+ Pirmā Mozus 1 >

1 Iesākumā Dievs radīja debesis un zemi.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 Un zeme bija tumša un tukša, un tumsa bija pār dziļumiem, un Dieva Gars lidinājās pa ūdeņu virsu.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 Un Dievs sacīja: Lai top gaisma. Tad tapa gaisma.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 Un Dievs redzēja gaismu labu esam. Un Dievs šķīra gaismu no tumsas.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 Un Dievs nosauca gaismu par dienu, un tumsu Viņš nosauca par nakti. Un tapa vakars un tapa rīts, pirmā diena.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 Tad Dievs sacīja: Lai top izplatījums ūdeņu starpā un lai tas šķir ūdeni no ūdens.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 Un Dievs darīja izplatījumu, un darīja starpu to ūdeni, kas izplatījuma apakšā, un to ūdeni, kas izplatījuma virsū; un tā notika.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 Un Dievs nosauca izplatījumu par debesi. Un tapa vakars un tapa rīts, otra diena.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 Tad Dievs sacīja: Lai ūdens debess apakšā krājās vienā vietā, ka sausums top redzams; un tā notika.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 Un Dievs nosauca sausumu par zemi, un to ūdeņu krājumu Viņš nosauca par jūru. Un Dievs redzēja to labu esam.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 Un Dievs sacīja: Lai zeme izdod zaļumu un zāli, kas savu sēklu nes, auglīgus kokus, kas augļus nes pēc savas kārtas, kam sava sēkla iekš sevis ir virs zemes; un tā notika.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 Un zeme izdeva zaļumu un zāli, kas savu sēklu nes pēc savas kārtas, un kokus, kas augļus nes, kam sava sēkla iekš sevis pēc savas kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 Un tapa vakars un tapa rīts, trešā diena.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 Tad Dievs sacīja: Lai top spīdekļi debess izplatījumā, kas šķir dienu no nakts un kas dod zīmes un laikus un dienas un gadus;
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 Un lai tie ir par spīdekļiem debess izplatījumā un spīd virs zemes; un tā notika.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 Un Dievs darīja divus lielus spīdekļus, lielāko spīdekli, dienu valdīt un mazāko spīdekli, naktī valdīt, - un zvaigznes.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 Un Dievs tos lika debess izplatījumā, lai tie spīd uz zemi.
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 Un valda dienu un nakti un šķir gaismu no tumsas. Un Dievs redzēja to labu esam.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 Un tapa vakars un tapa rīts, ceturtā diena.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 Tad Dievs sacīja: Lai pa pulkiem rodas ūdenī kustošas dzīvas dvašas un putni, kas virs zemes skrien apakš debess izplatījuma.
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 Un Dievs radīja lielus jūras zvērus un visādas dzīvas dvašas, kas lien, ko ūdens pa pulkiem izdod pēc viņu kārtām, un visādus spārnainus putnus pēc viņu kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 Un Dievs tos svētīja sacīdams: Vaislojaties un vairojaties un piepildiet ūdeni jūrā, un putni lai vairojās virs zemes.
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 Un tapa vakars un tapa rīts, piektā diena.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 Tad Dievs sacīja: Lai zeme izdod dzīvas dvašas pēc viņu kārtas, lopus, tārpus un zemes zvērus pēc viņu kārtas; un tā notika.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 Un Dievs darīja zemes zvērus pēc viņu kārtas un lopus pēc viņu kārtas un visādus zemes tārpus pēc viņu kārtas. Un Dievs redzēja to labu esam.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 Un Dievs sacīja: Darīsim cilvēkus pēc mūsu ģīmja, pēc mūsu līdzības, lai tie valda pār zivīm jūrā un pār putniem apakš debess un pār lopiem un pār visu zemi un pār visiem tārpiem, kas lien virs zemes.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 Un Dievs radīja cilvēku pēc Sava ģīmja, pēc Dieva ģīmja Viņš to radīja, un radīja tos, vīrieti un sievieti.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 Un Dievs tos svētīja, un Dievs uz tiem sacīja: Augļojaties un vairojaties un piepildiet zemi un pārvaldiet to un valdat pār zivīm jūrā un pār putniem apakš debess un pār visām dvašām, kas lien virs zemes.
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 Un Dievs sacīja: Redzi, Es jums esmu devis visādu zāli, kas nes sēklu, kas ir pa visu zemes virsu, un visus kokus, kam savi augļi iekš sevis un kas nes sēklu, jums par ēdamo.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 Un visiem zvēriem virs zemes un visiem putniem apakš debess un visiem tārpiem virs zemes, kam dzīva dvaša, esmu devis visādu zaļu zāli par barību. Un tā notika.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 Un Dievs uzlūkoja visu, ko Viņš bija darījis, un redzi, tas bija ļoti labs. Un tapa vakars un tapa rīts, sestā diena.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

+ Pirmā Mozus 1 >