< اشعیا 11 >

و نهالی از تنه یسی بیرون آمده، شاخه‌ای از ریشه هایش خواهدشکفت. ۱ 1
Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.
و روح خداوند بر او قرار خواهدگرفت، یعنی روح حکمت و فهم و روح مشورت و قوت و روح معرفت و ترس خداوند. ۲ 2
Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu, Mzimu wauphungu ndi wamphamvu, Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.
وخوشی او در ترس خداوند خواهد بود و موافق رویت چشم خود داوری نخواهد کرد و بر وفق سمع گوشهای خویش تنبیه نخواهد نمود. ۳ 3
Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa. Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso, kapena kugamula mlandu potsata zakumva;
بلکه مسکینان را به عدالت داوری خواهد کرد و به جهت مظلومان زمین براستی حکم خواهد نمود. و جهان را به عصای دهان خویش زده، شریران رابه نفخه لبهای خود خواهد کشت. ۴ 4
koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo, adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi. Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake; atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.
و کمربندکمرش عدالت خواهد بود و کمربند میانش امانت. ۵ 5
Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.
و گرگ با بره سکونت خواهد داشت و پلنگ با بزغاله خواهد خوابید و گوساله و شیر و پرواری با هم، و طفل کوچک آنها را خواهد راند. ۶ 6
Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi, mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.
و گاوبا خرس خواهد چرید و بچه های آنها با هم خواهند خوابید و شیر مثل گاو کاه خواهد خورد. ۷ 7
Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi, ana awo adzagona pamodzi, ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.
و طفل شیرخواره بر سوراخ مار بازی خواهدکرد و طفل از شیر باز داشته شده دست خود را برخانه افعی خواهد گذاشت. ۸ 8
Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba, ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.
و در تمامی کوه مقدس من ضرر و فسادی نخواهند کرد زیرا که جهان از معرفت خداوند پر خواهد بود مثل آبهایی که دریا را می‌پوشاند. ۹ 9
Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga pa phiri lopatulika la Yehova, pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.
و در آن روز واقع خواهد شد که ریشه یسی به جهت علم قوم‌ها برپا خواهد شد و امت هاآن را خواهند طلبید و سلامتی او با جلال خواهدبود. ۱۰ 10
Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero.
و در آن روز واقع خواهد گشت که خداوند بار دیگر دست خود را دراز کند تا بقیه قوم خویش را که از آشور و مصر و فتروس وحبش و عیلام و شنعار و حمات و از جزیره های دریا باقی‌مانده باشند باز آورد. ۱۱ 11
Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.
و به جهت امت‌ها علمی برافراشته، رانده شدگان اسرائیل را جمع خواهد کرد، وپراکندگان یهودا را از چهار طرف جهان فراهم خواهد آورد. ۱۲ 12
Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera, ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli; Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.
و حسد افرایم رفع خواهد شد ودشمنان یهودا منقطع خواهند گردید. افرایم بریهودا حسد نخواهد برد و یهودا افرایم را دشمنی نخواهد نمود. ۱۳ 13
Nsanje ya Efereimu idzatha, ndipo adani a Yuda adzatha; Efereimu sadzachitira nsanje Yuda, ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.
و به‌جانب مغرب بر دوش فلسطینیان پریده، بنی مشرق را با هم غارت خواهند نمود. و دست خود را بر ادوم و موآب دراز کرده، بنی عمون ایشان را اطاعت خواهندکرد. ۱۴ 14
Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo; ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa. Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu, ndipo Aamoni adzawagonjera.
و خداوند زبانه دریای مصر را تباه ساخته، دست خود را با باد سوزان بر نهر درازخواهد کرد، و آن را با هفت نهرش خواهد زد ومردم را با کفش به آن عبور خواهد داد. ۱۵ 15
Yehova adzaphwetsa mwendo wa nyanja ya Igupto; adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha pa mtsinje wa Yufurate. Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.
و به جهت بقیه قوم او که از آشور باقی‌مانده باشند شاه راهی خواهد بود. چنانکه به جهت اسرائیل در روز بر‌آمدن ایشان از زمین مصربود. ۱۶ 16
Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira amene anatsalira ku Asiriya, monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli pamene amachokera ku Igupto.

< اشعیا 11 >