< اول تواریخ 12 >

و اينانند که نزد داود به صِقلَغ آمدند، هنگامي که او هنوز از ترس شاؤل بن قَيس گرفتار بود، و ايشان از آن شجاعان بودند که در جنگ معاون او بودند. ۱ 1
Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
و به کمان مسلح بودند و سنگها و تيرها از کمانها از دست راست و دست چپ مي انداختند و از برادران شاؤل بنياميني بودند. ۲ 2
Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
سردار ايشان اَخيعَزَر بود، و بعد از او يوآش پسران شَماعَه جِبعاتي و يزيئيل و فالَط پسران عَزمُوت و بَراکَه و ييهُوي عناتوتي، ۳ 3
Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
و يشمَعياي جِبعُوني که در ميان آن سي نفر شجاع بود، و بر آن سي نفر برتري داشت و اِرميا و يحزيئيل و يوحانان و يوزابادِ جَديراتي، ۴ 4
ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
و اَلعُوزاي و يريموت وبَعلِيا و شَمَريا و شَفَطياي حَرُوفي، ۵ 5
Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
و اَلقانَه و يشَيا و عَزَرئيل و يوعَزَر و يشُبعام که از قُورَحيان بودند، ۶ 6
Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
ويوعيلَه و زَبديا پسران يرُوحام جَدوري. ۷ 7
ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
و بعضي از جاديان که مردان قوي شجاع و مردان جنگ آزموده و مسلح به سپر و تيراندازان که روي ايشان مثل روي شير و مانند غزال کوهي تيزرو بودند، خوشتن را نزد داود در ملاذ بيابان جدا ساختند، ۸ 8
Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
که رئيس ايشان عازَر و دومين عُوبَديا و سومين اَلِيآب بود، ۹ 9
Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
و چهارمين مِشمَنَّه و پنجمين اِرميا، ۱۰ 10
wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
و ششم عَتّاي و هفتم اَلِيئيل، ۱۱ 11
wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
و هشتم يوحانان و نهم اَلزاباد، ۱۲ 12
wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
و دهم اِرميا و يازدهم مَکبَنَّاي. ۱۳ 13
wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
اينان از بني جاد رؤساي لشکر بودند که کوچکتر ايشان برابر صد نفر و بزرگتر برابر هزار نفر مي بود. ۱۴ 14
Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
اينانند که در ماه اول از اُردُن عبور نمودند هنگامي که آن از تمامي حدودش سيلان کرده بود و جميع ساکنان و اديها را هم به طرف مشرق و هم به طرف مغرب منهزم ساختند. ۱۵ 15
Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
و بعضي از بني بنيامين و يهودا نزد داود به آن ملاذ آمدند. ۱۶ 16
Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
داود به استقبال ايشان بيرون آمده، ايشان را خطاب کرده، گفت: « اگر با سلامتي براي اعانت من نزد من آمديد، دل من با شما ملصق خواهد شد؛ و اگر براي تسليم نمودن من به دست دشمنانم آمديد، با آنکه ظلمي در دست من نيست، پس خداي پدران ما اين را ببيند و انصاف نمايد.» ۱۷ 17
Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
آنگاه روح بر عماساي که رئيس شلاشيم بود نازل شد (و او گفت): « اي داود ما از آن تو و اي پسر يسي ما با تو هستيم؛ سلامتي، سلامتي بر تو باد، و سلامتي بر انصار تو باد زيرا خداي تو نصرت دهنده تو است.» پس داود ايشان را پذيرفته، سرداران لشکر ساخت. ۱۸ 18
Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
و بعضي از مَنَّسي به داود ملحق شدند هنگامي که او همراه فلسطينيان براي مقاتله با شاؤل مي رفت؛ اما ايشان را مدد نکردند زيرا که سرداران فلسطينيان بعد از مشورت نمودن، او را پس فرستاده، گفتند که: « او با سرهاي ما به آقاي خود شاؤل ملحق خواهد شد.» ۱۹ 19
Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
و هنگامي که به صِقلَغ مي رفت، بعضي از مَنَّسي به او پيوستند يعني عَدناح و يوزاباد و يدِيعَئيل و ميکائيل و يوزاباد و اَلِيهُو و صِلتاي که سرداران هزارهاي مَنَّسي بودند. ۲۰ 20
Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
ايشان داود را به مقاومت فوجهاي (عَمالَقه) مدد کردند، زيرا جميع ايشان مردان قوي شجاع و سردار لشکر بودند. ۲۱ 21
Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
زيرا در آن وقت، روز به روز براي اعانت داود نزد وي مي آمدند تا لشکرِ بزرگ، مثل لشکر خدا شد. ۲۲ 22
Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
و اين است شماره افراد آناني که براي جنگ مسلح شده، نزد داود به حَبرُون آمدند تا سلطنت شاؤل را بر حسب فرمان خداوند به وي تحويل نمايند. ۲۳ 23
Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
از بني يهودا شش هزار و هشتصد نفر که سپر و نيزه داشتند و مسلح جنگ بودند. ۲۴ 24
Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
از بني شَمعون هفت هزار و يکصد نفر که مردان قوي شجاع براي جنگ بودند. ۲۵ 25
Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
از بني لاوي چهار هزار و ششصد نفر. ۲۶ 26
Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
و يهُوياداع رئيس بني هارون و سه هزار و هفتصد نفر همراه وي. ۲۷ 27
mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
و صادوق که جوان قوي و شجاع بود با بيست ودو سردار از خاندان پدرش. ۲۸ 28
ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
و از بني بنيامين سه هزار نفر از برادران شاؤل و تا آن وقت اکثر ايشان وفاي خاندان شاؤل را نگاه مي داشتند. ۲۹ 29
Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
و از بني افرايم بيست هزار و هشتصد نفر که مردان قوي و شجاع و در خاندان پدران خويش نامور بودند. ۳۰ 30
Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
و از نصف سبط مَنَّسي هجده هزار نفر که به نامهاي خود تعيين شده بودند که بيايند و داود را به پادشاهي نصب نمايند. ۳۱ 31
Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
و از بني يسّاکار کساني که از زمانها مخبر شده، مي فهميدند که اسرائيليان چه بايد بکنند، سرداران ايشان دوست نفر و جميع برادران ايشان فرمان بردار ايشان بودند. ۳۲ 32
Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
و از زبولون پنجاه هزار نفر که با لشکر بيرون رفته، مي توانستند جنگ را با همه آلات حرب بيارايند و صف آرايي کنند و دو دل نبودند. ۳۳ 33
Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
و از نَفتالي هزار سردار و با ايشان سي و هفت هزار نفر با سپر و نيزه. ۳۴ 34
Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
و از بني دان بيست و هشت هزار و ششصد نفر براي جنگ مهيا شدند. ۳۵ 35
Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
و از اَشِير چهل هزار نفر که با لشکر بيرون رفته، مي توانستند جنگ را مهيا سازند. ۳۶ 36
Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
و از آن طرف اُردُن از بني جاد و نصف سبط مَنَّسي صد و بيست هزار نفر که با جميع آلات لشکر براي جنگ (مهيا شدند). ۳۷ 37
Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
جميع اينها مردان جنگي بودند که بر صف آرائي قادر بودند با دل کامل به حَبرُون آمدند تا داود را بر تمامي اسرائيل به پادشاهي نصب نمايند، و تمامي بقيه اسرائيل نيز براي پادشاه ساختن داود يک دل بودند. ۳۸ 38
Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
و در آنجا با داود سه روز اکل و شرب نمودند زيرا که برادران ايشان به جهت ايشان تدارک ديده بودند. ۳۹ 39
Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
و مجاوران ايشان نيز تا يسّاکار و زبولون و نَفتالي نان بر الاغها و شتران و قاطران و گاوان آوردند و مأکولات از آرد و قرصهاي انجير و کشمش و شراب و روغن و گاوان و گوسفندان به فراواني آوردند چونکه در اسرائيل شادماني بود. ۴۰ 40
Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

< اول تواریخ 12 >