< 1 Bhakolinto 3 >

1 Bhakilishitu ajangunji, nne punaliji na mmanganya nangammeleketelanga mbuti bhandu bha mmbumu. Ikabheje mbuti bhandu bha pashilambolyo, malinga ashinambombe nndamo ja shi Kilishitu.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 Nashinkumpanganga mabhele, nngabha shalya shanonopa, pabha nkashilepelenje. Nkali nnaino nkashikombolanga.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 Numbe mmanganyanji launo nnakagulilanga indu ya pa shilambolyo. Pabha kungwenunji lushipagwa lupimililo na mpwai, bhuli mmanganya nngabha malinga bhandunji bha pa shilambolyo? Nnatamangana kwa kagulila nkubho gwa bhandunji bha pashilambolyo.
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 Mundu jumo munkumbi gwenunji pabheleketa kuti nne jwa a Pauli na juna kuti nne jwa a Apolo, bhuli, yeneyo ikalangula kuti nnatamangana malinga bhandu bha pa shilambolyo?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 A Apolo ni agani? Na a Pauli ni agani? Uwe bhatumishipe twampeleshelenje mmanganya ngulupai. Kila mundu munkumbi gwetu anatenda malinga shapegwilwe na Bhakulungwa.
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 Nne nashinkupanda mmbeju, a Apolo gubhajitilile mashi, ikabheje bhameshiye mmbeju a Nnungu.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 Kwa nneyo, jwa mmbone nngabha apandile mmbeju jula eu ajitilile mashi, ikabhe bha mmbone a Nnungu bhameshiye mmbeju.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Apandile jula eu ajitilile mashi bhowe bhanalingananga, ikabheje kila mundu shaposhele upo yakwe kwa liengo lyatendile.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 Pabha uwe na mmanganyanji, tubhowe tubhakamula liengo lya a Nnungu pamo, na mmanganya ni malinga nngunda gwabho na nyumba jabho.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 Kwa jangutilwa na nema jimbegwilwe na a Nnungu, malinga nkushenga akwete lunda, aolile nshingi gwa nyumba na mundu juna gwaishe shenga pa ntundu jakwe. Ikabheje kila mundu alolesheye shakuti shenga panani jakwe.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 Jwakwa mundu juna shaolele maimbo ga shenga, paolelwe pala, yani a Yeshu Kilishitu.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Ibhaga mundu shaashenje panani jakwe, kwa shaabhu eu maganga ga ela eu maganga ga bhei jikuklungwa, na juna shaashenjele nkali mikongo eu maamba eu manyai.
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 Ikabheje, lyubha lya ukumu liengo lya kila mundu shilibhoneshe mobha gushibhaishe a Kilishitu. Pabha, lyene lyubhalyo a Nnungu shibhapime kushimilika kwa kila liengo.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 Monaga shashenjile mundu shibhonekaga kulonjeya, bhai shaposhele upo.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 Ikabheje shashenjile mundu shitinikaga, bhai, akapegwa upo, ikabheje nnyene shatapulwe mbuti akolobhweshe pa moto.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Bhuli, nkakwimanyanga kuti mmanganya ni likanisha, na kuti Mbumu jwa a Nnungu anatama mmunda jenunji?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 Bhai, mundu aangabhanyaga likanisha lya a Nnungulyo, a Nnungu shibhanng'angabhanye jwene mundujo, pabha likanisha lya a Nnungu, ni lya Ukonjelo na lyene likanisha lya a Nnungulyo, ni mmanganyanji.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Nnaitembanje! Mundu jojowe munkumbi gwenunji aiganishiyaga kuti ashikola lunda malinga lwa pa shilambolyo, mbaya aiputuye nkupinga akole lunda lwa kweli. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 Pabha lunda lwa pa shilambolyo pano ni ungumba kwa a Nnungu. Na Majandiko ga Ukonjelo gakuti, “A Nnungu bhanakwaakamulanga bhakwetenje lunda, nkupenya kwabhonji.”
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 Kabhili Majandiko gakuti, “Bhakulungwa bhamumanyi ng'aniyo ya bhakwetenje lunda kuti ikapwaa.”
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Bhai mundu anaipunile bhandu. Pabha indu yowe yenunji.
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Ibhaga a Pauli, eu a Apolo, eu a Kepa, eu shilambolyo, eu gumi na kuwa, eu indu ipali, nnaino na ikwiya, yowe ni yenunji,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 ikabheje mmanganya ni bha a Kilishitu na bhalabho a Kilishitu ni bha a Nnungu.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Bhakolinto 3 >