< اول سموئیل 24 >

و واقع شد بعد از برگشتن شاول از عقب فلسطینیان که او را خبر داده، گفتند: «اینک داود در بیابان عین جدی است.» ۱ 1
Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
و شاول سه هزار نفر برگزیده را از تمامی اسرائیل گرفته، برای جستجوی داود و کسانش بر صخره های بزهای کوهی رفت. ۲ 2
Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
و به‌سر راه به آغلهای گوسفندان که در آنجا مغاره‌ای بود، رسید. وشاول داخل آن شد تا پایهای خود را بپوشاند. وداود و کسان او در جانبهای مغاره نشسته بودند. ۳ 3
Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
و کسان داود وی را گفتند: «اینک روزی که خداوند به تو وعده داده است که همانا دشمن تورا به‌دستت تسلیم خواهم نمود تا هر‌چه درنظرت پسند آید به او عمل نمایی.» و داودبرخاسته، دامن ردای شاول را آهسته برید. ۴ 4
Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
وبعد از آن دل داود مضطرب شد از این جهت که دامن شاول را بریده بود. ۵ 5
Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
و به کسان خود گفت: «حاشا بر من از جانب خداوند که این امر را به آقای خود مسیح خداوند بکنم، و دست خود رابر او دراز نمایم چونکه او مسیح خداوند است.» ۶ 6
Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
پس داود کسان خود را به این سخنان توبیخ نموده، ایشان را نگذاشت که بر شاول برخیزند، وشاول از مغاره برخاسته، راه خود را پیش گرفت. ۷ 7
Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
و بعد از آن، داود برخاسته، از مغاره بیرون رفت و در عقب شاول صدا زده، گفت: «ای آقایم پادشاه.» و چون شاول به عقب خود نگریست داود رو به زمین خم شده، تعظیم کرد. ۸ 8
Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
و داود به شاول گفت: «چرا سخنان مردم را می‌شنوی که می‌گویند اینک داود قصد اذیت تو را دارد. ۹ 9
Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
اینک امروز چشمانت دیده است که چگونه خداوند تو را در مغاره امروز به‌دست من تسلیم نمود، و بعضی گفتند که تو را بکشم، اما چشمم برتو شفقت نموده، گفتم دست خود را بر آقای خویش دراز نکنم، زیرا که مسیح خداوند است. ۱۰ 10
Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
و‌ای پدرم ملاحظه کن و دامن ردای خود را دردست من ببین، زیرا از اینکه جامه تو را بریدم و تورا نکشتم بدان و ببین که بدی و خیانت در دست من نیست، و به تو گناه نکرده‌ام، اما تو جان مراشکار می‌کنی تا آن را گرفتار سازی. ۱۱ 11
Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
خداونددر میان من و تو حکم نماید، و خداوند انتقام مرااز تو بکشد اما دست من بر تو نخواهد شد. ۱۲ 12
Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
چنانکه مثل قدیمان می‌گوید که شرارت ازشریران صادر می‌شود اما دست من بر تو نخواهدشد. ۱۳ 13
Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
و در عقب کیست که پادشاه اسرائیل بیرون می‌آید و کیست که او را تعاقب می‌نمایی، در عقب سگ مرده‌ای بلکه در عقب یک کیک! ۱۴ 14
“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
پس خداوند داور باشد و میان من و تو حکم نماید و ملاحظه کرده دعوی مرا با تو فیصل کند ومرا از دست تو برهاند.» ۱۵ 15
Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
و چون داود از گفتن این سخنان به شاول فارغ شد، شاول گفت: «آیا این آواز توست‌ای پسر من داود.» و شاول آواز خود را بلند کرده، گریست. ۱۶ 16
Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
و به داود گفت: «تو از من نیکوترهستی زیرا که تو جزای نیکو به من رسانیدی و من جزای بد به تو رسانیدم. ۱۷ 17
Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
و تو امروز ظاهرکردی که چگونه به من احسان نمودی چونکه خداوند مرا به‌دست تو تسلیم کرده، و مرانکشتی. ۱۸ 18
Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
و اگر کسی دشمن خویش را بیابد، آیا او را به نیکویی رها نماید؟ پس خداوند تو را به نیکویی جزا دهد به‌سبب آنچه امروز به من کردی. ۱۹ 19
Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
و حال اینک می‌دانم که البته پادشاه خواهی شد و سلطنت اسرائیل در دست تو ثابت خواهد گردید. ۲۰ 20
Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
پس الان برای من قسم به خداوند بخور که بعد از من ذریه مرا منقطع نسازی، و اسم مرا از خاندان پدرم محو نکنی.» ۲۱ 21
Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
و داود برای شاول قسم خورد، و شاول به خانه خود رفت و داود و کسانش به مامن خویش آمدند. ۲۲ 22
Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

< اول سموئیل 24 >