< اشعیا 32 >

اینک پادشاهی به عدالت سلطنت خواهد نمود و سروران به انصاف حکمرانی خواهند کرد. ۱ 1
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
و مردی مثل پناه گاهی از باد و پوششی از طوفان خواهد بود. و مانندجویهای آب در جای خشک و سایه صخره عظیم در زمین تعب آورنده خواهد بود. ۲ 2
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
وچشمان بینندگان تار نخواهد شد و گوشهای شنوندگان اصغا خواهد کرد. ۳ 3
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
و دل شتابندگان معرفت را خواهد فهمید و زبان الکنان کلام فصیح را به ارتجال خواهد گفت. ۴ 4
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
و مرد لئیم بار دیگرکریم خوانده نخواهد شد و مرد خسیس نجیب گفته نخواهد گردید. ۵ 5
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
زیرا مرد لئیم به لامت متکلم خواهد شد و دلش شرارت را بعمل خواهد آورد تا نفاق را بجا آورده، به ضد خداوندبه ضلالت سخن گوید و جان گرسنگان را تهی کند و آب تشنگان را دور نماید. ۶ 6
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
آلات مرد لئیم نیز زشت است و تدابیر قبیح می‌نماید تا مسکینان را به سخنان دروغ هلاک نماید، هنگامی که مسکینان به انصاف سخن می‌گویند. ۷ 7
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
اما مردکریم تدبیرهای کریمانه می‌نماید و به کرم پایدارخواهد شد. ۸ 8
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
‌ای زنان مطمئن برخاسته، آواز مرا بشنوید وای دختران ایمن سخن مرا گوش گیرید. ۹ 9
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
‌ای دختران ایمن بعد از یک سال و چند روزی مضطرب خواهید شد زانرو که چیدن انگور قطع می‌شود و جمع کردن میوه‌ها نخواهد بود. ۱۰ 10
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
‌ای زنان مطمئن بلرزید و‌ای دختران ایمن مضطرب شوید. لباس را کنده، برهنه شوید و پلاس بر میان خود ببندید. ۱۱ 11
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
برای مزرعه های دلپسند وموهای بارور سینه خواهند زد. ۱۲ 12
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
بر زمین قوم من خار و خس خواهد رویید بلکه بر همه خانه های شادمانی در شهر مفتخر. ۱۳ 13
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
زیرا که قصر منهدم وشهر معمور متروک خواهد شد و عوفل ودیده بانگاه به بیشه‌ای سباع و محل تفرج خران وحشی و مرتع گله‌ها تا به ابد مبدل خواهد شد. ۱۴ 14
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
تا زمانی که روح از اعلی علیین بر ما ریخته شود و بیابان به بوستان مبدل گردد و بوستان به جنگل محسوب شود. ۱۵ 15
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
آنگاه انصاف در بیابان ساکن خواهد شد و عدالت در بوستان مقیم خواهد گردید. ۱۶ 16
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
و عمل عدالت سلامتی ونتیجه عدالت آرامی و اطمینان خواهد بود تاابدالاباد. ۱۷ 17
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
و قوم من در مسکن سلامتی و درمساکن مطمئن و در منزلهای آرامی ساکن خواهند شد. ۱۸ 18
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
و حین فرود آمدن جنگل تگرگ خواهد بارید و شهر به درکه اسفل خواهد افتاد. ۱۹ 19
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
خوشابحال شما که بر همه آبها تخم می‌کاریدو پایهای گاو و الاغ را رها می‌سازید. ۲۰ 20
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

< اشعیا 32 >