< اول تواریخ 14 >

و حيرام پادشاه صور، قاصدان با چوب سرو آزاد و بنايان و نجاران نزد داود فرستاده تا خانه اي براي او بسازند. ۱ 1
Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
و داود دانست که خداوند او را به پادشاهي اسرائيل استوار داشته است، زيرا که سلطنتش به خاطر قوم او اسرائيل به درجه بلند برافراشته شده بود. ۲ 2
Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
و داود در اورشليم با زنان گرفت، و داود پسران و دختران ديگر توليد نمود. ۳ 3
Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
و اين است نامهاي فرزنداني که در اورشليم براي وي به هم رسيدند: شَمُّوع و شُوباب و ناتان و سُليمان، ۴ 4
Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
و یبحار و اَلِيشُوع و اَلِيفالَط، ۵ 5
Ibihari, Elisua, Elipeleti,
و نُوجَه و نافَج و يافِيع، ۶ 6
Noga, Nefegi, Yafiya,
و اَلِيشامَع و بَعلياداع و اَلِيفَلَط. پيروزي داود بر فلسطينيان ۷ 7
Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
و چون فلسطينيان شنيدند که داود به پادشاهي تمام اسرائيل مسح شده است، پس فلسطينيان برآمدند تا داود را (براي جنگ) بطلبند؛ و چون داود شنيد، به مقابله ايشان برآمد. ۸ 8
Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
و فلسطينيان آمده، در وادي رفائيم منتشر شدند. ۹ 9
Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
و داود از خدا مسألت نموده، گفت: « آيا به مقابله فلسطينيان برآيم و آيا ايشان را به دست من تسليم خواهي نمود؟» خداوند او را گفت: « برآي وايشان را به دست تو تسليم خواهم کرد.» ۱۰ 10
Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
پس به بَعل فَراصِيم برآمدند و داود ايشان را در آنجا شکست داد و داود گفت: « خدا بر دشمنان من به دست من مثل رخنه آب رخنه کرده است.» بنابراين آن مکان را بَعل فَراصِيم نام نهادند. ۱۱ 11
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
و خدايان خود را در آنجا ترک کردند و داود امر فرمود که آنها را به آتش بسوزانند. ۱۲ 12
Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
و فلسطينيان بار ديگر در آن وادي منتشر شدند. ۱۳ 13
Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
و داود باز از خدا سؤال نمود و خدا او را گفت: « از عقب ايشان مرو بلکه از ايشان رو گردانيده، در مقابل درختان توت به ايشان نزديک شو. ۱۴ 14
Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
و چون در سر درختان توت آواز قدمها بشنوي، آنگاه براي جنگ بيرون شو، زيرا خدا پيش روي تو بيرون رفته است تا لشکر فلسطينيان را مغلوب سازد.» ۱۵ 15
Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
پس داود بر وفق آنچه خدا اورا امر فرموده بود، عمل نمود و لشکر فلسطينيان را از جِبعُون تا جارز شکست دادند. ۱۶ 16
Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
و اسم داود در جميع اراضي شيوع يافت و خداوند ترس او را بر تمامي امّت ها مستولي ساخت. ۱۷ 17
Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

< اول تواریخ 14 >