeneko pakati pa anthu amene anatsala mʼdzikomo.
و چون تمامی سرداران لشکر که در صحرابودند و مردان ایشان شنیدند که پادشاه بابل جدلیاابن اخیقام را بر زمین نصب کرده و مردان و زنان واطفال و فقیران زمین را که به بابل برده نشده بودندبه او سپرده است، ۷ 7
Panali atsogoleri ena a nkhondo ndi anthu awo amene sanadzipereke nawo. Iwowa anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu kukhala bwanamkubwa wa dzikolo ndipo kuti yamuyika kukhala wolamulira amuna, akazi ndi ana amene anali osauka kwambiri mʼdzikomo, amene sanawagwire ukapolo kupita nawo ku Babuloni.
آنگاه ایشان نزد جدلیا به مصفه آمدند یعنی اسماعیل بن نتنیا و یوحانان ویوناتان پسران قاریح و سرایا ابن تنحومت وپسران عیفای نطوفاتی و یزنیا پسر معکاتی ایشان و مردان ایشان. ۸ 8
Iwowa anapita ku Mizipa kwa Gedaliya. Amene anapitawo ndi awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani ndi Yonatani ana a Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti, ana a Efai a ku Netofa, ndi Yezaniya mwana wa Maaka, iwowo pamodzi ndi anthu awo.
و جدلیا ابن اخیقام بن شافان برای ایشان و کسان ایشان قسم خورده، گفت: «ازخدمت نمودن به کلدانیان مترسید. در زمین ساکن شوید و پادشاه بابل را بندگی نمایید و برای شمانیکو خواهد شد. ۹ 9
Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani, anawalonjeza iwo pamodzi ndi anthuwo mwalumbiro. Ndipo anati, “Musaope kuwatumikira Ababuloni. Khalani mʼdziko muno, tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo zinthu zidzakuyenderani bwino.
و اما من اینک در مصفه ساکن خواهم شد تا به حضور کلدانیانی که نزد ما آیندحاضر شوم و شما شراب و میوه جات و روغن جمع کرده، در ظروف خود بگذارید و درشهرهایی که برای خود گرفته‌اید ساکن باشید.» ۱۰ 10
Ine ndidzakhala ku Mizipa kuti ndizikuyimirirani kwa Ababuloni amene azidzabwera kwa ife, koma inu muzikolola vinyo wanu, zipatso zanu, mafuta anu ndi kuzisunga mʼmitsuko yanu, nʼkumakhala mʼmizinda imene mwalandayo.”
و نیز چون تمامی یهودیانی که در موآب ودر میان بنی عمون و در ادوم و سایر ولایات بودندشنیدند که پادشاه بابل و بقیه‌ای از یهود راواگذاشته و جدلیا ابن اخیقام بن شافان را بر ایشان گماشته است، ۱۱ 11
Nawonso Ayuda onse a ku Mowabu, ku Amoni, ku Edomu ndi a ku mayiko ena onse anamva kuti mfumu ya ku Babuloni inasiyako anthu ena ku Yuda ndipo kuti inasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala bwanamkubwa wawo.
آنگاه جمیع یهودیان از هرجایی که پراکنده شده بودند مراجعت کردند و به زمین یهودا نزد جدلیا به مصفه آمدند و شراب ومیوه جات بسیار و فراوان جمع نمودند. ۱۲ 12
Tsono Ayuda onsewo anabwerera ku Yuda, ku Mizipa kwa Gedaliya, kuchokera ku mayiko onse kumene anabalalikira. Ndipo anakolola zipatso zochuluka ndi vinyo wambiri.
و یوحانان بن قاریح و همه سرداران لشکری که در بیابان بودند نزد جدلیا به مصفه آمدند، ۱۳ 13
Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri a ankhondo onse amene sanadzipereke aja anabwera ku Mizipa kwa Gedaliya
و او را گفتند: «آیا هیچ می‌دانی که بعلیس پادشاه بنی عمون اسماعیل بن نتنیا رافرستاده است تا تو را بکشد؟» اما جدلیا ابن اخیقام ایشان را باور نکرد. ۱۴ 14
ndipo anamufunsa kuti, “Kodi sukudziwa kuti Baalisi mfumu ya Aamoni watuma Ismaeli mwana wa Netaniya kuti akuphe?” Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu sanawankhulupirire.
پس یوحانان بن قاریح جدلیا را در مصفه خفیه خطاب کرده، گفت: «اذن بده که بروم و اسماعیل بن نتنیا رابکشم و کسی آگاه نخواهد شد. چرا او تو رابکشد و جمیع یهودیانی که نزد تو فراهم آمده اندپراکنده شوند و بقیه یهودیان تلف گردند؟» ۱۵ 15
Tsono Yohanani mwana wa Kareya, mwamseri anawuza Gedaliya ku Mizipa kuti, “Loleni ndipite ndikaphe Ismaeli mwana wa Netaniya, ndipo palibe amene ati adziwe. Akuphereninji ndi kuchititsa Ayuda onse, amene akuzungulirani kuti abalalike ndi kuti otsala a ku Yuda awonongeke?”
اماجدلیا ابن اخیقام به یوحانان بن قاریح گفت: «این کار را مکن زیرا که درباره اسماعیل دروغ می‌گویی.» ۱۶ 16
Koma Gedaliya mwana wa Ahikamu anawuza Yohanani mwana wa Kareya kuti, “Usachite zimenezo! Zimene ukunena za Ismaeli ndi zabodza.”

< ارمیا 40 >