< اول تواریخ 14 >
و حيرام پادشاه صور، قاصدان با چوب سرو آزاد و بنايان و نجاران نزد داود فرستاده تا خانه اي براي او بسازند. | ۱ 1 |
Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
و داود دانست که خداوند او را به پادشاهي اسرائيل استوار داشته است، زيرا که سلطنتش به خاطر قوم او اسرائيل به درجه بلند برافراشته شده بود. | ۲ 2 |
Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
و داود در اورشليم با زنان گرفت، و داود پسران و دختران ديگر توليد نمود. | ۳ 3 |
Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
و اين است نامهاي فرزنداني که در اورشليم براي وي به هم رسيدند: شَمُّوع و شُوباب و ناتان و سُليمان، | ۴ 4 |
Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
و یبحار و اَلِيشُوع و اَلِيفالَط، | ۵ 5 |
Ibihari, Elisua, Elipeleti,
و نُوجَه و نافَج و يافِيع، | ۶ 6 |
Noga, Nefegi, Yafiya,
و اَلِيشامَع و بَعلياداع و اَلِيفَلَط. پيروزي داود بر فلسطينيان | ۷ 7 |
Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
و چون فلسطينيان شنيدند که داود به پادشاهي تمام اسرائيل مسح شده است، پس فلسطينيان برآمدند تا داود را (براي جنگ) بطلبند؛ و چون داود شنيد، به مقابله ايشان برآمد. | ۸ 8 |
Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
و فلسطينيان آمده، در وادي رفائيم منتشر شدند. | ۹ 9 |
Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
و داود از خدا مسألت نموده، گفت: « آيا به مقابله فلسطينيان برآيم و آيا ايشان را به دست من تسليم خواهي نمود؟» خداوند او را گفت: « برآي وايشان را به دست تو تسليم خواهم کرد.» | ۱۰ 10 |
Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
پس به بَعل فَراصِيم برآمدند و داود ايشان را در آنجا شکست داد و داود گفت: « خدا بر دشمنان من به دست من مثل رخنه آب رخنه کرده است.» بنابراين آن مکان را بَعل فَراصِيم نام نهادند. | ۱۱ 11 |
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
و خدايان خود را در آنجا ترک کردند و داود امر فرمود که آنها را به آتش بسوزانند. | ۱۲ 12 |
Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
و فلسطينيان بار ديگر در آن وادي منتشر شدند. | ۱۳ 13 |
Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
و داود باز از خدا سؤال نمود و خدا او را گفت: « از عقب ايشان مرو بلکه از ايشان رو گردانيده، در مقابل درختان توت به ايشان نزديک شو. | ۱۴ 14 |
Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
و چون در سر درختان توت آواز قدمها بشنوي، آنگاه براي جنگ بيرون شو، زيرا خدا پيش روي تو بيرون رفته است تا لشکر فلسطينيان را مغلوب سازد.» | ۱۵ 15 |
Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
پس داود بر وفق آنچه خدا اورا امر فرموده بود، عمل نمود و لشکر فلسطينيان را از جِبعُون تا جارز شکست دادند. | ۱۶ 16 |
Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
و اسم داود در جميع اراضي شيوع يافت و خداوند ترس او را بر تمامي امّت ها مستولي ساخت. | ۱۷ 17 |
Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.