< 1 Kongebok 21 >

1 Nogen tid efter hendte det som nu skal fortelles: Jisre'elitten Nabot hadde en vingård i Jisre'el ved siden av et slott som tilhørte Akab, kongen i Samaria.
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
2 Akab talte med Nabot og sa: Gi mig din vingård, så jeg kan ha den til kjøkkenhave! For den ligger tett ved mitt hus. Jeg vil gi dig en bedre vingård i stedet for den; eller om du så synes, vil jeg gi dig så meget i penger som den er verd.
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
3 Men Nabot svarte: Herren la det være langt fra mig å gi dig min fedrene arv.
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
4 Så gikk Akab hjem mismodig og harm for det svar jisre'elitten Nabot hadde gitt ham da han sa: Jeg vil ikke gi dig min fedrene arv. Og han la sig på sin seng og vendte ansiktet bort og vilde ikke ete.
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
5 Da kom hans hustru Jesabel inn til ham, og hun spurte ham: Hvorfor er du så mismodig og vil ikke ete?
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
6 Han svarte: Jeg talte med jisre'elitten Nabot og sa til ham: Gi mig din vingård for penger, eller om du ønsker, vil jeg gi dig en annen vingård i stedet. Men han sa: Jeg vil ikke gi dig min vingård.
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
7 Da sa hans hustru Jesabel til ham: Du får nu vise at du er konge over Israel; stå op, et og vær vel til mote! Jeg skal sørge for at du får jisre'elitten Nabots vingård.
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
8 Så skrev hun et brev i Akabs navn og satte segl på det med hans signetring; og hun sendte brevet til de eldste og fornemste i hans by, de som bodde sammen med Nabot.
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
9 Og i brevet skrev hun således: Utrop en faste og la Nabot sitte øverst blandt folket,
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
10 og la to onde menn sitte midt imot ham, sa de kan vidne mot ham og si: Du har bannet Gud og kongen. Før ham så ut og sten ham ihjel!
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
11 Og mennene i byen, de eldste og fornemste som bodde i hans by, gjorde som Jesabel hadde sendt dem bud om, således som det var skrevet i det brev hun hadde sendt dem.
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
12 De utropte en faste og lot Nabot sitte øverst blandt folket,
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
13 og de to onde menn kom og satte sig midt imot ham; og de onde menn vidnet mot Nabot i folkets påhør og sa: Nabot har bannet Gud og kongen. Og de førte ham utenfor byen og stenet ham ihjel.
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
14 Så sendte de bud til Jesabel og lot si: Nabot er blitt stenet og er død.
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
15 Med det samme Jesabel hørte at Nabot var blitt stenet og var død, sa hun til Akab: Stå op og ta jisre'elitten Nabots vingård i eie, den som han ikke vilde la dig få for penger! For Nabot lever ikke lenger; han er død.
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
16 Da Akab hørte at Nabot var død, stod han op for å gå ned til Jisre'elitten Nabots vingård og ta den eie.
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
17 Men Herrens ord kom til tisbitten Elias, og det lød således:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
18 Gjør dig rede og gå ned og møt Akab, Israels konge, som bor i Samaria! Nu er han i Nabots vingård; han er gått der ned for å ta den i eie.
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
19 Og du skal tale således til ham: Så sier Herren: Har du nu både myrdet og arvet? Og du skal si til ham: Så sier Herren: På det sted hvor hundene slikket Nabots blod, skal hundene også slikke ditt blod.
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
20 Men Akab sa til Elias: Har du funnet mig, du min fiende? Han svarte: Ja, jeg har funnet dig, fordi du har solgt dig til å gjøre hvad ondt er i Herrens øine.
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
21 Derfor vil jeg føre ulykke over dig og feie efter dig og utrydde alle menn i Akabs hus, både myndige og umyndige i Israel,
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
22 og jeg vil gjøre med ditt hus som med Jeroboams, Nebats sønns hus og med Baesas, Akias sønns hus, fordi du har vakt min harme, og fordi du har fått Israel til å synde.
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
23 Også om Jesabel har Herren talt og har sagt: Hundene skal fortære Jesabel ved Jisre'els voll.
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
24 Den av Akabs hus som dør i byen, skal hundene fortære, og den som dør på marken, skal himmelens fugler fortære.
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
25 Det har aldri vært nogen som Akab, han som solgte sig til å gjøre hvad ondt var i Herrens øine, fordi hans hustru Jesabel egget ham.
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
26 Hans ferd var overmåte vederstyggelig; han fulgte de motbydelige avguder, aldeles som amorittene hadde gjort, de som Herren drev bort for Israels barn.
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
27 Men da Akab hørte hvad Elias sa, sønderrev han sine klær og la sekk om sitt legeme og fastet; og han sov i sekk og gikk stille omkring.
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
28 Da kom Herrens ord til tisbitten Elias, og det lød således:
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
29 Har du sett at Akab har ydmyket sig for mig? Fordi han har ydmyket sig for mig, vil jeg ikke la ulykken komme i hans dager, men i hans sønns dager vil jeg la ulykken komme over hans hus.
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

< 1 Kongebok 21 >