< دانیال 6 >

و داریوش مصلحت دانست که صد و بیست والی بر مملکت نصب نماید تا بر تمامی مملکت باشند. ۱ 1
Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse,
و بر آنهاسه وزیر که یکی از ایشان دانیال بود تا آن والیان به ایشان حساب دهند و هیچ ضرری به پادشاه نرسد. ۲ 2
ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke.
پس این دانیال بر سایر وزراء و والیان تفوق جست زیرا که روح فاضل دراو بود وپادشاه اراده داشت که او را بر تمامی مملکت نصب نماید. ۳ 3
Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse.
پس وزیران و والیان بهانه می‌جستند تا شکایتی در امور سلطنت بر دانیال بیاورند اما نتوانستند که هیچ علتی یا تقصیری بیابند، چونکه او امین بود و خطایی یا تقصیری دراو هرگز یافت نشد. ۴ 4
Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito.
پس آن اشخاص گفتند که «در این دانیال هیچ علتی پیدا نخواهیم کرد مگراینکه آن را درباره شریعت خدایش در او بیابیم.» ۵ 5
Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”
آنگاه این وزراء و والیان نزد پادشاه جمع شدند و او را چنین گفتند: «ای داریوش پادشاه تابه ابد زنده باش. ۶ 6
Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali!
جمیع وزرای مملکت و روسا و والیان و مشیران و حاکمان با هم مشورت کرده‌اند که پادشاه حکمی استوار کند و قدغن بلیغی نماید که هر کسی‌که تا سی روز از خدایی یا انسانی سوای تو‌ای پادشاه مسالتی نماید درچاه شیران افکنده شود. ۷ 7
Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango.
پس‌ای پادشاه فرمان رااستوار کن و نوشته را امضا فرما تا موافق شریعت مادیان و فارسیان که منسوخ نمی شود تبدیل نگردد.» ۸ 8
Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.”
بنابراین داریوش پادشاه نوشته وفرمان را امضا نمود. ۹ 9
Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.
اما چون دانیال دانست که نوشته امضا شده است به خانه خود درآمد و پنجره های بالاخانه خود را به سمت اورشلیم باز نموده، هر روز سه مرتبه زانو می‌زد و دعا می‌نمود و چنانکه قبل ازآن عادت می‌داشت نزد خدای خویش دعامی کرد و تسبیح می‌خواند. ۱۰ 10
Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale.
پس آن اشخاص جمع شده، دانیال را یافتند که نزد خدای خودمسالت و تضرع می‌نماید. ۱۱ 11
Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize.
آنگاه به حضور پادشاه نزدیک شده، درباره فرمان پادشاه عرض کردند که «ای پادشاه آیافرمانی امضا ننمودی که هر‌که تا سی روز نزدخدایی یا انسانی سوای تو‌ای پادشاه مسالتی نماید در چاه شیران افکنده شود؟» پادشاه درجواب گفت: «این امر موافق شریعت مادیان وفارسیان که منسوخ نمی شود صحیح است.» ۱۲ 12
Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?” Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”
پس ایشان در حضور پادشاه جواب دادند وگفتند که «این دانیال که از اسیران یهودا می‌باشد به تو‌ای پادشاه و به فرمانی که امضا نموده‌ای اعتنانمی نماید، بلکه هر روز سه مرتبه مسالت خود رامی نماید.» ۱۳ 13
Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.”
آنگاه پادشاه چون این سخن راشنید بر خویشتن بسیار خشمگین گردید و دل خود را به رهانیدن دانیال مشغول ساخت و تاغروب آفتاب برای استخلاص او سعی می‌نمود. ۱۴ 14
Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.
آنگاه آن اشخاص نزد پادشاه جمع شدند و به پادشاه عرض کردند که «ای پادشاه بدان که قانون مادیان و فارسیان این است که هیچ فرمان یاحکمی که پادشاه آن را استوار نماید تبدیل نشود.» ۱۵ 15
Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”
پس پادشاه امر فرمود تا دانیال را بیاورند واو را در چاه شیران بیندازند و پادشاه دانیال راخطاب کرده، گفت: «خدای تو که او را پیوسته عبادت می‌نمایی تو را رهایی خواهد داد.» ۱۶ 16
Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”
وسنگی آورده، آن را بر دهنه چاه نهادند و پادشاه آن را به مهر خود و مهر امرای خویش مختوم ساخت تا امر درباره دانیال تبدیل نشود. ۱۷ 17
Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli.
آنگاه پادشاه به قصر خویش رفته، شب را به روزه بسربرد و به حضور وی اسباب عیش او را نیاوردند وخوابش از او رفت. ۱۸ 18
Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.
پس پادشاه صبح زود وقت طلوع فجر برخاست و به تعجیل به چاه شیران رفت. ۱۹ 19
Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija.
و چون نزد چاه شیران رسید به آوازحزین دانیال را صدا زد و پادشاه دانیال را خطاب کرده، گفت: «ای دانیال بنده خدای حی آیاخدایت که او را پیوسته عبادت می‌نمایی به رهانیدنت از شیران قادر بوده است؟» ۲۰ 20
Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”
آنگاه دانیال به پادشاه جواب داد که «ای پادشاه تا به ابد زنده باش! ۲۱ 21
Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali!
خدای من فرشته خود را فرستاده، دهان شیران را بست تا به من ضرری نرسانند چونکه به حضور وی در من گناهی یافت نشد و هم درحضور تو‌ای پادشاه تقصیری نورزیده بودم.» ۲۲ 22
Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”
آنگاه پادشاه بی‌نهایت شادمان شده، امر فرمود که دانیال را از چاه برآورند و دانیال را از چاه برآوردند و از آن جهت که بر خدای خود توکل نموده بود در اوهیچ ضرری یافت نشد. ۲۳ 23
Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.
و پادشاه امر فرمود تاآن اشخاص را که بر دانیال شکایت آورده بودندحاضر ساختند و ایشان را با پسران و زنان ایشان در چاه شیران انداختند و هنوز به ته چاه نرسیده بودند که شیران بر ایشان حمله آورده، همه استخوانهای ایشان را خرد کردند. ۲۴ 24
Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.
بعد از آن داریوش پادشاه به جمیع قومها و امت‌ها وزبانهایی که در تمامی جهان ساکن بودند نوشت که «سلامتی شما افزون باد! ۲۵ 25
Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti, “Mtendere uchuluke pakati panu!
از حضور من فرمانی صادر شده است که در هر سلطنتی ازممالک من (مردمان ) به حضور خدای دانیال لرزان و ترسان باشند زیرا که او خدای حی و تاابدالاباد قیوم است. و ملکوت او بی‌زوال وسلطنت او غیرمتناهی است. ۲۶ 26
“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.
او است که نجات می‌دهد و می‌رهاند و آیات و عجایب را درآسمان و در زمین ظاهر می‌سازد و اوست که دانیال را از چنگ شیران رهایی داده است.» ۲۷ 27
Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,
پس این دانیال در سلطنت داریوش و درسلطنت کورش فارسی فیروز می‌بود. ۲۸ 28
Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

< دانیال 6 >