< حزقیال 5 >

بگیر و آن را مثل استره حجام به جهت خود بکار برده، آن را بر سر و ریش خود بگذران وترازویی گرفته، مویها را تقسیم کن. ۱ 1
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
و چون روزهای محاصره را به اتمام رسانیده باشی، یک ثلث را در میان شهر به آتش بسوزان و یک ثلث راگرفته، اطراف آن را با تیغ بزن و ثلث دیگر را به بادها بپاش و من در عقب آنها شمشیری خواهم فرستاد. ۲ 2
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
و اندکی از آن را گرفته، آنها را در دامن خود ببند. ۳ 3
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
و باز قدری از آنها را بگیر و آنها را درمیان آتش انداخته، آنها را به آتش بسوزان وآتشی برای تمام خاندان اسرائیل از آن بیرون خواهد آمد.» ۴ 4
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
خداوند یهوه چنین می‌گوید: «من این اورشلیم را در میان امت‌ها قرار دادم و کشورها رابهر طرف آن. ۵ 5
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
و او از احکام من بدتر از امت‌ها واز فرایض من بدتر از کشورهایی که گرداگرد اومی باشد، عصیان ورزیده است زیرا که اهل او احکام مرا ترک کرده، به فرایض من سلوک ننموده‌اند.» ۶ 6
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
بنابراین خداوند یهوه چنین می‌گوید: «چونکه شما زیاده از امت هایی که گرداگرد شما می‌باشند غوغا نمودید و به فرایض من سلوک نکرده، احکام مرا بعمل نیاوردید، بلکه موافق احکام امت هایی که گرداگرد شما می‌باشندنیز عمل ننمودید، ۷ 7
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
لهذا خداوند یهوه چنین می‌گوید: من اینک من به ضد تو هستم و در میان تو به نظر امت‌ها داوریها خواهم نمود. ۸ 8
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
و با تو به‌سبب جمیع رجاساتت کارها خواهم کرد که قبل از این نکرده باشم و مثل آنها هم دیگر نخواهم کرد. ۹ 9
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
بنابراین پدران در میان تو پسران راخواهند خورد و پسران پدران خویش را خواهندخورد و بر تو داوریها نموده، تمامی بقیت تو رابسوی هر باد پراکنده خواهم ساخت.» ۱۰ 10
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
لهذاخداوند یهوه می‌گوید: «به حیات خودم قسم چونکه تو مقدس مرا بتمامی رجاسات و جمیع مکروهات خویش نجس ساختی، من نیز البته تورا منقطع خواهم ساخت و چشم من شفقت نخواهد نمود و من نیز رحمت نخواهم فرمود. ۱۱ 11
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
یک ثلث تو در میانت از وبا خواهند مرد و ازگرسنگی تلف خواهند شد. و یک ثلث به اطرافت به شمشیر خواهند افتاد و ثلث دیگر را بسوی هرباد پراکنده ساخته، شمشیر را در عقب ایشان خواهم فرستاد. ۱۲ 12
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
پس چون غضب من به اتمام رسیده باشد و حدت خشم خویش را بر ایشان ریخته باشم، آنگاه پشیمان خواهم شد. و چون حدت خشم خویش را بر ایشان به اتمام رسانده باشم، آنگاه خواهند دانست که من یهوه این را درغیرت خویش گفته‌ام. ۱۳ 13
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
و تو را در در نظر همه رهگذریان در میان امت هایی که به اطراف تومی باشند، به خرابی و رسوایی تسلیم خواهم نمود. ۱۴ 14
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
و چون بر تو به خشم و غضب وسرزنشهای سخت داوری کرده باشم، آنگاه این موجد عار و مذمت و عبرت و دهشت برای امت هایی که به اطراف تو می‌باشند خواهد بود. من که یهوه هستم این را گفتم. ۱۵ 15
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
و چون تیرهای بد قحطی را که برای هلاکت می‌باشد و من آنها رابه جهت خرابی شما می‌فرستم در میان شماانداخته باشم، آنگاه قحط را بر شما سخت‌ترخواهم گردانید و عصای نان شما را خواهم شکست. ۱۶ 16
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
و قحط و حیوانات درنده در میان توخواهم فرستاد تا تو را بی‌اولاد گردانند و وبا وخون از میان تو عبور خواهد کرد و شمشیری برتو وارد خواهم آورد. من که یهوه هستم این راگفتم.» ۱۷ 17
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< حزقیال 5 >